< 5 Mosebog 12 >

1 Dette er de Anordninger og Lovbud, I omhyggeligt skal handle efter i det Land, HERREN, dine Fædres Gud, giver dig i Eje, saa længe I lever paa Jorden.
Awa ndi malangizo ndi malamulo amene muyenera kusamalitsanso kuti muwatsatire mʼdziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu wakupatsani kuti mutenge pa nthawi yonse imene muti mudzakhale mʼdzikomo.
2 I skal i Bund og Grund ødelægge alle de Steder, hvor de Folk, I driver bort, dyrker deres Guder, paa de høje Bjerge, paa Højene og under alle grønne Træer!
Muwonongeretu kwathunthu malo onse a pamwamba pa mapiri ataliatali ndi pa mapiri angʼonoangʼono ndi pansi pa mtengo uliwonse wotambalala pamene mitundu imene muyilande dzikolo ankapembedzerapo milungu yawo.
3 I skal nedbryde deres Altre og sønderslaa deres Stenstøtter, I skal opbrænde deres Asjerastøtter og omhugge deres Gudebilleder og udrydde deres Navn fra hvert saadant Sted.
Mugumule maguwa awo ansembe, ndi kuphwanya miyala yawo yachipembedzo ndipo mutenthe pa moto mafano awo a Asera: mugwetse mafano a milungu yawo ndi kufafaniza mayina awo mʼmalo amenewo.
4 I maa ikke bære eder saaledes ad over for HERREN eders Gud;
Musapembedze Yehova Mulungu wanu monga mmene amachitira iwowa.
5 men til det Sted, HERREN eders Gud udvælger blandt alle eders Stammer for at stedfæste sit Navn og lade det bo der, skal I søge, og der skal du gaa hen;
Koma inu muzifunafuna kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati pa mafuko anu kuti ayikeko dzina lake ndi kukhalako. Ku malo amenewa muyenera kupitako.
6 derhen skal I bringe eders Brændofre og Slagtofre, eders Tiender og Offerydelser, eders Løfteofre og Frivilligofre og de førstefødte af eders Hornkvæg og Smaakvæg;
Kumeneko muzipititsako zopereka zanu ndi nsembe zanu zopsereza, ndi chakhumi chanu ndi mphatso zapadera zimene munalonjeza kupereka ndi zopereka zanu zaufulu ndi ana oyamba a ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu.
7 der skal I holde Maaltid for HERREN eders Guds Aasyn og sammen med eders Husstand være glade over alt, hvad I erhverver, hvad HERREN din Gud velsigner dig med.
Kumeneko, pamaso pa Yehova Mulungu wanu, inu ndi mabanja anu mudzadya ndi kusangalalako pa china chilichonse chimene mudzakhudza, chifukwa Yehova Mulungu wanu wakudalitsani.
8 I maa ikke bære eder ad, som vi nu for Tiden gør her, hvor enhver gør, hvad han finder for godt;
Musadzachite monga tikuchitira lero lino, aliyense kumachita zimene akuona kuti ndi zoyenera,
9 thi endnu er I jo ikke kommet til det Hvilested og den Arvelod, HERREN din Gud vil give dig.
pakuti simunafike ku malo opumulirako ndi ku cholowa chimene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
10 Men naar I er gaaet over Jordan og har fæstet Bo i det Land, HERREN eders Gud vil give eder til Arv, og han faar skaffet eder Ro for alle eders Fjender trindt omkring, saa I kan bo trygt,
Koma mudzawoloka Yorodani ndi kukhazikika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, ndipo Iye adzakupatsani inu mpumulo ku adani anu okuzungulirani kuti mukhale motchinjirizidwa.
11 da skal det Sted, HERREN eders Gud udvælger til Bolig for sit Navn, være det, hvorhen I skal bringe alt, hvad jeg paalægger eder, eders Brændofre og Slagtofre, eders Tiender og Offerydelser og alle eders udvalgte Løfteofre, som I lover HERREN;
Tsono kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe kuti azikhalako muzikabweretsako chilichonse chimene ndikulamulirani inu: zopereka ndi nsembe zanu zopsereza, chakhumi chanu ndi mphatso zapadera, ndi chuma chanu chonse chosankhika chimene munalonjeza kwa Yehova.
12 og der skal I være glade for HERREN eders Guds Aasyn sammen med eders Sønner og Døtre, eders Trælle og Trælkvinder og Leviten inden eders Porte; thi han har jo ingen Arvelod og Del som I andre.
Ndipo kumeneko inu mukasangalale pamaso pa Yehova Mulungu wanu pamodzi ndi ana anu aamuna ndi ana anu aakazi, antchito anu aamuna ndi adzakazi anu, ndi Alevi a mʼmidzi yanu, amene alibe gawo kapena cholowa chawochawo.
13 Vogt dig for at ofre dine Brændofre paa et hvilket som helst Sted, dit Øje falder paa.
Musamalitse kuti musakaphere nsembe zanu zopsereza paliponse pamene mungafune.
14 Men paa det Sted HERREN udvælger i en af dine Stammer, der skal du ofre dine Brændofre, og der skal du gøre alt, hvad jeg paalægger dig.
Mukaphere pa malo okhawo amene Yehova adzawasankhe mwa limodzi la mafuko anu, ndipo kumeneko mukasunge chilichonse chimene ndikulamulireni.
15 Derimod maa du, saa meget du lyster, slagte Kvæg og nyde Kød rundt om i dine Byer, alt som HERREN din Gud velsigner dig; urene og rene maa spise det, som var det Gazeller eller Hjorte.
Koma mukhoza kumapha ziweto zanu mʼmizinda iliyonse ndi kudya nyama yake mmene mungafunire, ngati kuti ndi agwape kapena mbawala, monga mwadalitso limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. Woyeretsedwa ndi wosayeretsedwa akhoza kuyidya.
16 Kun Blodet maa I ikke nyde; det skal du lade løbe ud paa Jorden som Vand.
Koma musamadye magazi. Muziwathira pansi ngati madzi.
17 Men inden dine Porte maa du ikke nyde Tienden af dit Korn, din Most og din Olie eller de førstefødte af dit Hornkvæg og Smaakvæg eller noget af dine Løfteofre og Frivilligofre eller nogen af dine Offerydelser;
Musamadyere mʼmizinda yanu chakhumi cha tirigu wanu ndi vinyo watsopano ndi mafuta, kapena za ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu, kapena chilichonse chimene mwalonjeza kuchipereka, nsembe zanu zaufulu, kapena mphatso zapadera,
18 men for HERREN din Guds Aasyn, paa det Sted, HERREN din Gud udvælger, skal du nyde alt dette sammen med din Søn og Datter, din Træl og Trælkvinde og Leviten inden dine Porte, og du skal være glad for HERREN din Guds Aasyn over alt, hvad du erhverver dig.
mʼmalo mwake, muzidya pamaso pa Yehova Mulungu wanu, kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhira inu, ana anu aamuna ndi aakazi, antchito anu aamuna ndi adzakazi anu, ndi Alevi ochokera mʼmizinda yanu, ndipo mudzasangalale pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa chilichonse chimene mudzachikhudza.
19 Vogt dig vel for at glemme Leviten, saa længe du lever i dit Land!
Muonetsetse kuti musawataye Alevi pa masiku onse amene mukhale mʼdziko lanumo.
20 Naar HERREN din Gud udvider dine Landemærker, som han har lovet dig, og du da faar Lyst til Kød og siger: »Jeg vil have Kød at spise«, saa spis kun Kød, saa meget du lyster.
Yehova Mulungu wanu akadzakulitsa dziko lanu monga anakulonjezerani, ndipo mukapukwa nyama mumanena kuti, “Ndikufuna nyama,” pamenepo mudzadya mmene mungafunire.
21 Hvis det Sted, HERREN din Gud udvælger for der at stedfæste sit Navn, ligger langt fra dig, saa maa du slagte af dit Hornkvæg og Smaakvæg, som HERREN giver dig, saaledes som jeg har paalagt dig, og spise det inden dine Porte, saa meget du lyster.
Ngati malo amene Yehova Mulungu wanu awasankha kuti ayike Dzina lake ali kutali kwambiri ndi inu, mukhoza kupha ziweto pakati pa ngʼombe ndi nkhosa zimene Yehova wakupatsani, monga ndinakulamulani, ndipo mʼmizinda yanuyanu mukhoza kuzidya mmene mungafunire.
22 Men du skal spise det, som man spiser Gazeller og Hjorte; baade urene og rene maa spise det.
Muzidye ngati mukudya gwape kapena mbawala. Onse oyeretsedwa monga mwa mwambo ndi osayeretsedwa omwe akhoza kudya.
23 Kun maa du ufravigeligt afholde dig fra at nyde Blodet; thi Blodet er Sjælen, og du maa ikke nyde Sjælen tillige med Kødet.
Koma muonetsetse kuti musadye magazi, chifukwa magazi ndi moyo, ndipo musamadye moyo pamodzi ndi nyama.
24 Du maa ikke nyde det, men du skal lade det løbe ud paa Jorden som Vand.
Inu musamadye magazi, muziwathira pansi ngati madzi.
25 Afhold dig fra at nyde det, for at det kan gaa dig og dine Børn efter dig vel, idet du gør, hvad der er ret i HERRENS Øjne.
Musamadye magazi kuti zikuyendereni bwino inu pamodzi ndi ana anu a pambuyo panu, popeza mudzakhala mukuchita zoyenera pamaso pa Mulungu.
26 Men dine hellige Gaver og Løfteofre skal du komme med til det Sted, HERREN udvælger;
Koma mutenge zinthu zanu zoyeretsedwa ndi china chilichonse chimene munalumbira kupereka, ndi kupita kumalo kumene Yehova adzasankhe.
27 og du skal bringe dine Brændofre, baade Kødet og Blodet, paa HERREN din Guds Alter; og Blodet af dine Slagtofre skal udøses paa HERREN din Guds Alter, men Kødet maa du spise.
Mupereke nsembe zanu zopsereza pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu, nyama pamodzi ndi magazi omwe. Magazi a nsembe zanu athiridwe pambali pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu, koma nyamayo mukhoza kudya.
28 Adlyd omhyggeligt alle disse Bud, som jeg i Dag paalægger dig, for at det kan gaa dig og dine Børn efter dig vel til evig Tid, idet du gør, hvad der er godt og ret i HERREN din Guds Øjne.
Onetsetsani kuti muzimvera mawu onsewa amene ndikukupatsani kuti zinthu zizikuyenderani bwino nthawi zonse inu ndi ana anu chifukwa mudzakhala mukuchita zabwino ndi zoyenera pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
29 Naar HERREN din Gud udrydder de Folk, du drager hen at drive bort, og du har drevet dem bort og bosat dig i deres Land,
Yehova Mulungu wanu adzachotsa pamaso panu mitundu ya anthu amene mukufuna kuwathira nkhondo ndi kuwalanda dzikolo. Koma mukawapirikitsa ndi kukhazikika mʼdziko lawo,
30 saa vogt dig for at lade dig lokke til at gaa i deres Fodspor, efter at de er udryddet foran dig, og for at spørge dig for angaaende deres Guder, idet du siger: »Hvorledes plejede disse Folkeslag at dyrke deres Guder? Saaledes vil ogsaa jeg bære mig ad.«
ndipo pamene iwo awonongeka pamaso panu, samalirani kuti musakodwe mu msampha pa kufufuza za milungu yawo, nʼkumati, “Kodi anthu a mitunduwa amatumikira bwanji milungu yawo? Ifenso tichita momwemo.”
31 Saaledes maa du ikke bære dig ad over for HERREN din Gud; thi alt, hvad der er HERREN en Vederstyggelighed, alt, hvad han hader, har de gjort over for deres Guder; ja, de brændte endog deres Sønner og Døtre til Ære for deres Guder!
Musapembedze Yehova Mulungu wanu momwe amachitira iwowo, chifukwa popembedza milungu yawoyo amachita zonyansa zamitundumitundu zimene Yehova amadana nazo. Amatentha ngakhale ana awo aamuna ndi aakazi pa moto ngati nsembe za kwa milungu yawo.
32 Alt, hvad jeg paalægger eder, skal I omhyggeligt udføre. Du maa hverken lægge noget til eller trække noget fra.
Onetsetsani kuti mukuchita zimene ndikukulamulirani. Musawonjezerepo kapena kuchotserapo.

< 5 Mosebog 12 >