< 2 Samuel 18 >

1 Derpaa holdt David Mønstring over sit Mandskab og satte Tusindførere og Hundredførere over dem;
Davide anasonkhanitsa anthu amene anali naye ndipo anasankha atsogoleri ena olamulira ankhondo 1,000 ndi ena olamulira ankhondo 100.
2 og David delte Mandskabet i tre Dele; den ene Tredjedel stillede han under Joab, den anden under Abisjaj, Zerujas Søn og Joabs Broder, og den sidste Tredjedel under Gatiten Ittaj. Kongen sagde saa til Folkene: »Jeg vil selv drage med i Kampen!«
Davide anatumiza asilikaliwo atawagawa patatu: gulu loyamba limalamulidwa ndi Yowabu, gulu lachiwiri limalamulidwa ndi Abisai ndipo gulu lachitatu limalamulidwa ndi Itai Mgiti. Mfumu inawuza asilikaliwo kuti, “Inenso ndipita nanu ndithu.”
3 Men de svarede: »Du maa ikke drage med; thi om vi flygter, ænser man ikke os; ja, selv om Halvdelen af os falder, ænser man ikke os, men du gælder lige saa meget som ti Tusinde af os; derfor er det bedst, at du holder dig rede til at ile os til Hjælp fra Byen.«
Koma anthuwo anati, “Inu musapite nafe. Ngati tidzathamangitsidwa, iwowo sadzasamala za ife. Ngakhale theka la ife litafa, iwo sadzasamalako. Koma inuyo ndinu ofunika kuposa asilikali 10,000. Nʼkwabwino kwambiri kuti inu muzititumizira chithandizo kuchokera ku mzindako.”
4 Kongen svarede: »Jeg gør, hvad I finder bedst!« Derpaa stillede Kongen sig ved Porten, medens hele Mandskabet drog ud, hundredvis og tusindvis.
Mfumu inayankha kuti, “Ine ndichita chimene chili chokukomerani.” Kotero mfumu inayima pambali pa chipata pamene ankhondo onse amayenda mʼmagulu a anthu 100 ndi a 1,000.
5 Men Kongen gav Joab, Abisjaj og Ittaj den Befaling: »Far nu lempeligt med den unge Absalom!« Og hele Mandskabet hørte, hvorledes Kongen gav alle Øversterne Befaling om Absalom.
Mfumu inalamulira Yowabu, Abisai ndi Itai kuti, “Mumukomere mtima Abisalomu chifukwa cha ine.” Ndipo asilikali onse anamva pamene mfumu imalamula izi za Abisalomu kwa wolamulira aliyense.
6 Derpaa rykkede Krigerne i Marken mod Israel, og Slaget kom til at staa i Efraims Skov.
Ankhondo anayenda kupita kukachita nkhondo ndi Israeli, ndipo nkhondo inachitika mʼnkhalango ya Efereimu.
7 Der blev Israels Hær slaaet af Davids Folk, og der fandt et stort Mandefald Sted den Dag; der faldt 200 000 Mand.
Aisraeli anagonjetsedwa kumeneko ndi ankhondo a Davide. Tsiku limenelo anaphedwa anthu okwanira 20,000.
8 Kampen bredte sig over hele Egnen, og Skoven fortærede den Dag flere Folk end Sværdet.
Nkhondo inafalikira ku madera onse akumidzi ndipo anthu akufa chifukwa cha zoopsa za mʼnkhalango anali ambiri tsiku limenelo kuposa akufa ndi lupanga.
9 Absalom selv stødte paa nogle af Davids Folk; Absalom red paa sit Muldyr, og da Muldyret kom ind under en stor Terebintes tætte Grene, blev hans Hoved hængende i Terebinten, saa han hang mellem Himmel og Jord, medens Muldyret, han sad paa, løb bort.
Tsono zinachitika kuti Abisalomu anakumana ndi asilikali a Davide. Iye anali atakwera bulu ndipo pamene buluyo amadutsa pansi pa nthambi zambiri za mtengo wa thundu, mutu wa Abisalomu unakodwa mu mtengomo. Iye anasiyidwa atatsakamira mʼmalele, pamene bulu amene anakwerapoyo amapitirira.
10 En Mand, der saa det meldte det til Joab og sagde: »Jeg saa Absalom hænge i en Terebinte.«
Mmodzi mwa asilikali ataona zimenezi, anamuwuza Yowabu kuti, “Ine ndamuona Abisalomu ali lende mu mtengo wa thundu.”
11 Da sagde Joab til Manden, der havde meldt ham det: »Naar du saa det, hvorfor slog du ham da ikke til Jorden med det samme? Saa havde jeg givet dig ti Sekel Sølv og et Bælte!«
Yowabu anati kwa munthu amene anamuwuza zimenezi, “Ukuti chiyani! Unamuona? Nʼchifukwa chiyani sunamukanthire pansi pomwepo? Ndipo ine ndikanakupatsa ndalama za siliva khumi ndi lamba wausilikali.”
12 Men Manden svarede Joab: »Om jeg saa havde faaet tilvejet tusind Sekel, havde jeg ikke lagt Haand paa Kongens Søn; thi vi hørte jo selv, hvorledes Kongen bød dig, Abisjaj og Ittaj: Vogt vel paa den unge Absalom!
Koma munthuyo anayankha kuti, “Ngakhale atandipatsa mʼmanja mwanga ndalama zasiliva 1,000, sindingatambasule dzanja langa kupha mwana wa mfumu. Ife tikumva, mfumu inalamula inu Abisai ndiponso Itai kuti, ‘Mutetezeni mnyamatayo Abisalomu chifukwa cha ine!’
13 Dersom jeg havde handlet svigefuldt imod ham — intet bliver jo skjult for Kongen — vilde du have ladet mig i Stikken!«
Ndipo sindikanayika moyo wanga pa chiswe pakuti palibe chimene chimabisika pamaso pa mfumu komanso inu simukanditeteza.”
14 Da sagde Joab: »Saa gør jeg det for dig!« Dermed greb han tre Spyd og stødte dem i Brystet paa Absalom, som endnu levede og hang mellem Terebintens Grene.
Yowabu anati, “Ine sinditayanso nthawi ndi iwe.” Ndipo anatenga mikondo itatu mʼmanja mwake ndipo anabaya pamtima pa Abisalomu, Abisalomuyo akanali ndi moyo pa mtengo wa thundu.
15 Derpaa traadte ti unge Mænd, der var Joabs Vaabendragere, til og gav Absalom Dødsstødet.
Ndipo anthu khumi onyamula zida za Yowabu anazungulira Abisalomu, kumubaya ndi kumupha.
16 Joab lod nu støde i Hornet, og Hæren opgav at forfølge Israel, thi Joab bød Folkene standse.
Kenaka Yowabu analiza lipenga ndipo asilikali analeka kuthamangitsa Israeli pakuti Yowabu anawaletsa.
17 Derpaa tog de og kastede Absalom i en stor Grube i Skoven og ophobede en mægtig Stendynge over ham. Og hele Israel flygtede hver til sit.
Iwo anatenga Abisalomu ndi kumuponya mʼdzenje lalikulu mʼchipululumo ndipo anawunjikapo miyala ikuluikulu. Nthawiyi Aisraeli onse anathawa kupita ku nyumba zawo.
18 Men medens Absalom endnu levede, havde han taget og rejst sig den Stenstøtte, som staar i Kongedalen; thi han sagde: »Jeg har ingen Søn til at bevare Mindet om mit Navn.« Han havde opkaldt Stenstøtten efter sig selv, og endnu den Dag i Dag kaldes den »Absaloms Minde«.
Abisalomu ali ndi moyo anadzimangira chipilala mʼchigwa cha mfumu, pakuti ankaganiza kuti, “Ine ndilibe mwana wamwamuna amene adzakhale chikumbutso changa.” Chipilalacho anachitchula dzina lake lomwe ndipo mpaka lero chimatchedwa chipilala cha Abisalomu.
19 Da sagde Ahima'az, Zadoks Søn: »Lad mig løbe hen og bringe Kongen den gode Tidende, at HERREN har skaffet ham Ret over for hans Fjender!«
Tsono Ahimaazi mwana wa Zadoki anati, “Ndiloleni ndithamange ndi kukapereka uthenga kwa mfumu kuti Yehova wayipulumutsa mʼdzanja la adani ake.”
20 Men Joab svarede ham: »Du skal ikke være den, der bringer Bud i Dag; en anden Gang kan du bringe Bud, men i Dag skal du ikke gøre det, da Kongens Søn er død!«
Yowabu anamuwuza iye kuti, “Iwe si amene uti ukanene zimenezi lero. Ukapereka uthenga nthawi ina, koma usatero lero, chifukwa mwana wa mfumu wafa.”
21 Og Joab sagde til Etiopieren: »Gaa du hen og meld Kongen, hvad du har set!« Da kastede Etiopieren sig til Jorden for Joab og ilede af Sted.
Kenaka Yowabu anawuza Mkusi kuti, “Pita ukawuze mfumu zimene waona.” Mkusiyo anawerama pamaso pa Yowabu ndipo anathamanga kupita.
22 Men Ahima'az, Zadoks Søn, sagde atter til Joab: »Ske, hvad der vil! Lad ogsaa mig løbe bag efter Etiopieren!« Da sagde Joab: »Hvorfor vil du det, min Søn? For dig er der ingen Budløn at hente!«
Ahimaazi mwana wa Zadoki ananenanso kwa Yowabu kuti, “Zivute zitani, chonde mundilole kuti ndipite pambuyo pa Mkusiyo.” Koma Yowabu anayankha kuti, “Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukufuna kupita? Ulibe nkhani yoti ukalandire nayo mphotho.”
23 Men han blev ved: »Ske, hvad der vil! Jeg løber!« Saa sagde han: »Løb da!« Og Ahima'az løb ad Vejen gennem Jordanegnen og naaede frem før Etiopieren.
Iye anati, “Zivute zitani ine ndikufuna kuti ndipite.” Choncho Yowabu anati “Pita!” Ndipo Ahimaazi anathamanga kudzera njira ya ku chigwa ndipo anamupitirira Mkusi uja.
24 David sad just mellem de to Porte, og Vægteren steg op paa Porttaget ved Muren; da han saa ud, se, da kom en Mand løbende alene.
Nthawi imeneyo nʼkuti Davide atakhala pakati pa zipata ziwiri, chakubwalo ndi chamʼkati. Mlonda anakwera pa khoma nakayimirira pa denga la chipata. Anati atayangʼana, anaona munthu akuthamanga yekhayekha.
25 Vægteren raabte og meldte det til Kongen, og Kongen sagde: »Er han alene, har han Bud at bringe!« Men medens Manden fortsatte sit Løb og kom nærmere,
Mlonda uja anapita kwa mfumu ndipo anafotokoza. Mfumu inati, “Ngati ali yekha ali ndi nkhani yabwino” Ndipo munthuyo anayandikira.
26 saa Vægteren en anden Mand komme løbende og raabte ned i Porten: »Der kommer een Mand til løbende alene!« Kongen sagde: »Ogsaa han har Bud at bringe!«
Mlonda uja anaonanso munthu wina akuthamanga, ndipo anayitana woyangʼanira pa chipata, “Taona, munthu winanso akuthamanga ali yekha!” Mfumu inati, “Iye akubweretsanso nkhani yabwino.”
27 Da raabte Vægteren: »Den forreste løber saaledes, at det ser ud til at være Ahima'az, Zadoks Søn!« Kongen sagde: »Det er en god Mand, han kommer med godt Bud!«
Mlonda uja anati, “Munthu akuthamanga patsogoloyo, kathamangidwe kake kakufanafana ndi mmene amathamangira Ahimaazi, mwana wa Zadoki.” Mfumu inati, “Ameneyo ndi munthu wabwino, ndipo akubwera ndi nkhani yabwino.”
28 Imidlertid var Ahima'az kommet nærmere og raabte til Kongen: »Hil dig!« Saa kastede han sig ned paa Jorden for Kongen og sagde: »Lovet være HERREN din Gud, som gav dem, der løftede Haand mod min Herre Kongen, i din Haand!«
Ndipo Ahimaazi anafuwula kwa mfumu, “Zonse zili bwino!” Iye anagwada pamaso pa mfumu nkhope yake atagunditsa pansi ndipo anati, “Yehova Mulungu wathu alemekezedwe! Iye wapereka mʼdzanja lathu anthu amene anawukira inu mbuye wanga mfumu.”
29 Kongen spurgte: »Er den unge Absalom uskadt?« Ahima'az svarede: »Jeg saa, at der var stor Tummel, da Kongens Træl Joab sendte din Træl af Sted, men jeg ved ikke, hvad det var.«
Mfumu inafunsa, “Kodi mnyamata uja Abisalomu watetezedwa?” Ahimaazi anayankha, “Pamene Yowabu amati azindituma ine mtumiki wanu ndinaona chipiringu cha anthu, koma sindikudziwa chinali chiyani.”
30 Kongen sagde da: »Træd til Side og stil dig der!« Og han traadte til Side og blev staaende.
Mfumu inati, “Ima apo ndipo udikire.” Kotero iye anapita pa mbali nayima pamenepo.
31 I det samme kom Etiopieren; og Etiopieren sagde: »Der er Bud til min Herre Kongen: HERREN har i Dag skaffet dig Ret over for alle dine Modstandere!«
Kenaka Mkusi uja anafika ndipo anati, “Mbuye wanga mfumu imvani nkhani yabwino! Yehova wakupulumutsani inu lero kwa onse amene anakuwukirani.”
32 Kongen spurgte Etiopieren: »Er den unge Absalom uskadt?« Og han svarede: »Det gaa min Herre Kongens Fjender og alle dine Modstandere som den unge Mand!«
Mfumu inafunsa Mkusiyo kuti, “Kodi mnyamata uja Abisalomu watetezedwa?” Mkusiyo anayankha kuti, “Adani anu mbuye wanga mfumu, pamodzi ndi anthu onse amene amakuwukirani, ziwaonekere zomwe zamuonekera mnyamatayo.”
33 Da blev Kongen dybt rystet, og han gik op i Stuen paa Taget over Porten og græd; og han gik frem og tilbage og klagede: »Min Søn Absalom, min Søn, min Søn Absalom! Var jeg blot død i dit Sted! Absalom, min Søn, min Søn!«
Mfumu inanthunthumira. Inapita ku chipinda cha mmwamba cha pa chipata kukalira. Pamene imapita, inkati: “Iwe mwana wanga Abisalomu! Mwana wanga! Mwana wanga Abisalomu! Zikanakhala bwino ndikanafa ndine mʼmalo mwako! Iwe Abisalomu, mwana wanga, mwana wanga!”

< 2 Samuel 18 >