< Anden Kongebog 4 >
1 En Kvinde, som var gift med en af Profetsønnerne raabte til Elisa: »Din Træl, min Mand, er død; og du ved, at din Træl frygtede HERREN. Og nu kommer en, der har Krav paa ham, for at tage mine to Drenge til Trælle!«
Mkazi wa mmodzi mwa ana a aneneri anafuwula kwa Elisa kuti, “Mtumiki wanu, mwamuna wanga wamwalira ndipo inu mukudziwa kuti ankaopa Yehova. Koma tsopano munthu amene mwamuna wanga anakongolako zinthu zake, akubwera kudzatenga ana anga awiri aamuna kuti akhale akapolo ake.”
2 Da sagde Elisa til hende: »Hvad kan jeg gøre for dig? Sig mig, hvad du har i Huset?« Hun svarede: »Din Trælkvinde har ikke andet i Huset end et Krus Olie.«
Elisa anayankha mayiyo kuti, “Kodi ufuna ndikuchitire chiyani? Tandiwuza uli ndi chiyani mʼnyumba mwako?” Mayiyo anayankha kuti, “Mdzakazi wanu alibe kanthu kalikonse koma timafuta pangʼono chabe.”
3 Da sagde han: »Gaa ud og bed alle dine Naboer om tomme Dunke, ikke for faa!
Elisa anati, “Pita kabwereke mitsuko yonse yopanda kanthu kwa anzako. Usakabwereke mitsuko yochepa.
4 Saa lukker du dig inde med dine Sønner og fylder paa alle disse Dunke, og naar de er fulde, sætter du dem til Side!«
Kenaka ukalowe mʼnyumba mwako ndi kudzitsekera iwe ndi ana ako. Mukakatero mukakhuthulire mafuta mʼmitsuko yonseyo, ndipo mtsuko uliwonse ukadzaza muzikawuyika pambali.”
5 Saa gik hun fra ham og lukkede sig inde med sine Sønner; og de rakte hende Dunkene, medens hun fyldte paa.
Mayi uja anachoka kwa Elisa nakadzitsekera ndi ana ake. Anthu anabweretsa mitsuko kwa iye ndipo ankathiramo mafuta.
6 Og da Dunkene var fulde, sagde hun til Sønnen: »Ræk mig een Dunk til!« Men han svarede: »Der er ikke flere Dunke!« Da holdt Olien op at flyde.
Mitsuko yonse itadzaza, mayiyo anawuza mwana wake kuti, “Bweretsa mtsuko wina.” Koma iye anayankha kuti, “Mitsuko yonse yatha.” Pamenepo mafuta analeka kutuluka.
7 Det kom hun og fortalte den Guds Mand; og han sagde: »Gaa hen og sælg Olien og betal din Gæld; og lev saa med dine Sønner af Resten!«
Mayiyo anapita nakamuwuza munthu wa Mulungu amene anamuyankha kuti, “Pita, kagulitse mafutawo ndipo ukabweze ngongole ija. Ndalama zotsalazo zikakhale zako ndi ana ako.”
8 Det skete en Dag, at Elisa paa sin Vej kom til Sjunem. Der boede en velhavende Kvinde, som nødte ham til at spise hos sig; og hver Gang han senere kom forbi, tog han derind og spiste.
Tsiku lina Elisa anapita ku Sunemu. Kumeneko kunkakhala mayi wina wachuma amene anawumiriza Elisa kuti adye chakudya. Choncho nthawi iliyonse imene Elisa amadutsa kumeneko, ankayima ndi kudya.
9 Hun sagde nu til sin Mand: »Jeg ved, af det er en hellig Guds Mand, der stadig kommer her forbi;
Mayiyo anawuza mwamuna wake kuti, “Taonani, ine ndikudziwa kuti munthu amene amadutsa pano nthawi zambiriyu ndi munthu woyera wa Mulungu.
10 lad os mure en lille Stue paa Taget og sætte Seng, Bord, Stol og Lampe ind til ham, for at han kan gaa derind, naar han kommer til os!«
Tiyeni timumangire kachipinda kakangʼono pa denga la nyumbayi ndi kumuyikiramo bedi ndi tebulo, mpando ndi nyale. Akabwera kuno azikhala mʼmenemo.”
11 Saa kom han en Dag derhen og gik op i Stuen og lagde sig.
Tsiku lina pamene Elisa anafika ku Sunemu, iye anakalowa mʼchipinda chake chija nagona mʼmenemo.
12 Og han sagde til sin Tjener Gehazi: »Kald paa Sjunemkvinden!« Og han kaldte paa hende, og hun traadte frem for ham.
Iye anati kwa mtumiki wake Gehazi, “Muyitane Msunemuyu.” Ndipo anapita kukamuyitana mayiyo, ndipo anabwera nayima pamaso pa Elisa.
13 Da sagde han til Gehazi: »Sig til hende: Se, du har haft al den Ulejlighed for vor Skyld; hvad kan jeg gøre for dig? Ønsker du, at jeg skal tale din Sag hos Kongen eller Hærføreren?« Men hun svarede: »Jeg bor midt iblandt mit Folk!«
Elisa anati kwa Gehazi, “Muwuze mayiyo kuti, ‘Wavutika potichitira zonsezi. Nanga tsopano ifeyo tikuchitire chiyani? Kodi ukufuna kuti tikadziwitse mfumu kapena mtsogoleri wa ankhondo zimene watichitirazi?’” Mayiyo anayankha kuti, “Ine ndimakhala mwamtendere pakati pa abale anga.”
14 Da sagde han: »Hvad kan jeg da gøre for hende?« Gehazi sagde: »Jo, hun har ingen Søn, og hendes Mand er gammel.«
Elisa anafunsanso Gehazi kuti, “Kodi tingamuchitire chiyani?” Gehazi anati, “Ndithu, mayiyu alibe mwana ndipo mwamuna wake ndi wokalamba.”
15 Da sagde han: »Kald paa hende!« Og han kaldte paa hende, og hun tog Plads ved Døren.
Pamenepo Elisa anati, “Muyitane.” Choncho Gehazi anamuyitana, ndipo iye anabwera nayima pa khomo.
16 Da sagde han: »Om et Aar ved denne Tid har du en Dreng ved Brystet!« Men hun sagde: »Nej dog, Herre! Den Guds Mand maa ikke narre sin Trælkvinde!«
Elisa anati kwa mayiyo, “Nthawi ngati yomwe ino chaka chamawa, udzakhala utanyamula mwana wamwamuna mʼmanja mwako.” Mayiyo anatsutsa zimenezi nanena kuti, “Ayi mbuye wanga. Inu munthu wa Mulungu, musanamize mdzakazi wanu!”
17 Men Kvinden blev frugtsommelig og fødte en Søn Aaret efter ved samme Tid, saaledes som Elisa havde sagt hende.
Koma mayi uja anakhala woyembekezera, ndipo chaka chotsatiracho, nthawi ngati yomweyo anabereka mwana wamwamuna monga momwe Elisa anamuwuzira.
18 Da Drengen var blevet stor, gik han en Dag ud til sin Fader hos Høstfolkene.
Mwana uja anakula, ndipo tsiku lina anapita kwa abambo ake amene anali ndi anthu odula tirigu.
19 Da sagde han til sin Fader: »Mit Hoved, mit Hoved!« Og hans Fader sagde til en Karl: »Bær ham hjem til hans Moder!«
Mwanayo anafuwula kwa abambo ake kuti, “Mayo! Mutu wanga ine! Mayo! Mutu wanga ine!” Abambo akewo anawuza wantchito wake kuti, “Munyamule ndi kukamupereka kwa amayi ake.”
20 Han tog, ham og har ham hjem til hans Moder, og han sad paa hendes Skød til Middag; saa døde han.
Wantchito uja atamunyamula ndi kumupereka kwa amayi ake. Mwanayo anakhala pa miyendo ya amayi akeyo mpaka masana, ndipo pambuyo pake anamwalira.
21 Men hun gik op og lagde ham paa den Guds Mands Seng, og derefter lukkede hun Døren og gik.
Mayiyo ananyamula mwanayo nakamugoneka pa bedi la munthu wa Mulungu uja. Kenaka anatseka chitseko iye nʼkuchokapo.
22 Saa kaldte hun paa sin Mand og sagde: »Send mig en af Karlene med et Æsel, for at jeg hurtig kan komme hen til den Guds Mand og hjem igen!«
Iye anayitanitsa mwamuna wake namuwuza kuti, “Tumizireni wantchito mmodzi ndi bulu mmodzi kuti ndipite mofulumira kwa munthu wa Mulungu nʼkubwererako.”
23 Han spurgte: »Hvad vil du hos ham i Dag? Det er jo hverken Nymaanedag eller Sabbat!« Men hun sagde: »Lad mig om det!«
Mwamuna wakeyo anafunsa kuti, “Chifukwa chiyani ukupita kwa iyeyo lero? Lero si tsiku la Chikondwerero cha Mwezi Watsopano kapena tsiku la Sabata.” Mayiyo anayankha kuti, “Zonse zili bwino.”
24 Derpaa sadlede hun Æselet og sagde til Karlen: »Driv nu godt paa! Stands mig ikke i Farten, før jeg siger til!«
Mayiyo anamangirira chishalo pa bulu ndipo anawuza wantchito wake kuti, “Yendetsa bulu mofulumira. Usachepetse liwiro pokhapokha nditakuwuza.”
25 Saa drog hun af Sted og kom til den Guds Mand paa Kamels Bjerg. Da den Guds Mand fik Øje paa hende i Frastand, sagde han til sin Tjener Gehazi: »Se, der er Sjunemkvinden!
Choncho ananyamuka nakafika kwa munthu wa Mulungu uja ku Phiri la Karimeli. Munthu wa Mulungu ataona mayiyo patali, anawuza mtumiki wake Gehazi kuti, “Taona! Msunemu uyo!
26 Løb hende straks i Møde og spørg hende: Har du det godt? Har din Mand det godt? Har Drengen det godt?« Hun svarede: »Ja, vi har det godt!«
Thamanga msanga ukakumane naye ndipo ukamufunse kuti, ‘Kodi muli bwino? Kodi mwamuna wanu ali bwino? Kodi mwana wanu ali bwino?’” Mayiyo anayankha kuti, “Zonse zili bwino.”
27 Men da hun kom hen til den Guds Mand paa Bjerget, klamrede hun sig til hans Fødder. Gehazi traadte til for at støde hende bort, men den Guds Mand sagde: »Lad hende være, hun er i Vaande, og HERREN har dulgt det for mig og ikke aabenbaret mig det!«
Atafika kwa munthu wa Mulunguyo pa phiripo, mayiyo anagwira mapazi a Elisa. Gehazi anabwera kuti amukankhe, koma munthu wa Mulungu anati, “Musiye! Iyeyu ali pa mavuto aakulu, koma Yehova wandibisira zimenezi ndipo sanandiwuze chifukwa chake.”
28 Da sagde hun: »Har jeg vel bedt min Herre om en Søn? Sagde jeg ikke, at du ikke maatte narre mig?«
Tsono mayiyo anati, “Mbuye wanga, kodi ine ndinakupemphani mwana? Kodi sindinakuwuzeni kuti musandinamize?”
29 Saa sagde han til Gehazi: »Omgjord din Lænd, tag min Stav i Haanden og drag af Sted! Møder du nogen, saa hils ikke paa ham, og hilser nogen paa dig, saa gengæld ikke hans Hilsen; og læg min Stav paa Drengens Ansigt!«
Elisa anawuza Gehazi kuti, “Manga lamba mʼchiwuno mwako, tenga ndodo yanga mʼdzanja lako ndipo thamanga. Ngati ukumana ndi munthu wina aliyense, usamupatse moni, ndipo ngati wina akupatsa moni, usayankhe. Ukagoneke ndodo yanga pa nkhope ya mwanayo.”
30 Men Drengens Moder sagde: »Saa sandt HERREN lever, og saa sandt du lever, jeg gaar ikke fra dig!« Da stod han op og gik med hende.
Koma mayi wake wa mwana uja anati, “Pali Yehova wamoyo ndiponso pali inu nomwe, ineyo sindidzakusiyani.” Choncho Elisa ananyamuka natsatira mayiyo.
31 Imidlertid var Gehazi gaaet i Forvejen og havde lagt Staven paa Drengens Ansigt; men ikke en Lyd hørtes, og der var intet Livstegn. Da vendte han tilbage og gik Elisa i Møde, meldte ham det og sagde: »Drengen vaagnede ikke!«
Gehazi anatsogola nakagoneka ndodoyo pa nkhope ya mwanayo, koma sipanamveke mawu kapena kugwedezeka kuonetsa kuti ali moyo. Choncho Gehazi anabwerera kukakumana ndi Elisa ndipo anamuwuza kuti, “Mwanayo sanatsitsimuke.”
32 Og da Elisa var kommet ind i Huset, saa han Drengen ligge død paa Sengen.
Ndipo Elisa atafika ku nyumbako, taonani, mwanayo anali wakufa atamugoneka pa bedi lake.
33 Han gik da hen og lukkede sig inde med ham og bad til HERREN.
Elisa analowa mʼnyumbamo natseka chitseko. Anali awiri okha mʼchipindamo ndipo iye anapemphera kwa Yehova.
34 Derpaa steg han op og lagde sig oven paa Drengen med sin Mund paa hans Mund, sine Øjne paa hans Øjne og sine Hænder paa hans Hænder, og medens han saaledes bøjede sig over ham, blev Drengens Legeme varmt.
Kenaka anakwera pa bedi ndi kumugonera mwanayo, pakamwa pake panakhudzana ndi pakamwa pa mwanayo, maso ake anakhudzana ndi maso a mwanayo, ndipo manja ake anakhudzana ndi manja a mwanayo. Pamene ankadzitambalitsa yekha pa mwanayo, thupi la mwanayo linayamba kufunda.
35 Saa steg han ned og gik een Gang frem og tilbage i Huset, og da han atter steg op og bøjede sig over Drengen, nyste denne syv Gange og slog Øjnene op.
Elisa anatembenuka nayenda uku ndi uku kamodzi mʼchipindamo ndipo kenaka anakweranso pa bedi nagoneranso mwanayo. Mwanayo anayetsemula kasanu ndi kawiri ndipo anatsekula maso ake.
36 Derpaa kaldte han paa Gehazi og sagde: »Kald paa Sjunemkvinden!« Han kaldte saa paa hende, og hun kom til ham. Da sagde han: »Tag din Dreng!«
Elisa anayitana Gehazi ndipo anati, “Muyitane Msunemuyo.” Ndipo anaterodi. Mayiyo atabwera, Elisa anati, “Tenga mwana wako.”
37 Og hun traadte hen og faldt ned for hans Fødder og kastede sig til Jorden, tog saa sin Dreng og gik ud.
Mayiyo analowa, nagwada pa mapazi a Elisa, naweramitsa mutu wake pansi. Kenaka ananyamula mwana wake natuluka.
38 Dengang Hungersnøden var i Landet, vendte Elisa tilbage til Gilgal. Som nu Profetsønnerne sad hos ham, sagde han til sin Tjener: »Sæt den store Gryde over og kog en Ret Mad til Profetsønnerne!«
Elisa anabwerera ku Giligala ndipo ku dera limenelo kunali njala. Elisa akukumana ndi ana a aneneri, anati kwa mtumiki wake, “Ika mʼphika waukulu pa moto ndipo uwaphikire chakudya anthu awa.”
39 Saa gik en ud paa Marken for at plukke Urter, og da han fandt en Slyngplante med vilde Agurker, plukkede han saa mange, han kunde bære i sin Kappe; da han kom tilbage, skar han dem itu og kom dem i Gryden, thi han kendte dem ikke.
Mmodzi mwa ana aneneriwo anapita kuthengo kukafuna ndiwo ndipo anakapeza mpesa wakuthengo. Iye anathyolako zipatso zake nadzaza nsalu yake. Atabwerera, anazidula zipatsozo naziyika mu mʼphika, ngakhale kuti panalibe amene ankazidziwa.
40 Derpaa øste man op for Mændene, for at de kunde spise, men saa snart de smagte Maden, skreg de op og raabte: »Døden er i Gryden, du Guds Mand!« Og de kunde ikke spise Maden.
Anawapakulira anthu chakudyacho, koma atayamba kudya, anthuwo anafuwula kuti, “Inu munthu wa Mulungu muli imfa mu mʼphikamu!” Ndipo sakanatha kudya chakudyacho.
41 Men han sagde: »Hent noget Mel!« Og da han havde hældt det i Gryden, sagde han: »Øs nu op for Folkene, saa de kan spise!« Saa var der ingen Ulykke i Gryden mere.
Elisa anati, “Bweretsani ufa.” Iye anathira ufa mu mʼphikamo ndipo anati, “Perekani chakudyachi kwa anthu kuti adye.” Ndipo mu mʼphikamo munalibenso zoopsa.
42 Engang kom en Mand fra Ba'al-Sjalisja og bragte den Guds Mand Brød af nyt Korn, tyve Bygbrød, og nyhøstet Korn i sin Ransel. Da sagde han: »Giv Folkene det at spise!«
Munthu wina wochokera ku Baala-Salisa anabwera atamutengera munthu wa Mulungu malofu a barele makumi awiri opangidwa kuchokera ku zokolola zoyamba kucha, pamodzinso ndi ngala zatsopano za tirigu. Elisa anati kwa munthuyo, “Apatse anthu kuti adye.”
43 Men hans Tjener sagde: »Hvorledes skal jeg kunne sætte dette frem for hundrede Mennesker?« Men han sagde: »Giv Folkene det at spise! Thi saa siger HERREN: De skal spise og levne!«
Mtumiki wake anafunsa kuti, “Kodi ndikachigawe motani chakudyachi kwa anthu 100?” Koma Elisa anamuwuzanso kuti, “Apatse anthu adye. Pakuti izi ndi zimene Yehova akunena kuti, ‘Iwo adzadya chakudyachi ndipo china chidzatsalako.’”
44 Da satte han det frem for dem, og de spiste og levnede efter HERRENS Ord.
Tsono iye anachipereka kwa anthuwo ndipo anadya china nʼkutsalako, molingana ndi mawu a Yehova.