< Daniel 3 >

1 Kong Nebukadnezar lod lave en Billedstøtte af Guld, tresindstyve Alen høj og seks Alen bred, og han opstillede den paa Dalsletten Dura i Landsdelen Babel.
Mfumu Nebukadinezara anapangitsa fano la golide lotalika mamita 27 ndi mulifupi mwake mamita atatu, ndipo analiyimika mʼchigwa cha Dura mʼchigawo cha Babuloni.
2 Saa sendte Kong Nebukadnezar Bud for at sammenkalde Satraper, Landshøvdinger, Statholdere, Overdommere, Skatmestre, lovkyndige, Dommere og alle andre Embedsmænd i Landsdelen, at de skulde komme til Stede, naar Billedstøtten, som Kong Nebukadnezar havde ladet opstille, blev indviet.
Kenaka iye anayitanitsa akalonga, abwanamkubwa, nduna, aphungu, asungichuma, oweruza milandu, anyakwawa ndi akulu ena onse a madera a dzikolo, kuti abwere ku mwambo wotsekula fano limene analiyimika lija.
3 Da samledes Satraperne, Landshøvdingerne, Statholderne, Overdommerne, Skatmestrene, de lovkyndige, Dommerne og alle andre Embedsmænd i Landsdelen til Indvielsen af Billedstøtten, som Kong Nebukadnezar havde ladet opstille, og de stillede sig foran den.
Choncho akalonga, abwanamkubwa, nduna, aphungu, asungichuma, oweruza milandu, anyakwawa, ndi akulu ena onse a madera a dzikolo, anasonkhana kudzachita mwambo wotsekulira fano limene mfumu Nebukadinezara analiyimika, ndipo mlaliki anayimirira pamaso pa fanolo nati:
4 Saa raabte en Herold med høj Røst: »Det tilkendegives eder, I Folk, Stammer og Tungemaal:
“Inu anthu a mitundu yonse ndi a ziyankhulo zonse, mukulamulidwa kuti muchite izi: mitundu ya anthu ndi a chiyankhulo chilichonse
5 Naar I hører Horn, Fløjter, Citre, Harper, Hakkebrætter, Sækkepiber og alle Haande andre Instrumenter klinge, skal I falde ned og tilbede Guldbilledstøtten, som Kong Nebukadnezar har ladet opstille.
mukadzamva kulira kwa lipenga, chitoliro, zeze, sansi, chisakasa, mngoli ndi nyimbo za mtundu uliwonse, muyenera kulambira ndi kupembedza fano la golide limene mfumu Nebukadinezara analiyimika.
6 Og den, som ikke falder ned og tilbeder, skal øjeblikkelig kastes i den gloende Ovn.«
Aliyense amene sadzalambira ndi kupembedza adzaponyedwa nthawi yomweyo mʼngʼanjo ya moto.”
7 Saa snart alt Folket nu hørte Horn, Fløjter, Citre, Harper, Hakkebrætter og alle Haande andre Instrumenter klinge, faldt de derfor ned — alle Folk, Stammer og Tungemaal — og tilbad Guldbilledstøtten, som Kong Nebukadnezar havde ladet opstille.
Choncho anthu onse aja atangomva kulira kwa lipenga, chitoliro, zeze, sansi, chisakasa, mngoli ndi nyimbo za mtundu uliwonse, analambira ndi kupembedza fano la golide limene mfumu Nebukadinezara analiyimika.
8 Men ved samme Lejlighed traadte nogle kaldæiske Mænd frem og førte Klage mod Jøderne.
Pa nthawi imeneyi alawuli ena anafika ndi kuwanenera zoyipa Ayuda.
9 De tog til Orde og sagde til Kong Nebukadnezar: »Kongen leve evindelig!
Iwo anati kwa mfumu Nebukadinezara, “Inu mfumu mukhale ndi moyo wautali!
10 Du, o Konge, har paabudt, at enhver, naar han hører Horn, Fløjter, Citre, Harper, Hakkebrætter, Sækkepiber og alle Haande andre Instrumenter klinge, skal falde ned og tilbede Guldbilledstøtten,
Inu mfumu, mwakhazikitsa lamulo kuti aliyense akamva kulira kwa lipenga, chitoliro, zeze, sansi, chisakasa, mngoli ndi nyimbo za mtundu uliwonse, ayenera kulambira ndi kupembedza fano la golide,
11 og at den, som ikke gør det, skal kastes i den gloende Ovn.
ndi kuti aliyense osalambira ndi kupembedza adzaponyedwa mʼngʼanjo ya moto.
12 Men nu er her nogle jødiske Mænd, som du har overdraget at styre Landsdelen Babel, Sjadrak, Mesjak og Abed-Nego; disse Mænd ænser ikke dit Paabud, o Konge; de dyrker ikke din Gud og tilbeder ikke Guldbilledstøtten, som du har ladet opstille.«
Koma alipo Ayuda ena Sadirake, Mesaki ndi Abedinego amene munawayika kuti ayangʼanire ntchito ya dera la ku Babuloni. Anthu amenewa sakumvera inu mfumu. Iwo sakutumikira milungu yanu kapena kulambira fano la golide limene munaliyimikalo.”
13 Da lod Nebukadnezar i Vrede og Harme Sjadrak, Mesjak og Abed-Nego hente; og da Mændene var ført frem for Kongen,
Tsono Nebukadinezara anakwiya ndi kupsa mtima kwambiri, ndipo anayitanitsa Sadirake, Mesaki ndi Abedenego. Choncho amuna awa anabwera pamaso pa mfumu,
14 sagde Nebukadnezar til dem: »Er det oplagt Raad, Sjadrak, Mesjak og Abed-Nego, at I ikke dyrker min Gud eller tilbeder Guldbilledstøtten, som jeg har ladet opstille?
ndipo Nebukadinezara anawafunsa kuti, “Kodi ndi zoona, Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, kuti simukutumikira milungu yanga kapena kupembedza fano la golide ndinaliyikalo?
15 Nu vel, hvis I er rede til, naar I hører Horn, Fløjter, Citre, Harper, Hakkebrætter, Sækkepiber og alle Haande andre Instrumenter klinge, at falde ned og tilbede Billedstøtten, som jeg har ladet lave, saa er alt godt; men gør I det ikke, skal I paa Stedet kastes i den gloende Ovn. Og hvilken Gud er der, som da kan fri eder af mine Hænder?«
Tsopano ngati muli okonzeka kulambira ndi kupembedza fano ndinalipanga, mukangomva kulira kwa lipenga chitoliro, zeze, sansi, chisakasa, mngoli ndi nyimbo za mtundu uliwonse, muchita bwino. Koma ngati simulipembedza, mudzaponyedwa mʼnganjo ya moto. Nanga ndi mulungu uti amene adzatha kukupulumutsani mʼmanja anga?”
16 Sjadrak, Mesjak og Abed-Nego svarede Kong Nebukadnezar: »Det har vi ikke nødig at svare dig paa!
Sadirake, Mesaki ndi Abedenego anayankha mfumu Nebukadinezara kuti, “Sikoyenera kuti tikuyankheni pa nkhani imeneyi.
17 Sker det, saa kan vor Gud, som vi dyrker, fri os af den gloende Ovn, og han vil fri os af din Haand, o Konge;
Ngati tiponyedwa mʼngʼanjo ya moto, Mulungu amene timamutumikira akhoza kutipulumutsa ku ngʼanjo yamotoyo, ndipo adzatilanditsa mʼdzanja lanu mfumu.
18 men hvis ikke, saa maa du vide, o Konge, at din Gud dyrker vi dog ikke, og Guldbilledstøtten, som du har ladet opstille, tilbeder vi ikke!«
Koma ngakhale Mulungu wathu atapanda kutipulumutsa, tikufuna mudziwe inu mfumu, kuti sitidzatumikira milungu yanu kapena kupembedza fano la golide limene munaliyimika.”
19 Da opfyldtes Nebukadnezar af Harme, og hans Ansigtsudtryk ændredes over for Sjadrak, Mesjak og Abed-Nego; han tog til Orde og sagde, at Ovnen skulde gøres syv Gange hedere end ellers,
Pamenepo Nebukadinezara anapsa mtima ndi Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, ndipo anayipidwa nawo. Iye analamulira kuti ngʼanjo ayitenthetse kasanu ndi kawiri kuposa nthawi zonse,
20 og bød nogle haandfaste Mænd i sin Hær binde Sjadrak, Mesjak og Abed-Nego og kaste dem i den gloende Ovn.
ndipo analamula ena mwa asilikali amphamvu kwambiri mʼgulu lake lankhondo kuti amange Sadirake, Mesaki ndi Abedenego ndi kuwaponya mʼngʼanjo ya moto.
21 Saa blev Mændene bundet i deres Kapper, Underklæder, Huer og andre Klædningsstykker og kastet i den gloende Ovn.
Choncho amuna awa, atavala mikanjo yawo, mabuluku, nduwira ndi zovala zina zonse, anamangidwa ndi kuponyedwa mʼngʼanjo ya moto.
22 Og eftersom Kongens Bud var skarpt og Ovnen ophedet til Overmaal, brændte Luen de Mænd ihjel, som bragte Sjadrak, Mesjak og Abed-Nego op paa Ovnen,
Tsono popeza lamulo la mfumu linali lofulumiza, ngʼanjo inatenthetsedwa kowirikiza mwakuti malawi ake anapha asilikali amene ananyamula Sadirake, Mesaki ndi Abedenego,
23 medens de tre Mænd, Sjadrak, Mesjak og Abed-Nego, bundne faldt ned i den gloende Ovn.
ndipo anyamata atatuwa, ali chimangidwire, anagwera mʼngʼanjo ya moto.
24 Da sloges Kong Nebukadnezar af Rædsel og stod hastigt op; og han tog til Orde og spurgte sine Raadsherrer: »Var det ikke tre Mænd, vi kastede bundne i Ilden?« De svarede Kongen: »Jo, det var, Konge!«
Kenaka mfumu Nebukadinezara anadabwa ndipo anafunsa nduna zake kuti, “Kodi sanali amuna atatu amene anamangidwa ndi kuponyedwa mʼmoto?” Iwo anayankha kuti, “Ndi zoonadi, mfumu.”
25 Han sagde da videre: »Men jeg ser fire Mænd gaa frit om i Ilden, og de har ingen Skade taget; og den fjerde ser ud som en Gudesøn.«
Iye anati, “Taonani! Ndikuona amuna anayi akuyendayenda mʼmoto, osamangidwa ndi osapwetekedwa ndipo wachinayi akuoneka ngati mwana wa milungu.”
26 Derpaa traadte Nebukadnezar hen til den gloende Ovns Dør og raabte: »Sjadrak, Mesjak og Abed-Nego, I, den højeste Guds Tjenere, kom ud!« Da gik Sjadrak, Mesjak og Abed-Nego ud af Ilden.
Pamenepo Nebukadinezara anayandikira pa khomo langʼanjo ya moto ndi kufuwula kuti, “Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, atumiki a Mulungu Wammwambamwamba, tulukani! Bwerani kuno!” Ndipo Sadirake, Mesaki ndi Abedenego anatuluka mʼmoto,
27 Og Satraperne, Landshøvdingerne, Statholderne og Kongens Raadsherrer samlede sig og saa, at Ilden ikke havde haft nogen Magt over hine Mænds Legemer, at deres Hovedhaar ikke var svedet, at deres Kapper var uskadte, og at der ikke var Brandlugt ved dem.
ndipo akalonga, akazembe, abwanamkubwa ndi nduna zamfumu anasonkhana mowazungulira. Anaona kuti moto sunatenthe matupi awo ngakhale tsitsi kumutu kwawo silinapse; zovala zawo sizinapse, ndipo sankamveka fungo la moto.
28 Saa sagde Nebukadnezar: »Lovet være Sjadraks, Mesjaks og Abed-Negos Gud, der sendte sin Engel og friede sine Tjenere, som i Tillid til ham overtraadte Kongens Bud og hengav deres Legemer for at undgaa at dyrke eller tilbede nogen anden Gud end deres egen!
Kenaka Nebukadinezara anati, “Atamandike Mulungu wa Sadirake, Mesaki ndi Abedenego, amene anatumiza mngelo wake ndi kupulumutsa atumiki ake! Iwo anakhulupirira Iye ndi kunyozera lamulo la mfumu ndipo anali okonzeka kutaya moyo wawo koposa kutumikira kapena kupembedza mulungu wina aliyense wosakhala Mulungu wawo.
29 Hermed paabyder jeg, at den, der i noget Folk, nogen Stamme og noget Tungemaal siger noget ondt om Sjadraks, Mesjaks og Abed-Negos Gud, skal hugges sønder og sammen, og hans Hus skal gøres til en Skarndynge; thi der gives ingen anden Gud, som saaledes kan frelse.«
Tsono ndikulamula kuti anthu a mitundu ina kaya chiyankhulo china chili chonse amene anganyoze Mulungu wa Sadirake, Mesaki ndi Abedenego adulidwe nthulinthuli ndipo nyumba zawo ndidzagwetsa ndi kusandutsa bwinja, popeza palibe Mulungu amene akhoza kupulumutsa mʼnjira yotere.”
30 Og Kongen gengav Sjadrak, Mesjak og Abed-Nego deres Stillinger i Landsdelen Babel.
Ndipo mfumu Nebukadinezara anakweza pa ntchito Sadirake, Mesaki ndi Abedenego mʼchigawo cha Babuloni.

< Daniel 3 >