< Efeserne 1 >

1 Paulus, Kristi Jesu Apostel ved Guds Villie, til de hellige, som ere i Efesus og ere troende i Kristus Jesus:
Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu. Kulembera oyera mtima a ku Efeso, okhulupirika mwa Khristu Yesu:
2 Naade være med eder og Fred fra Gud vor Fader og den Herre Jesus Kristus!
Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.
3 Lovet være Gud og vor Herres Jesu Kristi Fader, som har velsignet os med al aandelig Velsignelse i det himmelske i Kristus,
Tiyamike Mulungu, Atate a Ambuye athu Yesu Khristu, amene anatipatsa madalitso onse a uzimu kumwamba mwa Khristu.
4 ligesom han har udvalgt os i ham før Verdens Grundlæggelse til at være hellige og ulastelige for hans Aasyn,
Dziko lapansi lisanalengedwe, Mulungu anatisankhiratu mwa Khristu kuti tikhale oyera mtima ndi wopanda cholakwa pamaso pake. Mwa chikondi chake,
5 idet han i Kærlighed forudbestemte os til Sønneudkaarelse hos sig ved Jesus Kristus, efter sin Villies Velbehag,
Iye anakonzeratu kuti ife titengedwe ngati ana mwa Yesu Khristu, molingana ndi kukonda kwake ndi chifuniro chake.
6 til Pris for sin Naades Herlighed, som han benaadede os med i den elskede,
Anachita zimenezi kuti tiziyamika ulemerero wa chisomo chake, umene watipatsa kwaulere mwa Khristu amene amamukonda.
7 i hvem vi have Forløsningen ved hans Blod, Syndernes Forladelse, efter hans Naades Rigdom,
Mwa Yesu Khristu, chifukwa cha magazi ake, ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo athu molingana ndi kuchuluka kwa chisomo cha Mulungu
8 som han rigelig tildelte os i al Visdom og Forstand,
chimene anatipatsa mosawumira. Mwa nzeru zonse ndi chidziwitso,
9 idet han kundgjorde os sin Villies Hemmelighed, efter sin velbehagelige Beslutning, som han havde fattet hos sig selv,
Iye watiwululira chifuniro chake chimene chinali chobisika, chimene anachikonzeratu mwa Khristu, molingana ndi kukoma mtima kwake.
10 for at oprette en Husholdning i Tidernes Fylde, nemlig at sammenfatte sig alt i Kristus, det, som er i Himlene, og det, som er paa Jorden, i ham,
Chimene anakonza kuti chichitike nʼchakuti, ikakwana nthawi yake asonkhanitsa pamodzi mwa Khristu zinthu zonse za kumwamba ndi pa dziko lapansi.
11 i hvem vi ogsaa have faaet Arvelodden, forud bestemte efter hans Forsæt, der virker alt efter sin Villies Raad,
Iye anatisankhiratu mwa Khristu, atatikonzeratu molingana ndi machitidwe a Iye amene amachititsa zinthu zonse kuti zikwaniritse cholinga cha chifuniro chake,
12 for at vi skulde være til Pris for hans Herlighed, vi, som forud havde haabet paa Kristus,
nʼcholinga chakuti, ife amene tinali oyamba kukhala ndi chiyembekezo mwa Khristu, tiyamike ulemerero wake.
13 i hvem ogsaa I, da I hørte Sandhedens Ord, Evangeliet om eders Frelse, i hvem I ogsaa, da I bleve troende, bleve beseglede med Forjættelsens hellige Aand,
Ndipo inunso pamene munamva mawu a choonadi, Uthenga Wabwino wa chipulumutso chanu, munayikidwanso mwa Khristu. Mutakhulupirira, anakusindikizani chizindikiro pokupatsani Mzimu Woyera amene Iye analonjeza.
14 som er Pant paa vor Arv, til Ejendommens Forløsning, til Pris for hans Herlighed.
Mzimu Woyerayo ndi chikole chotsimikizira kuti tidzalandira madalitso athu, ndipo kuti Mulungu anatiwombola kuti tikhale anthu ake. Iye anachita zimenezi kuti timuyamike ndi kumulemekeza.
15 Derfor har ogsaa jeg, efter at have hørt om eders Tro paa den Herre Jesus og om eders Kærlighed til alle de hellige,
Choncho, kuyambira pamene ndinamva za chikhulupiriro chanu mwa Ambuye Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse,
16 ikke ophørt at takke for eder, idet jeg ihukommer eder i mine Bønner om,
ine sindilekeza kuyamika Mulungu chifukwa cha inu. Ndimakukumbukirani mʼmapemphero anga.
17 at vor Herres Jesu Kristi Gud, Herlighedens Fader, maa give eder Visdoms og Aabenbarelses Aand i Erkendelse af ham,
Ndimapemphera kuti Mulungu wa Ambuye athu Yesu Khristu, Atate a ulemerero akupatseni mzimu wa nzeru ndi wa vumbulutso, kuti mumudziwe kwenikweni.
18 gøre eders Hjertes Øjne oplyste til at kende, hvilket det Haab er, som han kaldte eder til, hvilken hans Arvs Herligheds Rigdom er iblandt de hellige,
Ndimapempheranso kuti maso a mitima yanu atsekuke ndi cholinga choti mudziwe chiyembekezo chimene Iye anakuyitanirani, chuma cha ulemerero chomwe chili mwa anthu oyera mtima.
19 og hvilken hans Krafts overvættes Storhed er over for os, som tro, alt efter hans Styrkes vældige Virkekraft,
Ndiponso ndikufuna kuti mudziwe mphamvu zake zazikulu koposa zimene zili mwa ife amene timakhulupirira. Mphamvuyi ndi yofanana ndi mphamvu yoposa ija
20 som han udviste paa Kristus, da han oprejste ham fra de døde og satte ham ved sin højre Haand i det himmelske,
imene inagwira ntchito pamene Mulungu anaukitsa Khristu kwa akufa, namukhazika Iye ku dzanja lake lamanja mʼdziko la kumwamba.
21 langt over al Magt og Myndighed og Kraft og Herredom og hvert Navn, som nævnes, ikke alene i denne Verden, men ogsaa i den kommende, (aiōn g165)
Anamukhazika pamwamba pa ulamuliro onse ndi mafumu, mphamvu ndi ufumu, ndiponso pamwamba pa dzina lililonse limene angalitchule, osati nthawi ino yokha komanso imene ikubwerayo. (aiōn g165)
22 og lagde alt under hans Fødder, og ham gav han som Hoved over alting til Menigheden,
Ndipo Mulungu anayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake ndi kumusankha Iyeyo kukhala mutu pa chilichonse chifukwa cha mpingo,
23 der er hans Legeme, fyldt af ham, som fylder alt i alle.
umene ndi thupi lake, chidzalo cha Iye amene adzaza chilichonse mu njira iliyonse.

< Efeserne 1 >