< Efeserne 3 >

1 Det er for denne Sags Skyld, at jeg, Paulus, Kristi Jesu Fange for eder, I Hedninger, —
Nʼchifukwa chake ine Paulo, ndili wamʼndende wa Khristu Yesu chifukwa cha inu anthu a mitundu ina.
2 om I da have hørt om Husholdningen med den Guds Naade, som blev given mig til eder,
Ndithudi, inu munamva za ntchito yachisomo cha Mulungu imene anandipatsa chifukwa cha inu,
3 at ved Aabenbarelse blev Hemmeligheden kundgjort mig, saaledes som jeg foran kortelig har skrevet,
ndicho chinsinsi chimene chinawululidwa kwa ine mwa vumbulutso, monga ndinakulemberani kale mwachidule.
4 hvoraf I, naar I læse det, kunne skønne min Indsigt i Kristi Hemmelighed,
Pamene mukuwerenga izi, inu mudzazindikira za chidziwitso changa pa chinsinsi cha Khristu,
5 som i andre Slægter ikke blev kundgjort for Menneskenes Børn, saaledes som den nu er bleven aabenbaret hans hellige Apostle og Profeter ved Aanden:
chimene sichinawululidwe kwa anthu amibado ina monga momwe tsopano chawululidwa ndi Mzimu wa Mulungu mwa atumwi oyera ndi aneneri.
6 Nemlig at Hedningerne ere Medarvinger og medindlemmede og meddelagtige i Forjættelsen i Kristus Jesus ved Evangeliet,
Chinsinsicho nʼchakuti, kudzera mu Uthenga Wabwino anthu a mitundu ina ndi olowamʼmalo pamodzi ndi Aisraeli, ndi ziwalo za thupi limodzi, ndi olandira nawo pamodzi malonjezo a mwa Khristu Yesu.
7 hvis Tjener jeg er bleven ifølge den Guds Naades Gave, som blev given mig ved hans Magts Virkekraft.
Mwachisomo cha Mulungu ndi mphamvu zake, ine ndinasanduka mtumiki wa Uthenga Wabwinowu.
8 Mig, den allerringeste af alle hellige, blev denne Naade given at forkynde Hedningerne Evangeliet om Kristi uransagelige Rigdom
Ngakhale ndili wamngʼono kwambiri pakati pa anthu onse a Mulungu, anandipatsa chisomo chimenechi cholalikira kwa anthu a mitundu ina chuma chopanda malire cha Khristu.
9 og at oplyse alle om, hvilken Husholdningen med den Hemmelighed er, som fra Evighed har været skjult i Gud, der skabte alle Ting, (aiōn g165)
Ndinasankhidwa kuti ndifotokoze momveka bwino kwa munthu aliyense za chinsinsi chimenechi, chinsinsi chimene kuyambira kale chinali chobisika mwa Mulungu amene analenga zinthu zonse. (aiōn g165)
10 for at Guds mangfoldige Visdom skulde nu ved Menigheden blive kundgjort for Magterne og Myndighederne i det himmelske,
Cholinga chake tsopano nʼchakuti, kudzera mwa mpingo, mafumu ndi a ulamuliro onse a kumwamba adziwe nzeru zochuluka za Mulungu.
11 efter det evige Forsæt, som han fuldbyrdede ved Kristus Jesus, vor Herre, (aiōn g165)
Chimenechi chinali chikonzero chamuyaya cha Mulungu, chimene chinachitika kudzera mwa Khristu Yesu Ambuye athu. (aiōn g165)
12 i hvem vi have Frimodigheden og Adgang med Tillid ved Troen paa ham.
Mwa Khristu ndi mwa chikhulupiriro chathu mwa Iye, timayandikira kwa Mulungu momasuka ndi molimbika mtima.
13 Derfor beder jeg, at I ikke tabe Modet over mine Trængsler, som jeg lider for eder, hvilket er en Ære for eder. —
Choncho, ine ndikukupemphani kuti musakhumudwe popeza ndikusautsidwa chifukwa cha inu pakuti masautso angawa ndi ulemerero wanu.
14 For denne Sags Skyld bøjer jeg mine Knæ for Faderen,
Nʼchifukwa chake ine ndikugwada pamaso pa Atate,
15 fra hvem enhver Faderlighed i Himle og paa Jord har sit Navn,
amene banja lililonse kumwamba ndi pa dziko lapansi limatchulidwa ndi dzina lawo.
16 at han vil give eder efter sin Herligheds Rigdom mægtigt at styrkes ved hans Aand i det indvortes Menneske;
Ndikupemphera kuti kuchokera mʼchuma cha ulemerero wake alimbikitse moyo wanu wa mʼkati ndi mphamvu za Mzimu wake,
17 at Kristus maa bo ved Troen i eders Hjerter,
kuti Khristu akhazikike mʼmitima mwanu mwachikhulupiriro. Ndipo ndikukupemphererani kuti muzikike ndi kukhazikika mʼchikondi
18 for at I, rodfæstede og grundfæstede i Kærlighed, kunne sammen med alle de hellige formaa at begribe, hvor stor Bredden og Længden og Dybden og Højden er,
kuti mukhale ndi mphamvu, kuti pamodzi ndi anthu oyera mtima onse muthe kuzindikira kupingasa, kutalika ndi kukwera komanso kuzama kwake kwa chikondi cha Khristu.
19 og at kende Kristi Kærlighed, som overgaar al Erkendelse, for at I kunne fyldes indtil hele Guds Fylde.
Ndikukupemphererani kuti mudziwe chikondi chija cha Khristu chopitirira nzeru za anthu, kuti mudzazidwe kwathunthu ndi moyo wa Mulungu mwini.
20 Men ham, som formaar over alle Ting at gøre langt ud over det, som vi bede eller forstaa, efter den Magt, som er virksom i os,
Tsopano kwa Iye amene angathe kuchita zochuluka kuposa zimene tingapemphe, kapena kuganiza molingana ndi mphamvu zake zimene zikugwira ntchito mwa ife,
21 ham være Ære i Menigheden og i Kristus Jesus igennem alle Slægterne i Evighedernes Evighed! Amen. (aiōn g165)
Iyeyo akhale ndi ulemu mu mpingo ndi mwa Khristu Yesu pa mibado yonse mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)

< Efeserne 3 >