< 2 Samuel 24 >
1 Men HERRENS vrede blussede atter op mod Israel, saa at han æggede David mod dem og sagde: »Gaa hen og hold Mandtal over Israel og Juda!«
Nthawi inanso Yehova anawakwiyira Aisraeli ndipo anawutsa mtima wa Davide kuti awavutitse ndipo anati, “Pita kawerenge Aisraeli ndi Ayuda.”
2 Kongen sagde da til Joab og Hærførerne, der var hos ham: »Drag rundt i alle Israels Stammer fra Dan til Be'ersjeba og hold Mønstring over Folket, for at jeg kan faa Tallet paa det at vide!«
Choncho mfumu inati kwa Yowabu pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo amene anali nawo. “Pitani pakati pa mafuko onse a Israeli kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba kuti mukawerenge anthu omenya nkhondo ndi cholinga choti ndidziwe chiwerengero chawo.”
3 Men Joab svarede Kongen: »Maatte HERREN din Gud forøge Folket hundredfold, og maatte min Herre Kongen selv opleve det — men hvorfor har min Herre Kongen sat sig sligt for?«
Koma Yowabu anayankha mfumu kuti, “Yehova Mulungu wanu achulukitse ankhondo anu kukhala miyandamiyanda, ndipo alole inu mbuye wanga mfumu mudzazione zimenezi. Koma nʼchifukwa chiyani inu mbuye wanga mfumu mukufuna kuchita zimenezi?”
4 Men Joab og Hærførerne maatte bøje sig for Kongens Ord. Joab og Hærførerne forlod derfor Kongen for at holde Mønstring over Israels Folk.
Komabe mawu a mfumu anapambana mawu a Yowabu ndi atsogoleri a ankhondo. Choncho anachoka pamaso pa mfumu kupita kukawerenga anthu omenya nkhondo mu Israeli.
5 De gik over Jordan og begyndte ved Aroer og Byen, der ligger midt i Dalen; drog ad Gad til og i Retning af Ja'zer;
Atawoloka Yorodani, iwo anamanga misasa yawo pafupi ndi Aroeri kummwera kwa mzinda wa ku chigwa ndipo kenaka iwo anapita ku dziko la Gadi mpaka ku Yazeri.
6 saa kom de til Gilead og til Hetiternes Land hen imod Kadesj, derpaa til Dan, og fra Dan vendte de sig hen mod Zidon;
Iwo anapita ku Giliyadi ndi ku chigwa cha Tahitimu Hodisi ndipo anapitirira mpaka ku Dani Yaani ndi madera ozungulira Sidoni.
7 saa kom de til Fæstningen Tyrus og alle Hivviternes og Kana'anæernes Byer, hvorfra de gik til Be'ersjeba i det judæiske Sydland.
Kenaka iwo anapita molunjika linga la ku Turo ndi ku mizinda yonse ya Ahivi ndi Akanaani. Pomaliza anapita ku Beeriseba ku Negevi wa ku Yuda.
8 Efter at de var draget hele Landet rundt i ni Maaneder og tyve Dage, kom de tilbage til Jerusalem.
Atayendayenda mʼdziko lonse anabwerera ku Yerusalemu patapita miyezi isanu ndi inayi ndi masiku makumi awiri.
9 Joab opgav derpaa Kongen Tallet, der var fundet ved Folketællingen, og Israel talte 800 000 kraftige, vaabenføre Mænd, Juda 500 000 Mænd.
Yowabu anapereka chiwerengero cha anthu ankhondo kwa mfumu: Mu Israeli munali anthu 800,000 amphamvu amene amadziwa kugwiritsa ntchito lupanga ndipo mu Yuda munali anthu 500,000.
10 Men efter at David havde holdt Mandtal over Folket, slog Samvittigheden ham, og han sagde til HERREN: »Jeg har syndet svarlig i, hvad jeg har gjort! Men tilgiv nu, HERRE, din Tjeners Brøde, thi jeg har handlet som en stor Daare!«
Davide anatsutsika mu mtima mwake atatha kuwerenga anthuwo ndipo anapemphera kwa Yehova kuti, “Ine ndachimwa kwambiri pa zimene ndachita. Tsono Yehova, ndikupempha kuti mukhululuke kulakwa kwa mtumiki wanu. Ine ndachita zopusa kwambiri.”
11 Da David stod op om Morgenen kom HERRENS Ord til Profeten Gad, Davids Seer, saaledes:
Davide asanadzuke mmawa mwake mawu a Yehova anafika kwa mneneri Gadi, mlosi wa Davide kuti,
12 »Gaa hen og sig til David: Saa siger HERREN; Jeg forelægger dig tre Ting; vælg selv, hvilken jeg skal lade times dig!«
“Pita ukamuwuze Davide kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikukupatsa zinthu zitatu izi. Usankhepo chimodzi pa zimenezi choti ndikuchitire.’”
13 Gad kom da til David og kundgjorde ham det og sagde: »Skal der komme tre Hungersnødsaar over dig i dit Land, eller vil du i tre Maaneder jages paa Flugt, forfulgt af din Fjende, eller skal der komme tre Dages Pest i dit Land? Overvej nu, hvad jeg skal svare ham, der har sendt mig!«
Choncho Gadi anapita kwa Davide ndipo anati kwa iye, “Kodi mungakonde kuti mʼdziko mwanu mukhale njala kwa zaka zitatu? Kapena kuti mukhale mukuthawa adani anu kwa miyezi itatu? Kapena kuti mʼdziko muno mukhale mliri kwa masiku atatu? Tsopano, ganizirani bwino ndipo musankhe chomwe mudzamuyankhe amene wandituma.”
14 David svarede Gad: »Jeg er i saare stor Vaande — lad os saa falde i HERRENS Haand, thi hans Barmhjertighed er stor; i Menneskehaand vil jeg ikke falde!«
Davide anati kwa Gadi, “Ine ndavutika kwambiri mu mtima mwanga. Ife atilange ndi Yehova pakuti chifundo chake ndi chachikulu, koma ndisalangidwe ndi anthu.”
15 Saa valgte David da Pesten. Ved Hvedehøstens Tid begyndte Soten at ramme Folket; og der døde 70 000 Mand af Folket fra Dan til Be'ersjeba.
Choncho Yehova anabweretsa mliri pa Aisraeli, kuyambira mmawa mpaka pa nthawi imene anafuna mwini wake, ndipo unapha anthu 70,000 kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba.
16 Da Engelen udrakte sin Haand mod Jerusalem for at ødelægge det, angrede HERREN det onde, og han sagde til Engelen, som ødelagde Folket »Nu er det nok, drag din Haand tilbage!« HERRENS Engel var da ved Jebusiten Aravnas Tærskeplads.
Pamene mngelo anatambasula dzanja lake kuti awononge Yerusalemu, Yehova anamva chisoni chifukwa cha zowawazo ndipo anati kwa mngelo amene ankawononga anthu uja, “Basi kwakwanira! Leka kuwononga.” Nthawi imeneyo mngelo wa Yehova anali atayima pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.
17 Men da David saa Engelen, som slog Folket, sagde han til HERREN: »Det er mig, der har syndet, mig, der har begaaet Brøden; men Faarene der, hvad har de gjort? Lad din Haand dog ramme mig og mit Fædrenehus!«
Davide ataona mngelo amene ankakantha anthu uja, anati kwa Yehova, “Ine ndi amene ndachimwa. Ine mʼbusa ndiye ndachita zoyipa. Anthuwa ali ngati nkhosa zosalakwa. Kodi iwowa achita chiyani? Langani ineyo pamodzi ndi banja langa.”
18 Samme Dag kom Gad til David og sagde: »Gaa op og rejs HERREN et Alter paa Jebusiten Aravnas Tærskeplads!«
Tsiku limenelo Gadi anapita kwa Davide ndi kukanena kuti, “Pitani kamangeni guwa lansembe la Yehova pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.”
19 Og David gik derop efter Gads Ord, saaledes som HERREN havde paabudt.
Ndipo Davide anapita monga momwe Yehova anamulamulira kudzera mwa Gadi.
20 Da Aravna, der var ved at tærske Hvede, saa ned og fik Øje paa Kongen og hans Folk, som kom hen imod ham, gik han ud og kastede sig paa sit Ansigt til Jorden for ham;
Arauna atayangʼana ndi kuona mfumu ndi anthu ake akubwera kumene kunali iye, iyeyo anatuluka ndi kuwerama pamaso pa mfumu mpaka nkhope yake kugunda pansi.
21 og Aravna sagde: »Hvorfor kommer min Herre Kongen til sin Træl?« David svarede: »For at købe Tærskepladsen af dig og bygge HERREN et Alter, at Folket maa blive friet fra Plagen!«
Arauna anati, “Nʼchifukwa chiyani mbuye wanga mfumu mwabwera kwa mtumiki wanu?” Davide anayankha kuti, “Kudzagula malo ako opunthira tirigu kuti ndimangire Yehova guwa lansembe kuti mliri uli pa anthuwa usiye.”
22 Da sagde Aravna til David: »Min Herre Kongen tage den og ofre, hvad ham tykkes ret! Her er Okserne til Brændoffer og Tærskeslæderne og Oksernes Stavtøj til Brændsel!
Arauna anati kwa Davide, “Mbuye wanga mfumu mutenge chilichonse chimene chikukondweretseni ndi kuchipereka nsembe. Nazi ngʼombe zazimuna za nsembe yopsereza, nazi zopunthira tirigu ndi magoli angʼombe kuti zikhale nkhuni.
23 Min Herre Kongens Træl giver Kongen det hele!« Og Aravna sagde til Kongen: »Maatte HERREN din Gud have Behag i dig!«
Inu mfumu, Arauna akupereka zonsezi kwa inu mfumu.” Arauna anatinso kwa iye, “Yehova Mulungu wanu akuvomerezeni.”
24 Men Kongen svarede Aravna: »Nej, jeg vil købe det af dig for dets fulde Værdi; jeg vil ikke bringe HERREN min Gud Brændofre, som intet koster mig!« Saa købte David Tærskepladsen og Okserne for halvtredsindstyve Sølvsekel;
Koma mfumu inayankha Arauna kuti, “Ayi, Ine ndikunenetsa kuti ndikulipira. Sindidzapereka kwa Yehova Mulungu wanga nsembe yopsereza imene sindinavutikire.” Kotero Davide anagula malo wopunthira tiriguwo ndi ngʼombe ndipo anapereka kwa Araunayo masekeli asiliva makumi asanu.
25 og David byggede HERREN et Alter der og ofrede Brændofre og Takofre. Da forbarmede HERREN sig over Landet, og Israel blev friet fra Plagen.
Davide anamanga guwa lansembe la Yehova pamenepo ndipo anaperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Ndipo Yehova anayankha pempherolo mʼmalo mwa dziko lonse, ndipo mliri unatha pa Aisraeli.