< 1 Samuel 14 >
1 Da hændte det en Dag, at Sauls Søn Jonatan sagde til sin Vaabendrager: »Kom, lad os gaa over til Filisternes Forpost her lige overfor!« Men til sin Fader sagde han intet derom.
Tsiku lina Yonatani mwana wa Sauli anawuza mnyamata wake womunyamulira zida zake za nkhondo kuti, “Tiye tiwoloke tipite ku kaboma ka Afilisti tsidya ilo.” Koma iye sanawuze abambo ake.
2 Saul sad just ved Udkanten af Geba under Granatæbletræet ved Tærskepladsen, og Folkene, som var hos ham, var omtrent 600 Mand.
Sauli ankakhala mʼmalire a Gibeya pa tsinde pa mtengo wamakangadza ku Migironi. Anthu amene anali naye analipo 600.
3 Og Ahija, en Søn af Ahitub, der var Broder til Ikabod, en Søn af Pinehas, en Søn af Eli, HERRENS Præst i Silo, bar Efoden. Men Folkene vidste intet om, at Jonatan var gaaet.
Pakati pawo panalinso Ahiya amene ankavala efodi. Iye anali mwana wa Ahitubi, mʼbale wake wa Ikabodi mwana wa Finehasi, mwana wa Eli, wansembe wa Yehova wa ku Silo. Koma palibe amene anadziwa kuti Yonatani wachoka.
4 I Passet, som Jonatan søgte at komme over for at angribe Filisternes Forpost, springer en Klippespids frem paa hver Side; den ene hedder Bozez, den anden Sene.
Pa mpata pamene Yonatani ankafuna kudutsa kukafika ku kaboma ka nkhondo ka Afilisti kunali thanthwe lotsetsereka mbali ina ndi lina lotsetsereka mbali inayo. Thanthwe limodzi linkatchedwa Bozezi ndipo linalo linkatchedwa Seni.
5 Den ene Spids rager i Vejret paa Nordsiden ud for Mikmas, den anden paa Sydsiden ud for Geba.
Thanthwe limodzi linali chakumpoto kuyangʼanana ndi Mikimasi, ndipo thanthwe linalo linali chakummwera kuyangʼanana ndi Geba.
6 Jonatan sagde da til Vaabendrageren: »Kom, lad os gaa over til disse uomskaarnes Forpost; maaske vil HERREN staa os bi, thi intet hindrer HERREN i at give Sejr, enten der er mange eller faa!«
Yonatani anawuza mnyamata wake womunyamulira zida uja kuti, “Tiye tiwoloke tipite ku kaboma ka anthu osachita mdulidwewo. Mwina Yehova adzatigwirira ntchito. Palibe chomuletsa Yehova kutipulumutsa, ngakhale tikhale ambiri kapena ochepa.”
7 Vaabendrageren svarede: »Gør, hvad du har i Sinde! Jeg gaar med; som du vil, vil ogsaa jeg!«
Mnyamata uja anati, “Chitani chilichonse chimene mtima wanu ukhumba. Ine ndili nanu pamodzi. Chimene mtima wanu ukhumba ndi chomwenso ine ndikhumba.”
8 Da sagde Jonatan: »Vi søger nu at komme over til de Mænd og sørger for, at de faar os at se.
Yonatani anati, “Tiye tsono tiwoloke kupita kumene kuli anthuwo ndi kukadzionetsa kwa iwo.
9 Hvis de saa siger til os: Staa stille, vi kommer hen til eder! saa bliver vi staaende, hvor vi staar, og gaar ikke op til dem.
Akatiwuza kuti, ‘Imani pomwepo mpaka tikupezeni,’ ife tikangoyima pomwepo osapita kumene kuli iwoko.
10 Men siger de: Kom op til os! gaar vi derop; thi saa har HERREN givet dem i vor Haand; det skal være vort Tegn!«
Koma akadzati, ‘Bwerani kuno,’ ndiye ife tikapitedi, chifukwa ichi chidzakhala chizindikiro chakuti Yehova wapereka mʼmanja mwathu.”
11 Da nu Filisternes Forpost fik Øje paa dem, sagde Filisterne: »Se, der kommer nogle Hebræere krybende ud af de Jordhuller, de har skjult sig i!«
Choncho awiriwa anadzionetsa ku kaboma ka nkhondo ka Afilisti. Tsono Afilistiwo anati, “Taonani! Aheberi akutuluka mʼmaenje mʼmene anabisala.”
12 Og Mændene, der stod paa Forpost, raabte til Jonatan og hans Vaabendrager: »Kom op til os, saa skal vi lære jer!« Da sagde Jonatan til Vaabendrageren: »Følg med derop, thi HERREN har givet dem i Israels Haand!«
Anthu a ku kaboma kaja anafuwula kwa Yonatani ndi mnyamata wake uja kuti, “Bwerani kuno ndipo tikuphunzitsani phunziro.” Ndipo Yonatani anati kwa mnyamata wake. “Nditsate pakuti Yehova wapereka Afilistiwa mʼmanja mwa Aisraeli.”
13 Saa klatrede Jonatan op paa Hænder og Fødder, og Vaabendrageren bagefter. Da flygtede de for Jonatan; og han huggede dem ned, og Vaabendrageren fulgte efter og gav dem Dødsstødet;
Choncho Yonatani anakwera mokwawa, ndipo mnyamata wake uja ankamutsata. Tsono Yonatani anathira nkhondo Afilisti aja namawagwetsa, ndipo mnyamata wake uja ankawapha pambuyo pa iyeyo.
14 og i første Omgang fældede Jonatan og hans Vaabendrager henved tyve Mand paa en Strækning af omtrent en halv Dags Pløjeland.
Nthawi yoyambayo Yonatani ndi mnyamata wake uja anapha anthu makumi awiri ndipo anawaphera pa malo ochepa okwanira ngati theka la ekala.
15 Da opstod der Rædsel baade i og uden for Lejren, og alle Krigerne, baade Forposten og Strejfskaren, sloges med Rædsel; tilmed kom der et Jordskælv, og det fremkaldte en Guds Rædsel.
Tsono gulu lonse la ankhondo, ndiye kuti iwo amene anali mʼmisasa ndi mʼminda ndiponso iwo amene anali ku kaboma ka ankhondo kaja, onse anagwidwa ndi mantha aakulu. Dzikonso linagwedezeka, choncho anthu anachita mantha koopsa.
16 Men da Sauls Udkigsmænd i Geba i Benjamin saa derhen, opdagede de, at det bølgede hid og did i Lejren.
Alonda a Sauli a ku Gibeya dziko la Benjamini atangomwaza maso anangoona chigulu cha asilikali chikumwazikana uku ndi uku.
17 Da sagde Saul til sine Folk: »Hold Mønstring og se efter, hvem af vore der er gaaet bort!« Og ved Mønstringen viste det sig, at Jonatan og hans Vaabendrager manglede.
Kenaka Sauli anawawuza anthu amene anali naye kuti, “Awerengeni asilikali kuti muona amene wachoka.” Atawawerenga anapeza kuti Yonatani ndi mnyamata wake womunyamulira zida zake za nkhondo palibe.
18 Da sagde Saul til Ahija: »Bring Efoden hid!« Han bar nemlig dengang Efoden foran Israel.
Tsono Sauli anawuza Ahiya kuti, “Bwera nalo Bokosi la Mulungulo.” (Nthawi imeneyo nʼkuti efodiyo ili ndi Ahiya pamaso pa Aisraeli).
19 Men medens Saul talte med Præsten, blev Forvirringen i Filisternes Lejr større og større. Saul sagde da til Præsten: »Lad det kun være!«
Pamene Sauli amayankhula ndi wansembe, phokoso limanka likulirakulira mu msasa wa Afilisti, Kotero Sauli anati kwa wansembe, “Leka kuwombeza.”
20 Og alle Sauls Krigere samlede sig om ham, og da de kom til Kamppladsen, se, da var den enes Sværd løftet mod den andens, og alt var i stor Forvirring.
Ndipo Sauli ndi asilikali onse amene anali naye anasonkhana kupita kukamenya nkhondo, ndipo anangoona chisokonezo chachikulu kwambiri. Afilisti akuphana okhaokha.
21 Og de Hebræere, som tidligere havde staaet under Filisterne og havde gjort dem Hærfølge, faldt fra og sluttede sig til Israel, som fulgte Saul og Jonatan.
Aheberi ena amene kale anali ndi Afilisti mpaka kukakhala ku misasa yawo, iwonso anatembenuka nakhala pamodzi ndi Aisraeli amene ankatsata Sauli ndi Yonatani.
22 Og da de israelitiske Mænd, som havde skjult sig i Efraims Bjerge, hørte, at Filisterne var paa Flugt, satte ogsaa de efter dem for at bekæmpe dem.
Ngakhale Aisraeli amene ankabisala ku dziko lamapiri la Efereimu atamva kuti Afilisti akuthawa, nawonso anawathamangitsa Afilistiwo nawathira nkhondo.
23 Saaledes gav HERREN Israel Sejr den Dag. Da Kampen havde strakt sig hen forbi Bet-Horon —
Nkhondo inapitirira mpaka kufika ku Beti-Aveni. Choncho Yehova anapulumutsa Aisraeli tsiku limenelo.
24 alle Krigerne var med Saul, omtrent 10 000 Mand, og Kampen bredte sig over Efraims Bjerge — begik Saul den Dag en stor Daarskab, idet han tog Folket i Ed og sagde: »Forbandet være hver den, som nyder noget før Aften, før jeg faar taget Hævn over mine Fjender!« Og alt Folket afholdt sig fra at spise.
Koma asilikali a Israeli anavutika tsiku limenelo, chifukwa Sauli anawalumbirira Aisraeli kuti, “Wotembereredwa munthu aliyense amene adzadya kusanade, ine ndisanalipsire adani anga!” Kotero palibe wankhondo aliyense amene analawa chakudya.
25 Der fandtes nogle Bikager paa Marken,
Gulu lonse la ankhondo linalowa mʼnkhalango mmene munali uchi.
26 og da Folket kom til Bikagerne, var Bierne borte; men ingen førte Haanden til Munden; thi Folket frygtede Eden.
Atalowa mʼnkhalango, anaona uchi ukukha, koma palibe amene anadya, pakuti ankaopa lumbiro lija.
27 Jonatan havde dog ikke hørt, at hans Fader tog Folket i Ed, og han rakte Spidsen af den Stav, han havde i Haanden, ud, dyppede den i en Bikage og førte Haanden til Munden; derved fik hans Øjne atter Glans.
Koma Yonatani sanamve kuti abambo ake anawalumbirira anthu aja choncho anatenga ndodo yake imene inali mʼdzanja lake ndipo anayipisa mu chisa cha njuchi. Choncho iye anadya uchiwo ndipo mʼmaso mwake munayera.
28 Da tog en af Krigerne til Orde og sagde: »Din Fader tog Folket i Ed og sagde: Forbandet være hver den, som nyder noget i Dag! Og dog var Folket udmattet.«
Kenaka mmodzi mwa Asilikali anamuwuza kuti, “Abambo ako alumbirira anthu nati, ‘Wotembereredwa munthu aliyense amene adye chakudya lero.’ Nʼchifukwa chake anthu alefuka.”
29 Men Jonatan sagde: »Min Fader styrter Landet i Ulykke! Se, hvor mine Øjne fik Glans, fordi jeg nød den Smule Honning!
Yonatani anati, “Abambo anga achita chinthu choyipira dziko. Taonani mʼmaso mwanga mwayera chifukwa ndalawa uchiwu pangʼono.
30 Nej, havde Folket blot i Dag spist dygtigt af Byttet, det tog fra Fjenden! Thi nu blev Filisternes Nederlag ikke stort.«
Zikanakhala zabwino kwambiri anthuwa akanadya lero zofunkha za adani awo. Zikanatero tikanapha Afilisti ochuluka.”
31 De slog da den Dag Filisterne fra Mikmas til Ajjalon, og Folket var meget udmattet.
Tsiku limenelo Aisraeli anapha Afilisti kuchokera ku Mikimasi mpaka ku Ayaloni. Koma Aisraeliwo analefuka kwambiri ndi njala.
32 Derfor kastede Folket sig over Byttet, tog Smaakvæg, Hornkvæg og Kalve og slagtede dem paa Jorden og spiste Kødet med Blodet i.
Choncho iwo anathamangira pa zofunkha ndipo anatenga nkhosa, ngʼombe ndi ana angʼombe. Iwo anazipha zonsezi nazidya pamodzi ndi magazi omwe.
33 Da meldte man det til Saul og sagde: »Se, Folket synder mod HERREN ved at spise Kødet med Blodet i!« Og han sagde: »I forbryder eder! Vælt mig en stor Sten herhen!«
Koma anthu ena anawuza Sauli kuti, “Taona anthu akuchimwira Yehova pakudya nyama yomwe ili ndi magazi.” Ndipo Sauli anati, “Mwaonetsa kusakhulupirika. Tsopano gubuduzirani mwala waukulu pano.”
34 Derpaa sagde Saul: »Gaa rundt iblandt Folket og sig til dem: Enhver skal bringe sin Okse eller sit Faar hen til mig og slagte det her! Saa kan I spise; men synd ikke mod HERREN ved at spise Kødet med Blodet i!« Da bragte hver og en af Folket, hvad han havde, og slagtede det der.
Kenaka Sauli anati, “Mwazikanani pakati pa anthu ndi kukawawuza kuti aliyense abwere ndi ngʼombe yake kapena nkhosa yake, ndipo adzayiphe pomwe pano ndi kuyidya. Musachimwire Yehova pakudya nyama imene ili ndi magazi.” Kotero aliyense anabwera ndi ngʼombe yake usiku womwewo ndi kuyipha pomwepo.
35 Og Saul byggede HERREN et Alter; det var det første Alter, han byggede HERREN.
Ndipo Sauli anamangira Yehova guwa. Ili linali guwa loyamba limene Sauli anamangira Yehova.
36 Derpaa sagde Saul: »Lad os drage ned efter Filisterne i Nat og udplyndre dem, før Dagen gryr, og ikke lade nogen af dem blive tilbage!« De svarede: »Gør, hvad du under for godt!« Men Præsten sagde: »Lad os her træde frem for Gud!«
Sauli anati, “Tiyeni titsatire Afilisti usikuwu ndi kulanda zinthu zawo mpaka mmawa. Tisasiyepo wamoyo ndi mmodzi yemwe.” Ankhondowo anayankha kuti, “Chitani chilichonse chimene chikukomerani.” Koma wansembe anati, “Tipemphe uphungu kwa Mulungu poyamba.”
37 Saa raadspurgte Saul Gud: »Skal jeg drage ned efter Filisterne? Vil du give dem i Israels Haand?« Men han svarede ham ikke den Dag.
Choncho Sauli anafunsa Mulungu kuti, “Kodi ndiwatsatire Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwathu?” Koma Mulungu sanamuyankhe tsiku limenelo.
38 Da sagde Saul: »Kom hid, alle Folkets Øverster, og se efter, hvad det er for en Synd, der er begaaet i Dag;
Choncho Sauli anati, “Bwerani kuno nonse atsogoleri a anthu, ndipo tiyeni tione kuti kodi tchimo limeneli lachitika bwanji lero?
39 thi saa sandt HERREN lever, han, som har givet Israel Sejr: Om det saa er min Søn Jonatan, der har begaaet den, skal han dø!« Men ingen af Folket svarede.
Pali Yehova amene amapulumutsa Israeli, ngakhale tchimolo litapezeka ndi mwana wanga Yonatani, iye afe ndithu.” Koma palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthuwo amene anamuyankha.
40 Da sagde han til hele Israel: »I skal være den ene Part, jeg og min Søn Jonatan den anden!« Folket svarede Saul: »Gør, hvad du finder for godt!«
Tsono Sauli anawuza Aisraeli onse kuti, “Inu mukhale mbali imodzi. Ine ndi mwana wanga Yonatani tikhala mbali inayo.” “Chitani chilichonse chimene chikukomerani.”
41 Derpaa sagde Saul til HERREN: »Israels Gud! Hvorfor svarer du ikke din Tjener i Dag? Hvis Skylden ligger hos mig eller min Søn Jonatan, HERRE, Israels Gud, saa lad Urim komme frem; men ligger den hos dit Folk Israel, saa lad Tummim komme frem!« Da ramtes Jonatan og Saul af Loddet, men Folket gik fri.
Ndipo Sauli anapemphera kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, “Chifukwa chiyani simunandiyankhe ine mtumiki wanu lero lino? Ngati tchimoli lipezeka ndi ine kapena ndi Yonatani mwana wanga, Inu Mulungu wa Israeli, aoneke ndi Urimu. Koma ngati wochimwa ndi anthu anu, Aisraeli aoneke Tamimu.” Maere anagwera Sauli ndi Yonatani ndipo anthu anapezeka osalakwa.
42 Saul sagde da: »Kast Lod mellem mig og min Søn Jonatan!« Saa ramtes Jonatan.
Sauli anati, “Chitani maere pakati pa ine ndi Yonatani mwana wanga.” Ndipo maere anagwera Yonatani.
43 Da sagde Saul til Jonatan: »Sig mig, hvad du har gjort!« Jonatan svarede: »Jeg nød lidt Honning paa Spidsen af Staven, jeg havde i Haanden. Se, jeg er rede til at dø!«
Kenaka Sauli anati kwa Yonatani, “Ndiwuze chimene wachita.” Ndipo Yonatani anamuwuza kuti, “Ine ndinangolawa uchi pangʼono ndi ndodo yangayi. Ndiye ine ndili wokonzeka kufa.”
44 Da sagde Saul: »Gud ramme mig baade med det ene og det andet! Du skal visselig dø, Jonatan!«
Sauli anati, “Mulungu andilange ngakhale kufa kumene, ngati sufa iwe Yonatani.”
45 Men Folket sagde til Saul: »Skal Jonatan dø, han, som har vundet Israel denne store Sejr? Det være langt fra! Saa sandt HERREN lever, ikke et Haar skal krummes paa hans Hoved; thi med Guds Hjælp vandt han Sejr i Dag!« Da udløste Folket Jonatan, og han blev friet fra Døden.
Koma anthuwo anafunsa Saulo kuti, “Kodi Yonatani afe, iye amene wagwira ntchito iyi yayikulu yopulumutsa Aisraeli? Osatheka! Pali Yehova ngakhale tsitsi ndi limodzi lomwe lapamutu pake silidzathothoka, pakuti wachita zimenezi lero ndi thandizo la Mulungu.” Choncho anthuwo anamupulumutsa Yonatani, ndipo sanaphedwe.
46 Men Saul holdt op med at forfølge Filisterne og drog hjem, medens Filisterne trak sig tilbage til deres Land.
Pambuyo pake Sauli analeka kulondola Afilisti, kenaka anabwerera ku dziko lawo.
47 Da Saul havde vundet Kongedømmet over Israel, førte han Krig med alle sine Fjender rundt om, Moab, Ammoniterne, Edom, Kongen af Zoba og Filisterne, og Sejren fulgte ham overalt, hvor han vendte sig hen.
Sauli ali mtsogoleri wa Israeli, anachita nkhondo ndi adani awa omuzungulira: Mowabu, Amoni, Edomu mafumu a ku Zoba ndi Afilisti. Kulikonse kumene ankapita ankawagonjetsa.
48 Han udførte Heltegerninger, slog Amalek og befriede Israel fra dem, som hærgede det.
Anachita nkhondo mwamphamvu ndi kugonjetsa Aamaleki. Choncho anapulumutsa Aisraeli mʼmanja mwa anthu amene ankawalanda zinthu zawo.
49 Sauls Sønner var Jonatan, Jisjvi og Malkisjua; af hans to Døtre hed den førstefødte Merab og den yngste Mikal.
Ana aamuna a Sauli anali Yonatani, Isivi ndi Maliki-Suwa. Analinso ndi ana aakazi awiri, dzina la mwana wake wamkulu wamkazi linali Merabi ndipo la mwana wake wamngʼono wamkazi linali Mikala.
50 Sauls Hustru hed Ahinoam, en Datter af Ahima'az; hans Hærfører hed Abiner, en Søn af Sauls Farbroder Ner;
Dzina la mkazi wake linali Ahinoamu. Iyeyu anali mwana wa Ahimaazi. Dzina la mkulu wa ankhondo a Sauli linali Abineri mwana wa Neri, mʼbale wa abambo a Sauli.
51 Sauls Fader Kisj og Abners Fader Ner var Sønner af Abiel.
Kisi abambo a Sauli ndi Neri abambo a Abineri anali ana a Abieli.
52 Men Krigen med Filisterne var haard, lige saa længe Saul levede; og hver Gang Saul traf en heltemodig og tapper Mand, knyttede han ham til sig.
Pa moyo wake wonse, Sauli ankakhalira kuchita nkhondo pakati pa Israeli ndi Afilisti. Ndipo Sauli ankati akaona munthu aliyense wamphamvu kapena wolimba mtima ankamulemba ntchito mu gulu lake lankhondo.