< 2 Samuel 12 >

1 Og HERREN sendte Natan til David. Da han kom ind til ham, sagde han: »Der boede to Mænd i samme By, en rig og en fattig.
Tsono Yehova anatumiza Natani kwa Davide. Atafika kwa Davide anati, “Panali anthu awiri mʼmizinda ina, wina wolemera ndi wina wosauka.
2 Den rige havde Smaakvæg og Hornkvæg i Mængde,
Munthu wolemerayo anali ndi nkhosa ndi ngʼombe zambiri,
3 medens den fattige ikke ejede andet end et eneste lille Lam, som han havde købt og opdrættet, og som var vokset op hos ham sammen med hans Børn; det aad af hans Brød, drak af hans Bæger og laa i hans Skød og var ham som en Datter.
koma wosaukayo analibe chilichonse kupatula kankhosa kamodzi kakakazi kamene anakagula. Iye anakasunga ndipo kanakula naye pamodzi ndi ana ake. Kamadya chakudya chake, kamamwera chikho chake ndipo kamagona mʼmanja mwake. Kanali ngati mwana wamkazi kwa iyeyo.
4 Men da den rige Mand engang fik Besøg, ømmede han sig ved at tage noget af sit eget Smaakvæg eller Hornkvæg og tillave det til den vejfarende Mand, som var kommet til ham, men tog den fattige Mands Lam og tillavede det til sin Gæst!«
“Ndipo mlendo anafika kwa munthu wolemera uja, koma munthu wolemerayo sanafune kutenga imodzi mwa nkhosa kapena ngʼombe zake kuti akonzere chakudya mlendo amene anafika kwa iye. Mʼmalo mwake anatenga mwana wankhosa wamkazi wa munthu wosauka uja nakonzera chakudya mlendo uja amene anabwera kwa iye.”
5 Da blussede Davids Vrede heftigt op mod den Mand, og han sagde til Natan: »Saa sandt HERREN lever: Den Mand, som gjorde det, er dødsens,
Davide anapsa mtima kwambiri chifukwa cha munthuyo ndipo anati kwa Natani, “Pali Yehova, munthu amene anachita zimenezi ayenera kufa basi!
6 og Lammet skal han erstatte firefold, fordi han handlede saa hjerteløst!«
Iye ayenera kulipira mwana wankhosa wamkaziyo kanayi, chifukwa anachita chinthu chimenechi ndipo analibe chifundo.”
7 Men Natan sagde til David: »Du er Manden! Saa siger HERREN, Israels Gud: Jeg salvede dig til Konge over Israel, og jeg friede dig af Sauls Haand;
Kenaka Natani anati kwa Davide, “Munthuyo ndinu! Yehova, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakudzoza kukhala mfumu ya Israeli, ndipo ndinakupulumutsa mʼdzanja la Sauli.
8 jeg gav dig din Herres Hus, lagde din Herres Hustruer i din Favn og gav dig Israels og Judas Hus; og var det for lidet, vilde jeg have givet dig endnu mere, baade det ene og det andet.
Ndinakupatsanso banja la mbuye wako ndiponso akazi a mbuye wako mʼmanja mwako. Ine ndinakupatsanso banja la Israeli ndi Yuda. Ndipo ngati zinthu zonse izi zinali zochepa, Ine ndikanakupatsa zambiri.
9 Hvorfor har du da ringeagtet HERRENS Ord og gjort, hvad der er ondt i hans Øjne? Hetiten Urias har du dræbt med Sværdet; hans Hustru har du taget til Ægte, og ham har du slaaet ihjel med Ammoniternes Sværd.
Nʼchifukwa chiyani unanyoza mawu a Yehova pochita chimene chili choyipa pamaso pake? Iwe unakantha Uriya Mhiti ndi lupanga ndipo unatenga mkazi wake kukhala wako. Uriyayo unamupha ndi lupanga la Aamoni.
10 Saa skal nu Sværdet aldrig vige fra dit Hus, fordi du ringeagtede mig og tog Hetiten Urias's Hustru til Ægte.
Ndipo tsopano lupanga silidzachoka pa nyumba yako, chifukwa unandinyoza ine ndi kutenga mkazi wa Uriya Mhiti kukhala wako.’
11 Saa siger HERREN: Se, jeg lader Ulykke komme over dig fra dit eget Hus, og jeg tager dine Hustruer bort for Øjnene af dig og giver dem til en anden, som skal ligge hos dine Hustruer ved højlys Dag.
“Yehova akuti, ‘Ine ndidzabweretsa tsoka pa iwe lochokera mʼbanja lako. Ndidzatenga akazi ako iwe ukuona ndi kuwapereka kwa wina amene ali pafupi nawe, ndipo iye adzagona ndi akazi ako masanasana Aisraeli onse akuona.
12 Thi du handlede i det skjulte, men jeg vil opfylde dette Ord i hele Israels Paasyn og ved højlys Dag!«
Iwe unachita zimenezi mwamseri koma Ine ndidzachita izi masanasana Aisraeli onse akuona.’”
13 Da sagde David til Natan: »Jeg har syndet mod HERREN!« Og Natan sagde til David: »Saa har HERREN ogsaa tilgivet dig din Synd; du skal ikke dø.
Kenaka Davide anati kwa Natani, “Ine ndachimwira Yehova.” Natani anayankha kuti, “Yehova wachotsa tchimo lanu. Simufa ayi.
14 Men fordi du ved denne Gerning har vist Foragt for HERREN, skal Sønnen, som er født dig, visselig dø!«
Komabe, popeza pochita zimenezi mwachititsa kuti adani a Yehova amunyoze, mwana amene akubalireniyo adzafa.”
15 Derpaa gik Natan til sit Hus. Og HERREN ramte det Barn, Urias's Hustru havde født David, med Sygdom.
Natani atapita kwawo, Yehova anakantha mwana amene mkazi wa Uriya anabereka ndipo anayamba kudwala.
16 Da søgte David Gud for Barnet, holdt Faste og gik hen og lagde sig om Natten paa Jorden i Sæk.
Davide anapempherera mwanayo kwa Mulungu. Iye anasala chakudya ndipo analowa mʼnyumba mwake nagona pansi usiku wonse.
17 De ældste i hans Hus kom til ham for at faa ham til at rejse sig, men han vilde ikke, og han holdt ikke Maaltid sammen med dem.
Akuluakulu a banja lake anayima pambali pake kuti amudzutse, koma iye anakana, ndipo sanadye chakudya chilichonse pamodzi ndi iwo.
18 Syvendedagen døde Barnet; men Davids Folk turde ikke lade ham vide, at Barnet var død, thi de tænkte: »Da Barnet levede, vilde han ikke laane os Øre, naar vi talte til ham; hvor kan vi da nu sige til ham, at Barnet er død? Han kunde gøre en Ulykke!«
Mwana anamwalira pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Antchito a Davide anaopa kumuwuza kuti mwanayo wamwalira, popeza ankaganiza kuti, “Pamene mwanayu anali ndi moyo, ife tinayankhula Davide koma sanatimvere. Nanga tingamuwuze bwanji kuti mwana wamwalira? Mwina atha kudzipweteka.”
19 Men da David saa, at hans Folk hviskede sammen, skønnede han, at Barnet var død. Saa spurgte David sine Folk: »Er Barnet død?« Og de svarede: »Ja, han er død!«
Davide anaona kuti antchito ake amanongʼonezana pakati pawo ndipo anazindikira kuti mwanayo wamwalira. Iye anafunsa kuti, “Kodi mwanayo wamwalira?” Iwo anayankha kuti, “Inde wamwalira.”
20 Da rejste David sig fra Jorden, tvættede og salvede sig, tog andre Klæder paa og gik ind i HERRENS Hus og bad; saa gik han hjem, forlangte at faa Mad sat frem og spiste.
Ndipo Davide anayimirira. Anakasamba nadzola mafuta ndi kusintha zovala zake. Pambuyo pake anapita ku nyumba ya Yehova kukapembedza. Kenaka anapita ku nyumba kwake ndipo atapempha chakudya anamupatsa nadya.
21 Da sagde hans Folk til ham: »Hvorledes er det dog, du bærer dig ad? Medens Barnet endnu levede, fastede du og græd; og nu da Barnet er død, rejser du dig og spiser!«
Antchito ake anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuchita zinthu motere? Pamene mwana anali ndi moyo, munkasala chakudya ndi kulira, koma tsopano pamene mwana wamwalira inu mukudzuka ndi kudya!”
22 Han svarede: »Saa længe Barnet levede, fastede jeg og græd; thi jeg tænkte: Maaske er HERREN mig naadig, saa Barnet bliver i Live.
Iye anayankha kuti, “Pamene mwana anali ndi moyo ine ndinkasala zakudya ndi kulira. Ine ndinkaganiza kuti, ‘Akudziwa ndani? Yehova atha kundikomera mtima kuti mwanayo akhale ndi moyo.’
23 Men hvorfor skulde jeg faste, nu han er død? Kan jeg bringe ham tilbage igen? Jeg gaar til ham, men han kommer ikke tilbage til mig!«
Koma tsopano wamwalira ndisaliranji chakudya? Kodi ndingathe kumubwezanso? Ine ndidzapita kumene kuli iyeko, koma iye sadzabwerera kwa ine.”
24 Derpaa trøstede David sin Hustru Batseba, og efter at han var gaaet ind til hende og havde ligget hos hende, fødte hun en Søn, som han kaldte Salomo, og ham elskede HERREN.
Ndipo Davide anatonthoza mkazi wake Batiseba, napita kwa iye ndi kugona naye. Iye anabereka mwana wamwamuna, ndipo anamutcha dzina lake Solomoni. Yehova ankamukonda iye.
25 Han overgav ham til Profeten Natan, og paa HERRENS Ord kaldte denne ham Jedidja.
Ndipo chifukwa chakuti Yehova ankamukonda iyeyo, Yehovayo anatumiza mawu kwa mneneri Natani kuti akamutchule Yedidiya.
26 Joab angreb imidlertid Rabba i Ammon og indtog Vandbyen.
Pa nthawi imeneyi Yowabu anamenyana ndi Raba ku Amoni ndipo analanda nsanja yaufumu.
27 Derpaa sendte Joab Bud til David og lod sige: »Jeg har angrebet Rabba og indtaget Vandbyen;
Ndipo Yowabu anatumiza amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Ine ndamenyana ndi Raba ndipo ndatenga zitsime zake za madzi.
28 kald nu Resten af Hæren sammen, saa du kan belejre Byen og indtage den, for at det ikke skal blive mig, der indtager den og faar mit Navn udraabt over den!«
Ndipo tsopano sonkhanitsani asilikali onse ndipo muzungulire mzindawo ndi kuwulanda.”
29 Da samlede David hele Hæren og drog til Rabba, angreb og indtog det.
Kotero Davide anasonkhanitsa ankhondo onse ndipo anapita ku Raba kukawuthira nkhondo ndi kuwulanda.
30 Og han tog Kronen af Milkoms Hoved; den var af Guld og vejede en Talent; der var en Ædelsten paa den, og den blev sat paa Davids Hoved. Et vældigt Bytte fra Byen førte han med sig,
Davide anachotsa chipewa chaufumu pamutu pa mfumu yawo ndipo Davide anavala chipewacho. Chipewacho chinkalemera makilogalamu asanu agolide, ndiponso chinali ndi miyala yokongola. Iye anatenga katundu wambiri kuchokera mu mzindawo,
31 og Indbyggerne slæbte han bort, satte dem til Savene, Jernhakkerne og Jernøkserne og lod dem trælle ved Teglovnene. Saaledes gjorde han ved alle Ammoniternes Byer. Derpaa vendte David og hele Hæren tilbage til Jerusalem.
ndipo anatulutsa anthu amene anali mʼmenemo, nawayika kuti azigwira ntchito ya macheka, yosula makasu ndi nkhwangwa, ndiponso yowomba njerwa. Davide anachita izi ndi mizinda yonse ya Aamoni. Kenaka iye pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo anabwerera ku Yerusalemu.

< 2 Samuel 12 >