< Anden Krønikebog 31 >

1 Da alt det var til ende, drog alle de Israeliter, som var til stede, ud til Judas Byer, og de sønderbrød Stenstøtterne, omhuggede Asjerastøtterne og nedrev Offerhøjene og Altrene i hele Juda og Benjamin og i Efraim og Manasse, saa der ikke blev Spor tilbage; saa vendte alle Israeliterne hjem, hver til sin Ejendom i deres Byer.
Zonse zitatha, Aisraeli onse amene anali kumeneko anapita ku mizinda ya ku Yuda, nakaphwanya miyala yachipembedzo ndi kudula mitengo ya mafano a Asera. Iwo anakawononga malo achipembedzo ndi maguwa ansembe amene anali mʼdziko lonse la Yuda, Benjamini, Efereimu ndi Manase. Atawononga zonsezi, Aisraeli anabwerera ku mizinda yawo ndi ku malo awo.
2 Saa ordnede Ezekias Præsternes og Leviternes Skifter, Skifte for Skifte, saa at hver enkelt Præst og Levit fik sin særlige Gerning med at ofre Brændofre og Takofre og med af gøre Tjeneste og love og prise i HERRENS Lejrs Porte.
Hezekiya anakhazikitsa magulu a ansembe ndi Alevi, gulu lililonse monga mwa ntchito zawo ngati ansembe kapena Alevi, kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, kutumikira, kuyamikira ndi kuyimba matamando pa zipata za ku malo okhala Yehova.
3 Hvad Kongen gav af sit Gods, var til Brændofrene, Morgen— og Aftenbrændofrene og Brændofrene paa Sabbaterne, Nymaanerne og Højtiderne, som det er foreskrevet i HERRENS Lov.
Kuchokera pa chuma chake, mfumu inapereka nsembe zopsereza za mmawa ndi madzulo ndiponso nsembe zopsereza za pa Chikondwerero cha Masabata, Chikondwerero cha Mwezi Watsopano ndipo inakhazikitsa zikondwerero monga zinalembedwera mʼmalamulo a Yehova.
4 Og han bød Folket, dem, der boede i Jerusalem, at afgive, hvad der tilkom Præsterne og Leviterne, for at de kunde holde fast ved HERRENS Lov.
Iyo inalamula anthu amene amakhala mu Yerusalemu kupereka gawo lawo kwa ansembe ndi Alevi kuti iwowo adzipereke ku malamulo a Yehova.
5 Saa snart det Bud kom ud, bragte Israeliterne i rigelig Mængde Førstegrøde af Korn, Most, Olie og Honning og al Markens Afgrøde, og de gav Tiende af alt i rigeligt Maal;
Lamuloli atangolilengeza, Aisraeli anapereka mowolowamanja zipatso zoyamba kucha za tirigu, vinyo watsopano, mafuta ndi uchi ndi zonse zomwe nthaka yawo inabereka. Anabweretsa zochuluka kwambiri, chakhumi cha chilichonse.
6 ogsaa de Israeliter, der boede i Judas Byer, gav Tiende af Hornkvæg og Smaakvæg, og de bragte Helliggaverne, der var helliget HERREN deres Gud, og lagde dem Bunke for Bunke.
Aisraeli ndi Ayuda amene amakhala mʼmizinda ya Yuda anabweretsanso chakhumi cha ngʼombe zawo ndi nkhosa ndi chakhumi cha zinthu zoyera zoperekedwa kwa Yehova Mulungu wawo, ndipo anaziyika mʼmilumilu.
7 I den tredje Maaned begyndte de at ophobe Bunkerne, og i den syvende Maaned var de færdige.
Anayamba kuchita izi mwezi wachitatu ndipo anatsiriza mwezi wachisanu ndi chiwiri.
8 Ezekias og Øversterne kom saa og synede Bunkerne, og de priste HERREN og hans Folk Israel.
Hezekiya ndi akuluakulu ake atabwera ndi kuona miluyo, anatamanda Yehova ndi kudalitsa anthu ake, Aisraeli.
9 Da Ezekias spurgte sig for hos Præsterne og Leviterne om Bunkerne,
Hezekiya anafunsa ansembe ndi Alevi za miluyi;
10 svarede Ypperstepræsten Azarja af Zadoks Hus: »Siden man begyndte at bringe Offerydelsen til HERRENS Hus, har vi spist os mætte og faaet rigelig tilovers, thi HERREN har velsignet sit Folk, saa at vi har faaet al den Rigdom her tilovers!«
ndipo Azariya, mkulu wa ansembe, ochokera ku banja la Zadoki anayankha kuti, “Kuyambira pamene anthu anayamba kubweretsa zopereka zawo ku Nyumba ya Yehova ife takhala ndi zokwanira kudya ndi zina zambiri zosunga, chifukwa Yehova wadalitsa anthu ake, ndipo mulu umenewu ndiye zotsala.”
11 Ezekias gav da Befaling til at indrette Kamre i HERRENS Hus; og det gjorde man.
Hezekiya analamula kuti akonze zipinda zosungiramo za mʼNyumba ya Yehova, ndipo izi zinachitika.
12 Saa bragte man samvittighedsfuldt Offerydelsen, Tienden og Helliggaverne derind. Den øverste Opsynsmand derover var Leviten Konanja, den næstøverste hans Broder Sjim'i;
Ndipo iwo mokhulupirika anabweretsa zopereka, chakhumi ndi mphatso zopatulika. Konaniya Mlevi ndiye amayangʼanira zinthu zimenezi ndipo mʼbale wake Simei ndiye anali wachiwiri wake.
13 og Jehiel, Azarja, Nahat, Asa'el, Jerimot, Jozabad, Eliel, Jismakjahu, Mahat og Benaja var Opsynsmænd under Konanja og hans Broder Sjim'i efter den Ordning, som var truffet af Ezekias og Azarja, Øversten i Guds Hus.
Yehieli, Azaziya, Nahati, Asaheli, Yerimoti, Yozabadi, Elieli, Isimakiya, Mahati ndi Benaya anali oyangʼanira motsogozedwa ndi Konaniya ndi Simei, mʼbale wake. Iwowa anasankhidwa ndi mfumu Hezekiya ndi Azariya mkulu woyangʼanira Nyumba ya Mulungu.
14 Leviten Kore, Jimnas Søn, der var Dørvogter paa Østsiden, havde Tilsyn med de frivillige Gaver til Gud og skulde uddele HERRENS Offerydelse og de højhellige Gaver;
Kore mwana wa Imuna Mlevi, mlonda wa Chipata Chakummawa, amayangʼanira zopereka zaufulu kwa Mulungu, ankagawa zopereka za kwa Yehova ndiponso mphatso zopatulika.
15 under ham sattes Eden, Minjamin, Jesua, Sjemaja, Amarja og Sjekanja i Præstebyerne til samvittighedsfuldt at forestaa Uddelingen til deres Brødre i Skifterne, baade store og smaa,
Edeni, Miniyamini, Yesuwa, Semaya, Amariya, Sekaniya amamuthandiza mokhulupirika mʼmizinda yonse a ansembe kugawira kwa ansembe anzawo monga mwa magulu awo, aakulu ndi aangʼono omwe.
16 dem af Mandkøn, der var indført i Fortegnelserne fra Treaarsalderen og opefter. Undtaget var alle, der kom til HERRENS Hus for efter de enkelte Dages Krav at udføre deres Embedsgerning efter deres Skifter.
Kuwonjezera apa, amagawira ana aamuna a zaka zitatu kapena kupitirira amene mayina awo anali mʼmbiri ya mibado yawo, amene adzalowe mʼNyumba ya Yehova kugwira ntchito za tsiku ndi tsiku za magulu awo, molingana ndi udindo ndi magulu awo.
17 Præsterne indførtes i Fortegnelserne efter deres Fædrenehuse, Leviterne fra Tyveaarsalderen og opefter efter deres Embedspligter, efter deres Skifter,
Ndipo anazigawa kwa ansembe amene analembetsa mayina awo mwa mbiri ya mabanja awo, chimodzimodzinso Alevi amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirira molingana ndi udindo wawo ndi magulu awo.
18 Og de indførtes i Fortegnelserne med hele deres Familie, deres Hustruer, Sønner og Døtre, hele Standen, thi de tog sig samvittighedsfuldt af det hellige.
Iwo anaphatikizanso ana onse aangʼono, akazi ndiponso ana aamuna ndi ana aakazi a gulu lonse amene analembedwa mʼmbiri ya mibado yawo iyi, pakuti anakhulupirika pa kudzipatula okha.
19 Arons Sønner, Præsterne, som boede paa Græsmarkerne omkring deres Byer, havde i hver By nogle navngivne Mænd til at uddele, hvad der tilkom alle af Mandkøn blandt Præsterne og de i Fortegnelserne indførte Leviter.
Kunena za ansembe, zidzukulu za Aaroni, amene amakhala mʼminda yozungulira mizinda yawo kapena mzinda wina uliwonse, anthu anasankhidwa mowatchula mayina kuti azipereka magawo kwa munthu wamwamuna aliyense pakati pawo ndiponso kwa onse amene analembedwa mʼmbiri ya mibado ya Alevi.
20 Saaledes gik Ezekias frem i hele Juda, og han gjorde, hvad der var godt, ret og sandt for HERREN hans Guds Aasyn.
Izi ndi zimene Hezekiya anachita mu Yuda monse, kuchita zabwino, zolungama ndi zokhulupirika pamaso pa Yehova Mulungu wake.
21 Alt, hvad han tog fat paa vedrørende Tjenesten i Guds Hus eller Loven eller Budet for saaledes at søge sin Gud, det gjorde han af hele sit Hjerte, og det lykkedes for ham.
Pa chilichonse chimene anachita pa ntchito ya Nyumba ya Mulungu ndi pa kumvera malangizo ndi malamulo, iye anafunafuna Mulungu wake ndipo anagwira ntchito ndi mtima wake wonse. Ndipo zinthu zimamuyendera bwino.

< Anden Krønikebog 31 >