< 1 Samuel 12 >
1 Da sagde Samuel til hele Israel: »Se, jeg har føjet eder i alt, hvad I har bedt mig om, og sat en Konge over eder.
Pambuyo pake Samueli anawuza Aisraeli onse kuti, “Ine ndamvera zonse zimene munandiwuza ndipo ndakupatsani mfumu kuti izikulamulirani.
2 Se, nu færdes Kongen for eders Ansigt; jeg er gammel og graa, og mine Sønner er nu iblandt eder; men jeg har færdedes for eders Ansigt fra min Ungdom indtil i Dag.
Tsopano muli ndi mfumu imene izikutsogolerani, koma ine ndakalamba, kumutu kwanga kuli imvi zokhazokha ndipo ana anga ali pamodzi ndi inu. Ndakhala ndili mtsogoleri wanu kuyambira ndili mnyamata mpaka lero.
3 Se, her staar jeg; viden imod mig i HERRENS og hans, Salvedes Paahør! Hvis Okse har jeg taget? Hvis Æsel har jeg taget? Hvem har jeg, undertrykt? Hvem har jeg gjort Uret? Af hvem har jeg taget Gave og derfor lukket Øjnene? I saa Fald vil jeg give eder Erstatning!«
Ine ndili pano. Ngati ndinalakwa chilichonse nditsutseni pamaso pa Yehova ndi wodzozedwa wake. Kodi ndinalanda ngʼombe ya yani? Kodi ndinalanda bulu wa yani? Kodi ndani amene ndinamudyera masuku pa mutu? Kodi ndinazunza yani? Kodi ndinalandira kwa yani chiphuphu choti nʼkundidetsa mʼmaso? Ngati ndinachita chilichonse cha izi, ine ndidzakubwezerani.”
4 Da sagde de: »Du har ikke undertrykt os eller gjort os Uret eller taget noget fra nogen.«
Iwo anayankha kuti, “Inu simunatidyere masuku pamutu kapena kutizunza. Simunalande kanthu kalikonse ka munthu.”
5 Derpaa sagde han til dem: »Saa er HERREN i Dag Vidne over for eder, ogsaa hans Salvede er Vidne, at I ikke har fundet noget hos mig.« De sagde: »Ja!«
Samueli anawawuza kuti, “Yehova ndiye mboni pakati pa inu ndi ine, ndiponso wodzozedwa wake ndi mboni kuti lero simunapeze chilichonse mʼdzanja langa.” Iwo anati, “Inde, Yehova ndiye mboni.”
6 Da sagde Samuel til Folket: »HERREN er Vidne, han, som udrustede Moses og Aron og førte eders Fædre op fra Ægypten.
Samueli anawawuzanso kuti, “Yehova ndiye amene anasankha Mose ndi Aaroni kuti atulutse makolo anu mʼdziko la Igupto.
7 Saa træd nu frem, at jeg kan gaa i Rette med eder for HERRENS Aasyn og kundgøre eder alle de Gerninger, HERREN i sin Retfærdighed har øvet mod eder og eders Fædre.
Nʼchifukwa chake tsopano imani pomwepa kuti ndikufotokozereni pamaso pa Yehova, za ntchito za chipulumutso zimene Yehova anachitira inu ndi makolo anu.
8 Da Jakob og hans Sønner var kommet til Ægypten, og Ægypterne plagede dem, raabte eders Fædre til HERREN, og HERREN sendte Moses og Aron, som førte eders Fædre ud af Ægypten, og han lod dem bosætte sig her.
“Yakobo atapita ku dziko la Igupto, Aiguptowo akuwazunza, iwo analirira kwa Yehova kuti awathandize, ndipo Yehova anatumiza Mose ndi Aaroni, amene anatulutsa makolo anu mʼdziko la Igupto ndi kudzawakhazika pa malo ano.
9 Men de glemte HERREN deres Gud; derfor prisgav han dem til Kong Jabin af Hazors Hærfører Sisera, til Filisterne og til Moabs Konge, saa de angreb dem.
“Koma iwo anayiwala Yehova Mulungu wawo, choncho Yehova anawapereka mʼdzanja la Sisera mkulu wa ankhondo wa mzinda wa Hazori, ndiponso mʼmanja mwa Afilisti ndi mfumu ya Mowabu. Mafumu onsewa anathira nkhondo makolo anu.
10 Da raabte de til HERREN og sagde: Vi har syndet, thi vi forlod HERREN og dyrkede Ba'alerne og Astarterne; men fri os nu af vore Fjenders Haand, saa vil vi dyrke dig!
Tsono iwo analira kwa Yehova nati, ‘Ife tachimwa, chifukwa tamusiya Yehova ndi kumatumikira mafano a Baala ndi Asiteroti. Koma tsopano tilanditseni mʼmanja mwa adani athu ndipo tidzakutumikirani.’
11 Saa sendte HERREN Jerubba'al, Barak, Jefta og Samuel; og han friede eder af eders Fjenders Haand rundt om, saa I kunde bo i Tryghed.
Choncho Yehova anatumiza Yeru-Baala, Bedani, Yefita ndi Samueli ndipo anakulanditsani mʼmanja mwa adani anu amene anakuzungulirani, kotero munakhala mwamtendere.
12 Men da I saa Ammoniterkongen Nahasj rykke frem imod eder, sagde I til mig: Nej, en Konge skal herske over os uagtet HERREN eders Gud var eders Konge!
“Koma mutaona kuti Nahasi mfumu ya Amoni inkabwera kudzamenyana nanu, inu munandiwuza kuti, ‘Ayi, ife tikufuna mfumu kuti itilamulire,’ ngakhale kuti Yehova Mulungu wanu ndiye anali mfumu yanu.
13 Og nu, her staar Kongen, som I har valgt og krævet; se, HERREN har sat en Konge over eder!
Tsopano nayi mfumu imene mwayisankha, imene munayipempha. Onani, Yehova wakupatsani mfumu.
14 Hvis I frygter HERREN og tjener ham, adlyder hans Røst og ikke er genstridige mod HERRENS Bud, men følger HERREN eders Gud, baade I og Kongen, som har faaet Herredømmet over eder, da skal det gaa eder vel.
Ngati muziopa Yehova ndi kumamutumikira ndi kumamumvera, osamupandukira ndiponso ngati inu pamodzi ndi mfumu yanu mudzatsata Yehova Mulungu wanu, ndiye zinthu zonse zidzakuyenderani bwino.
15 Adlyder I derimod ikke HERRENS Røst, men er genstridige mod HERRENS Bud, da skal HERRENS Haand ramme eder og eders Konge og ødelægge eder.
Koma mukapanda kumvera Yehova ndi kumupandukira, ndiye adzakulangani pamodzi ndi mfumu yanu yomwe.
16 Træd nu frem og se den vældige Gerning, HERREN vil øve for eders Øjne!
“Tsono imani pomwepa kuti muone chinthu chachikulu chimene Yehova ali pafupi kuchita pamaso panu!
17 Har vi ikke Hvedehøst nu? Men jeg vil raabe til HERREN, at han skal sende Torden og Regn, for at I kan kende og se, at det i HERRENS Øjne var en stor Brøde I begik, da I krævede en Konge!«
Kodi ino si nthawi yokolola tirigu? Komabe ndipemphera kwa Yehova kuti agwetse mvula ya mabingu. Zikatero mudzadziwa kuti tchimo lanu limene mwachita popempha mfumu kwa Yehova ndi lalikulu.”
18 Derpaa raabte Samuel til HERREN, og HERREN sendte samme Dag Torden og Regn. Da frygtede hele Folket saare for HERREN og Samuel,
Choncho Samueli anapemphera, ndipo Yehova anatumiza mvula ya mabingu tsiku lomwelo. Apo anthu aja anaopa kwambiri Yehova ndi Samueli.
19 og hele Folket sagde til Samuel: »Bed for dine Trælle til HERREN din Gud, at vi ikke skal dø, fordi vi til vore andre Synder har føjet den Brøde at kræve en Konge!«
Tsono anamupempha Samueli nati, “Chonde mutipempherere kwa Yehova, ife atumiki kuti tingafe pakuti pa machimo athu onse tawonjezapo tchimo lopempha mfumu.”
20 Da sagde Samuel til Folket: »Frygt ikke! Vel har I øvet al den Synd; men vend eder nu ikke fra HERREN, tjen ham af hele eders Hjerte
Samueli anayankha kuti, “Musaope, inu mwachitadi tchimo ili, koma musaleke kumutsata Yehova ndi kumutumikira ndi mtima wanu wonse.
21 og vend eder ikke til dem, som er Tomhed og hverken kan hjælpe eller frelse, fordi de er Tomhed.
Ndipo musatsate mafano achabechabe amene alibe phindu ndipo sangakupulumutseni popeza ndi achabechabe.
22 Thi for sit store Navns Skyld vil HERREN ikke forstøde sit Folk, da det jo har behaget HERREN at gøre eder til sit Folk.
Yehova adzakana anthu ake kuopa kuti dzina lake lamphamvu linganyozeke, pakuti chinamukondweretsa Yehova kuti akusandutseni inu kukhala anthu ake.
23 Det være ogsaa langt fra mig at synde mod HERREN og høre op med at bede for eder; jeg vil ogsaa vise eder den gode og rette Vej;
Ndiponso kunena za ine, zisachitike kuti ndichimwire Yehova pakulephera kukupemphererani. Ndipo ine ndidzakuphunzitsani njira yabwino ndi yolungama kuti muziyendamo.
24 men frygt HERREN og tjen ham oprigtigt af hele eders Hjerte; thi se, hvor store Ting han gjorde imod eder!
Koma onetsetsani kuti mukuopa Yehova ndi kumutumikira mokhulupirika ndi mtima wanu wonse. Nthawi zonse muziganizira zinthu zazikulu wakhala akukuchitirani.
25 Men hvis I handler ilde, skal baade I og eders Konge gaa til Grunde!«
Komabe mukapitirira kuchita zoyipa, ndiye kuti inu pamodzi ndi mfumu yanu mudzachotsedwa.”