< Første Kongebog 9 >

1 Men da Salomo var færdig med at opføre HERRENS Hus og Kongens Palads og alt, hvad han havde faaet Lyst til og sat sig for at udføre,
Solomoni atatsiriza kumanga Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu, ndi kukwaniritsa kuchita zonse zimene ankafuna,
2 lod HERREN sig anden Gang til Syne for ham, som han havde ladet sig til Syne for ham i Gibeon;
Yehova anamuonekera kachiwiri, monga momwe anamuonekera ku Gibiyoni.
3 og HERREN sagde til ham: »Jeg har hørt den Bøn og Begæring, du opsendte for mit Aasyn. Jeg har helliget dette Hus, som du har bygget, for der at stedfæste mit Navn til evig Tid, og mine Øjne og mit Hjerte skal være der alle Dage.
Yehova ananena kwa iye kuti: “Ndamva pemphero ndi pembedzero lako pa zimene wapempha pamaso panga. Ndayipatula Nyumba iyi, imene wamanga, poyikamo Dzina langa mpaka muyaya. Maso anga ndi mtima wanga zidzakhala pamenepo nthawi zonse.
4 Hvis du nu vandrer for mit Aasyn som din Fader David i Hjertets Uskyld og i Oprigtighed, saa du gør alt, hvad jeg har paalagt dig, og holder mine Anordninger og Lovbud,
“Kunena za iwe, ukayenda pamaso panga mokhulupirika, mwangwiro ndi moona mtima monga momwe anachitira abambo ako Davide, ndi kuchita zonse zimene ndakulamula ndi kusamalitsa malangizo ndi malamulo anga,
5 saa vil jeg opretholde din Kongetrone i Israel evindelig, som jeg lovede din Fader David, da jeg sagde: En Efterfølger skal aldrig fattes dig paa Israels Trone.
Ine ndidzakhazikitsa mpando wako waufumu pa Israeli mpaka muyaya, monga ndinalonjezera abambo ako Davide pamene ndinati, ‘Sipadzasowa munthu pa mpando waufumu wa Israeli.’
6 Men hvis I eller eders Børn vender eder bort fra mig og ikke holder mine Bud, mine Anordninger, som jeg har forelagt eder, men gaar hen og dyrker andre Guder og tilbeder dem,
“Koma ngati iwe kapena ana ako mudzapatuka ndi kuleka kusunga malamulo ndi mawu anga amene ndakupatsani ndi kupita kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza,
7 saa vil jeg udrydde Israel fra det Land, jeg gav dem; og det Hus, jeg har helliget for mit Navn, vil jeg forkaste fra mit Aasyn, og Israel skal blive til Spot og Spe blandt alle Folk,
pamenepo Ine ndidzazula Aisraeli mʼdziko limene ndinawapatsa ndiponso ndidzayikana Nyumba ino imene ndayipatula chifukwa cha Dzina langa. Pamenepo Aisraeli adzasanduka mwambi ndi chinthu chonyozedwa pakati pa anthu onse.
8 og dette Hus skal blive en Ruindynge, og enhver, som gaar der forbi, skal blive slaaet af Rædsel og give sig til at haanfløjte. Og naar man siger: Hvorfor har HERREN handlet saaledes mod dette Land og dette Hus?
Ndipo ngakhale kuti tsopano Nyumba ya Mulunguyi ndi yokongola kwambiri, onse amene adzadutsa pano adzadabwa kwambiri ndipo adzatsonya ndipo adzati, ‘Nʼchifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere mʼdziko muno ndi pa Nyumba ya Mulunguyi?’
9 skal der svares: Fordi de forlod HERREN deres Gud, som førte deres Fædre ud af Ægypten, og holdt sig til andre Guder, tilbad og dyrkede dem; derfor har HERREN bragt al denne Elendighed over dem!«
Anthu adzayankha kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti asiya Yehova Mulungu wawo amene anatulutsa makolo awo mʼdziko la Igupto, ndipo akangamira milungu ina ndi kumayipembedza ndi kuyitumikira. Choncho Iye wabweretsa zovuta zonsezi.’”
10 Da de tyve Aar var omme, i hvilke Salomo havde bygget paa de to Bygninger, HERRENS Hus og Kongens Palads —
Patatha zaka makumi awiri, ndiye nthawi imene Solomoni anamanga nyumba ziwirizi: Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu,
11 Kong Hiram af Tyrus havde sendt Salomo Cedertræ, Cyprestræ og Guld, saa meget han ønskede da gav Kong Salomo Hiram tyve Byer i Landskabet Galilæa.
Mfumu Solomoni anapereka mizinda makumi awiri ya ku Galileya kwa Hiramu mfumu ya ku Turo chifukwa Hiramu nʼkuti atapereka mitengo yonse ya mkungudza ndi ya payini ndiponso golide yense zimene Solomoni ankazifuna.
12 Men da Hiram kom fra Tyrus for at se de Byer, Salomo havde givet ham, syntes han ikke om dem;
Koma Hiramu atabwera kuchokera ku Turo kudzaona mizinda imene Solomoni anamupatsa, sanasangalatsidwe nayo mizindayo.
13 og han sagde: »Hvad er det for Byer, du har givet mig, Broder?« Derfor kaldte man den Kabullandet, som det hedder den Dag i Dag.
Iye anafunsa kuti, “Mʼbale wanga, kodi iyi nʼkukhala mizinda yondipatsa?” Ndipo iye anayitcha mizindayo Dziko la Kabuli, dzina lomwe amatchedwa mpaka lero lino.
14 Men Hiram sendte Kongen 120 Guldtalenter.
Koma Hiramu anali atatumiza kwa mfumu golide oposa makilogalamu 4,000.
15 Paa følgende Maade hang det sammen med de Hoveriarbejdere, Kong Salomo udskrev til at opføre HERRENS Hus, hans eget Palads, Millo, Jerusalems Mur, Hazor, Megiddo og Gezer
Izi ndi zimene anachita Mfumu Solomoni: Analamula anthu kuti agwire ntchito yathangata pomanga Nyumba ya Yehova, nyumba yake, malo achitetezo a Milo, mpanda wa Yerusalemu, Hazori, Megido ndi Gezeri.
16 (Farao, Ægypterkongen, var draget op, havde indtaget Gezer og stukket det i Brand; alle Kana'anæere, der boede i Byen, havde han ladet dræbe og derpaa givet sin Datter, Salomos Hustru den i Medgift.
(Farao mfumu ya ku Igupto inali itathira nkhondo ndi kulanda Gezeri. Iye anatentha mzindawo. Anapha Akanaani amene ankakhala mʼmenemo ndipo kenaka anawupereka ngati mphatso yaukwati kwa mwana wake wamkazi amene anakwatiwa ndi Solomoni.
17 Nu genopbyggede Salomo Gezer), Nedre-Bet-Horon,
Ndipo Solomoni anamanganso Gezeri.) Iye anamanga Beti-Horoni Wakumunsi,
18 Ba'alat, Tamar i Ørkenen i Juda Land,
Baalati ndi Tadimori ku chipululu, mʼdziko lake lomwelo,
19 alle Salomos Forraadsbyer, Vognbyerne og Rytterbyerne, og alt andet, som Salomo fik Lyst til at bygge i Jerusalem, i Libanon og i hele sit Rige:
pamodzinso ndi mizinda yake yosungira chuma ndiponso mizinda yosungiramo magaleta ndi akavalo ake. Anamanganso chilichonse chimene anafuna kumanga ku Yerusalemu, ku Lebanoni ndi ku madera onse amene iye ankalamulira.
20 Alt, hvad der var tilbage af Amoriterne, Hetiterne, Perizziterne, Hivviterne og Jebusiterne, og som ikke hørte til Israeliterne,
Panali anthu amene anatsala pakati pa mitundu ya Aamori, Ahiti, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi (anthu awa sanali Aisraeli).
21 deres Efterkommere, som var tilbage efter dem i Landet, og som Israeliterne ikke havde været i Stand til at lægge Band paa, dem udskrev Salomo til Hoveriarbejde, som det er den Dag i Dag.
Zimenezi ndiye zinali zidzukulu zawo zotsalira mʼdzikoli, anthu amene Aisraeli sanathe kuwawononga kotheratu. Solomoni anawatenga ndi kukhala akapolo ake ogwira ntchito yathangata, monga zilili mpaka lero lino.
22 Af Israeliterne derimod satte Salomo ingen til Arbejde, men de var Krigsfolk og Hoffolk, Hærførere og Høvedsmænd hos, ham og Førere for hans Stridsvogne og Rytteri. —
Koma Solomoni sanagwiritse ntchito ya ukapolo Mwisraeli aliyense; iwo anali anthu ake ankhondo, nduna zake, atsogoleri a ankhondo, akapitawo ake, olamulira magaleta ndi oyendetsa magaleta ake.
23 Tallet paa Overfogederne, der ledede Arbejdet for Salomo, var 550; de havde Tilsyn med Folkene, der arbejdede. —
Amenewa ndiwo anali akuluakulu oyangʼanira ntchito za Solomoni. Anthu okwana 550 ndiwo ankayangʼanira anthu amene ankagwira ntchitowo.
24 Faraos Datter var lige flyttet fra Davidsbyen ind i det Hus, han havde bygget til hende, da tog han fat paa at opføre Millo. —
Mwana wamkazi wa Farao atachoka mu Mzinda wa Davide, kupita ku nyumba ya mfumu imene Solomoni anamumangira, Solomoni anamanga malo achitetezo a Milo.
25 Tre Gange om Aaret ofrede Salomo Brændofre og Takofre paa det Alter, han havde bygget HERREN, og tændte Offerild for HERRENS Aasyn; og han fuldførte Templet.
Katatu pa chaka Solomoni ankapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pa guwa lansembe limene anamangira Yehova ndiponso ankafukiza lubani pamaso pa Yehova. Potero ankakwaniritsa zoyenera kuchitika mu Nyumba ya Yehova.
26 Kong Salomo byggede ogsaa Skibe i Ezjongeber, der ligger ved Elat ved det røde Havs Kyst i Edom;
Mfumu Solomoni anapanganso sitima zapamadzi ku Ezioni Geberi, malo amene ali pafupi ndi Eloti ku Edomu, mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.
27 og Hiram sendte sine Folk, befarne Søfolk, om Bord paa Skibene sammen med Salomos Folk.
Ndipo Hiramu anatumiza anthu ake oyendetsa sitima zapamadzi amene ankadziwa za pa nyanja kuti aziyendetsa pamodzi ndi anthu a Solomoni.
28 De sejlede til Ofir, hvor de hentede 420 Talenter Guld, som de bragte Kong Salomo.
Iwo anapita ku Ofiri ndipo anakatenga golide okwana makilogalamu 14,000, amene anamupereka kwa Mfumu Solomoni.

< Første Kongebog 9 >