< 1 Samuel 1 >

1 Der var en Mand fra Ramatajim, en Zufit fra Efraims Bjerge ved Navn Elkana, en Søn af Jerobam, en Søn af Elihu, en Søn af Tohu, en Søn af Zuf, en Efraimit.
Panali munthu wina wochokera ku Ramataimu, Mzofimu wa ku dziko la mapiri la Efereimu. Iyeyu dzina lake anali Elikana ndipo anali mwana wa Yerohamu, mwana wa Elihu, mwana wa Tohu, mwana wa Zufu wa fuko la Efereimu.
2 Han havde to Hustruer; den ene hed Hanna, den anden Peninna; Peninna havde Børn, men Hanna ikke.
Iye anali ndi akazi awiri, Hana ndi Penina. Penina anali ndi ana, koma Hana analibe.
3 Denne Mand drog hvert Aar op fra sin By for at tilbede Hærskarers HERRE og ofre til ham i Silo, hvor Elis to Sønner Hofni og Pinehas Var Præster for HERREN.
Chaka ndi chaka Elikana ankachoka ku mudzi kwawo kupita ku Silo kukapembedza ndi kukapereka nsembe kwa Yehova Wamphamvuzonse. Ku Siloko kunali ana awiri a Eli, Hofini ndi Finehasi amene anali ansembe a Yehova.
4 En Dag ofrede nu Elkana — han plejede at give sin Hustru Peninna og alle hendes Sønner og Døtre flere Dele,
Tsiku lopereka nsembe likafika Elikana amapereka magawo a nsembeyo kwa mkazi wake Penina ndi kwa ana ake onse aamuna ndi aakazi.
5 men skønt han elskede Hanna, gav han hende kun een Del, fordi HERREN havde tillukket hendes Moderliv;
Ngakhale ankamukonda Hana, koma ankamupatsa gawo limodzi popeza Yehova sanamupatse ana.
6 hendes Medbejlerske tilføjede hende ogsaa grove Krænkelser for den Skam, at HERREN havde tillukket hendes Moderliv.
Tsono popeza Yehova sanamupatse Hana ana, mkazi mnzakeyo ankamuyamba dala ndi cholinga chomukwiyitsa.
7 Saaledes gik det Aar efter Aar: hver Gang de drog op til HERRENS Hus, krænkede hun hende saaledes — saa skete det, at hun græd og ikke vilde spise.
Izi zimachitika chaka ndi chaka. Hana ankati akamapita ku Nyumba ya Yehova mkazi mnzakeyo ankamunyogodola. Choncho Hana ankangokhalira kulira osafuna ndi kudya komwe.
8 Da sagde hendes Mand Elkana til hende: »Hanna, hvorfor græder du, og hvorfor spiser du ikke? Hvorfor er du mismodig? Er jeg dig ikke mere værd end ti Sønner?«
Tsono mwamuna wake Elikana ankamufunsa kuti, “Hana ukulira chifukwa chiyani? Wakhumudwa ndi chiyani kuti sukufuna ndi kudya komwe? Kodi ine kwa iwe sindili woposa ana aamuna khumi?”
9 Men da de havde holdt Maaltid i Silo, stod Hanna op og traadte hen for HERRENS Aasyn, medens Præsten Eli sad paa sin Stol ved en af Dørstolperne i HERRENS Hus;
Tsiku lina atatha kudya ndi kumwa ku Silo kuja, Hana anayimirira kukapemphera. Nthawiyi nʼkuti wansembe Eli atakhala pa mpando pa khomo la Nyumba ya Yehova.
10 og i sin Vaande bad hun under heftig Graad til HERREN
Hana anavutika mʼmoyo mwake, ndipo anapemphera kwa Yehova akulira kwambiri.
11 og aflagde det Løfte: »Hærskarers HERRE! Hvis du vil se til din Tjenerindes Nød og komme mig i Hu og ikke glemme din Tjenerinde, men give din Tjenerinde en Søn, saa vil jeg give ham til HERREN alle hans Levedage, og ingen Ragekniv skal komme paa hans Hoved!«
Ndipo iye analumbira kuti, “Inu Yehova Wamphamvuzonse, ngati muyangʼana kusauka kwa mtumiki wanune, ndi kuyankha pemphero langa osandiyiwala ine mtumiki wanu pondipatsa mwana wamwamuna, ine ndidzamupereka mwanayo kwa inu Yehova masiku onse a moyo wake. Lumo silidzapita pa mutu pake.”
12 Saaledes bad hun længe for HERRENS Aasyn, og Eli iagttog hendes Mund;
Akupemphera choncho kwa Yehova, Eli ankamuyangʼana pakamwa.
13 men da Hanna talte ved sig selv, saa kun hendes Læber bevægede sig, og hendes Stemme ikke kunde høres, troede Eli, at hun var beruset,
Hana ankapemphera chamumtima ndipo milomo yake inkangogwedera koma mawu ake samamveka. Choncho Eli anaganiza kuti anali ataledzera.
14 og sagde til hende: »Hvor længe vil du gaa og være drukken? Se at komme af med din Rus!«
Ndipo anamufunsa Hana kuti, “Kodi mukhala chiledzerere mpaka liti? Pitani, ayambe wakuchokani vinyo mwamwayo.”
15 Men Hanna svarede: »Nej, Herre! Jeg er en haardt prøvet Kvinde; Vin og stærk Drik har jeg ikke drukket; jeg udøste kun min Sjæl for HERRENS Aasyn.
Koma Hana anayankha kuti, “Sichoncho mbuye wanga. Ndakhala ndikumukhuthulira Yehova chisoni changa. Sindinamwe vinyo kapena chakumwa choledzeretsa chilichonse, popeza nthawi yonseyi ndakhala ndikupereka kwa Yehova nkhawa yayikulu ndi mavuto anga.
16 Regn ikke din Trælkvinde for en daarlig Kvinde! Nej, hele Tiden har jeg talt ud af min dybe Kummer og Kvide!«
Musaganize kuti mtumiki wanu ndi kukhala mkazi wachabechabe. Ine ndakhala ndi kupereka nkhawa yanga yayikulu ndi zowawa zanga.”
17 Eli svarede: »Gaa bort i Fred! Israels Gud vil give dig, hvad du har bedt ham om!«
Eli anayankha, “Pitani mu mtendere, ndipo Mulungu wa Israeli akupatseni zimene mwamupemphazo.”
18 Da sagde hun: »Maatte din Trælkvinde finde Naade for dine Øjne!« Saa gik Kvinden sin Vej, og hun spiste og saa ikke længer forgræmmet ud.
Hana anati, “Mundikomerebe mtima mtumiki wanune.” Kenaka anachoka nakadya, ndipo sanaonekenso wachisoni.
19 Næste Morgen stod de tidligt op og kastede sig ned for HERRENS Aasyn; og saa vendte de tilbage og kom hjem til deres Hus i Rama. Og Elkana kendte sin Hustru Hanna, og HERREN kom hende i Hu;
Elikana ndi banja lake anadzuka mmawa mwake nakapemphera pamaso pa Yehova. Pambuyo pake anabwerera kwawo ku Rama. Elikana anakhala pamodzi ndi mkazi wake, ndipo Yehova anamukumbuka Hanayo.
20 og hun blev frugtsommelig og fødte en Søn Aaret efter og gav ham Navnet Samuel; »thi, « sagde hun, »jeg har bedt mig ham til hos HERREN!«
Motero Hana anakhala ndi pakati ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha dzina lake Samueli, popeza anati, “Ndinachita kumupempha kwa Yehova.”
21 Da Elkana nu med hele sit Hus drog op for at bringe HERREN det aarlige Offer og sit Løfteoffer,
Elikana ndi banja lake lonse anapita kukapereka nsembe ya pa chaka kwa Yehova ndi kukakwaniritsa malonjezo ake.
22 drog Hanna ikke med; thi hun sagde til sin Mand: »Jeg vil vente, til Drengen er vænnet fra, saa vil jeg bringe ham derhen, for at han kan stedes for HERRENS Aasyn og blive der for stedse!«
Koma Hana sanapite nawo popeza anawuza mwamuna wake kuti, “Mwanayu akadzaleka kuyamwa, ndidzapita naye ndi kukamupereka pamaso pa Yehova ndipo adzakhala kumeneko moyo wake wonse.”
23 Da sagde hendes Mand Elkana til hende: »Gør, som du synes! Bliv her, indtil du har vænnet ham fra! Maatte HERREN kun gøre dit Ord til Virkelighed!« Saa blev Kvinden hjemme og ammede sin Søn, indtil hun vænnede ham fra.
Elikana mwamuna wake anamuwuza kuti, “Chita chimene chakukomera. Tsala kuno mpaka utamusiyitsa kuyamwa, Yehova yekha akwaniritse mawu ake.” Choncho mkaziyo anatsala ku nyumba ndi kusamalira mwana wake mpaka atamuletsa kuyamwa.
24 Men da hun havde vænnet ham fra, tog hun ham med, desuden en treaars Tyr, en Efa Mel og en Dunk Vin, og hun kom til HERRENS Hus i Silo og havde Drengen med.
Atamuletsa kuyamwa, Hana anatenga mwanayo ali wachichepere, ndikupita naye ku nyumba ya Yehova ku Silo. Anatenga ngʼombe yamphongo ya zaka zitatu, ufa wa makilogalamu khumi, ndi thumba lachikopa la vinyo.
25 Da nu Tyren var slagtet, kom Drengens Moder til Eli
Tsono anapha ngʼombe yamphongo ija ndi kupereka mwana uja kwa Eli.
26 og sagde: »Hør mig, Herre! Saa sandt du lever, Herre, jeg er den Kvinde, som stod her ved din Side og bad til HERREN.
Ndipo Hana anati kwa Eli, “Mbuye wanga, ine ndikunenetsadi pamaso panu kuti ndine mkazi uja amene anayima pamaso panu ndi kumapemphera kwa Yehova.
27 Om denne Dreng bad jeg, og HERREN gav mig, hvad jeg bad ham om.
Ndinapempha mwana uyu, ndipo Yehova wandipatsa chimene ndinamupempha.
28 Derfor vil jeg ogsaa overlade ham til HERREN; hele sit Liv skal han være overladt til HERREN!« Og hun lod ham blive der for HERRENS Aasyn.
Ndiye tsopano ine ndikumupereka kwa Yehova. Pa moyo wake wonse adzakhala wa Yehova.” Ndipo onse anapembedza Yehova kumeneko.

< 1 Samuel 1 >