< Anden Krønikebog 36 >

1 Folket fra Landet tog nu Josias's Søn Joahaz og hyldede ham til Konge i Jerusalem i hans Faders Sted.
Tsono anthu a mʼdzikomo anatenga Yehowahazi mwana wa Yosiya namuyika kukhala mfumu mu Yerusalemu mʼmalo mwa abambo ake.
2 Joahaz var tre og tyve Aar gammel, da han blev Konge, og han herskede tre Maaneder i Jerusalem.
Yowahazi anali wa zaka 23 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa miyezi itatu.
3 Men Ægypterkongen afsatte ham fra Regeringen i Jerusalem og lagde en Skat af hundrede Talenter Sølv og ti Talenter Guld paa Landet.
Mfumu ya Igupto inamuchotsa pa udindo wa ufumu mu Yerusalemu ndipo inakhometsa msonkho dziko la Yuda wa makilogalamu 3,400 asiliva ndi agolide.
4 Derpaa gjorde Ægypterkongen hans Broder Eljakim til Konge over Juda og Jerusalem, og han ændrede hans Navn til Jojakim; hans Broder Joahaz derimod tog Neko med til Ægypten.
Mfumu ya Igupto inakhazika Eliyakimu, mʼbale wake wa Yehowahazi kukhala mfumu ya Yuda ndi Yerusalemu ndipo anasintha dzina la Eliyakimu kukhala Yehoyakimu. Koma Neko anatenga Yowahazi mʼbale wake wa Eliyakimu ndi kupita naye ku Igupto.
5 Jojakim var fem og tyve Aar gammel, da han blev Konge, og han herskede elleve Aar i Jerusalem. Han gjorde, hvad der var ondt i HERREN hans Guds Øjne.
Yehoyakimu anali wa zaka 25 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11. Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wake.
6 Kong Nebukadnezar af Babel drog op imod ham og lagde ham i Kobberlænker for at føre ham til Babel;
Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni anachita naye nkhondo ndipo anamumanga ndi zingwe zamkuwa ndi kumutenga kupita naye ku Babuloni.
7 og Nebukadnezar lod en Del af HERRENS Hus's Kar bringe til Babel og opstillede dem i sin Borg i Babel.
Nebukadinezara anatenganso zipangizo za ku Nyumba ya Yehova kupita nazo ku Babuloni ndipo anaziyika mʼnyumba ya Mulungu wake kumeneko.
8 Hvad der ellers er at fortælle om Jojakim og de Vederstyggeligheder, han øvede, hvad der er at sige om ham, staar optegnet i Bogen om Israels og Judas Konger. Og hans Søn Jojakin blev Konge i hans Sted.
Zochitika zina za pa ulamuliro wa Yehoyakimu, zinthu zonyansa zimene anachita ndi zonse zinapezeka kuti zinali zomutsutsa zalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda. Ndipo Yehoyakini mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
9 Jojakin var atten Aar gammel, da han blev Konge, og han herskede tre Maaneder og ti Dage i Jerusalem. Han gjorde, hvad der var ondt i HERRENS Øjne.
Yehoyakini anali ndi zaka 21 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa miyezi itatu ndi masiku khumi. Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
10 Næste Aar sendte Kong Nebukadnezar Folk og lod ham bringe til Babel tillige med HERRENS Hus's kostelige Kar; og han gjorde hans Broder Zedekias til Konge over Juda og Jerusalem.
Nthawi ya mphukira, mfumu Nebukadinezara inayitanitsa Yehoyakini ndipo inapita naye ku Babuloni, pamodzi ndi ziwiya zamtengowapatali za mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova, ndipo anayika Zedekiya malume wake kukhala mfumu ya Yuda ndi Yerusalemu.
11 Zedekias var een og tyve Aar gammel, da han blev Konge, og han herskede i elleve Aar i Jerusalem.
Zedekiya anali ndi zaka 21 pamene ankakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 11.
12 Han gjorde, hvad der var ondt i HERREN hans Guds Øjne. Han ydmygede sig ikke under de Ord, Profeten Jeremias talte fra HERRENS Mund.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wake ndipo sanadzichepetse yekha pamaso pa mneneri Yeremiya amene ankayankhula mawu a Yehova.
13 Desuden faldt han fra Kong Nebukadnezar, der havde taget ham i Ed ved Gud; og han var halsstarrig og forhærdede sit Hjerte, saa han ikke omvendte sig til HERREN, Israels Gud.
Iye anawukiranso mfumu Nebukadinezara amene anamulumbiritsa mʼdzina la Mulungu. Iyeyo anali wosamva ndipo anawumitsa mtima wake. Sanatembenukire kwa Yehova Mulungu wa Israeli.
14 Ligeledes gjorde alle Judas Øverster og Præsterne og Folket sig skyldige i megen Troløshed ved at efterligne alle Hedningefolkenes Vederstyggeligheder, og de besmittede HERRENS Hus, som han havde helliget i Jerusalem.
Kuwonjezera apo, atsogoleri onse a ansembe ndi anthu ena anapitirapitira kukhala osakhulupirika, kutsatira machitidwe onse onyansa a mitundu ina ndi kudetsa Nyumba ya Yehova Mulungu wawo, imene anayipatula mu Yerusalemu.
15 HERREN, deres Fædres Gud, sendte tidlig og silde manende Ord til dem ved sine Sendebud, fordi han ynkedes over sit Folk og sin Bolig;
Yehova, Mulungu wa makolo awo, ankatumiza mawu kwa iwo kudzera kwa amithenga ake kawirikawiri, chifukwa ankawamvera chisoni anthu ake ndi malo ake okhalapo.
16 men de spottede Guds Sendebud, lod haant om hans Ord og gjorde sig lystige over hans Profeter, indtil HERRENS Vrede mod hans Folk tog til i den Grad, at der ikke mere var Lægedom.
Koma iwo ananyoza amithenga a Mulungu, anapeputsa mawu awo ndipo ankaseka aneneri ake mpaka anawutsa mkwiyo wa Yehova pa anthu ake ndipo panalibenso mankhwala owachiritsa.
17 Han førte Kaldæernes Konge imod dem, og han dræbte deres unge Mandskab med Sværdet i deres hellige Tempel og ynkedes ikke over Yngling eller Jomfru, gammel eller Olding — alt overgav han i hans Haand.
Yehova anabweretsa mfumu ya anthu a ku Babuloni, imene inapha anyamata awo ndi lupanga ku malo opatulika, ndipo sanasiye kaya mnyamata kapena mtsikana, wamkulu kapena wokalamba. Mulungu anapereka onsewo kwa Nebukadinezara.
18 Alle Karrene i Guds Hus, store og smaa, HERRENS Hus's Skatte og Kongens og hans Øverstes Skatte lod han alt sammen bringe til Babel.
Iye ananyamula kupita nazo ku Babuloni zipangizo zonse za mʼNyumba ya Yehova Mulungu wawo, zazikulu ndi zazingʼono zomwe, ndi chuma cha mʼNyumba ya Yehova ndiponso chuma cha mfumu ndi akuluakulu ake.
19 De stak Ild paa Guds Hus, nedrev Jerusalems Mur, opbrændte alle dets Borge og ødelagde alle kostelige Ting deri.
Iwo anayatsa moto Nyumba ya Mulungu, ndipo anagwetsa makoma a Yerusalemu. Anatentha moto nyumba zonse zaufumu ndipo anawononga chilichonse chimene chinali chofunika.
20 Dem, Sværdet levnede, førte han som Fanger til Babel, hvor de blev Trælle for ham og hans Sønner, indtil Perserriget fik Magten,
Iye anagwira ukapolo anthu otsala amene anapulumuka ku lupanga ndi kupita nawo ku Babuloni, ndipo anakhala antchito ake ndi ana ake mpaka pamene ufumu wa Peresiya unakhazikitsidwa.
21 for at HERRENS Ord gennem Jeremias's Mund kunde opfyldes, indtil Landet fik sine Sabbater godtgjort; saa længe Ødelæggelsen varede, hvilede det, til der var gaaet halvfjerdsindstyve Aar.
Dziko linakondwera ndi masabata ake. Pa nthawi yonse ya chipasuko chake nthaka inapuma, mpaka zaka 70 zinakwana pokwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Yeremiya.
22 Men i Perserkongen Kyros's første Regeringsaar vakte HERREN, for at hans Ord gennem Jeremias's Mund kunde opfyldes, Perserkongen Kyros's Aand, saa han lod følgende udraabe i hele sit Rige og desuden kundgøre ved en Skrivelse:
Mʼchaka choyamba cha Koresi mfumu ya Peresiya, pofuna kukwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Yeremiya, Yehova anakhudza mtima wa mfumu ya Peresiya kuti alengeze mu ufumu wake wonse ndipo anazilemba:
23 »Perserkongen Kyros gør vitterligt: Alle Jordens Riger har HERREN, Himmelens Gud, givet mig; og han har paalagt mig at bygge ham et Hus i Jerusalem i Juda. Hvem iblandt eder, der hører til hans Folk, med ham være HERREN hans Gud, og han drage derop!«
Chimene mfumu Koresi ya Peresiya ikunena ndi ichi: “Yehova, Mulungu wakumwamba wandipatsa ine mafumu onse a dziko lapansi ndipo wandisankha kuti ndimumangire Nyumba ya Mulungu ku Yerusalemu ku Yuda. Aliyense wa anthu ake pakati panu, Yehova Mulungu wake akhale naye, ndipo apite.”

< Anden Krønikebog 36 >