< Zefanias 3 >
1 Ve den genstridige og besmittede, den Stad, som øver Undertrykkelse!
Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza, owukira ndi odetsedwa!
2 Den hører ikke paa nogen Røst, dep annammer ikke Tugt; den forlader sig ikke paa Herren, den holder sig ikke nær til sin Gud.
Sumvera aliyense, sulandira chidzudzulo. Sumadalira Yehova, suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.
3 Dens Fyrster i dens Midte ere brølende Løver; dens Dommere ere Aftenulve, som ikke levne et Ben til om Morgenen.
Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma, olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo, zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.
4 Dens Profeter ere letfærdige, troløse Mænd; dens Præster vanhellige Helligdommen, gøre Vold paa Loven.
Aneneri ake ndi odzikuza; anthu achinyengo. Ansembe ake amadetsa malo opatulika ndipo amaphwanya lamulo.
5 Herren er retfærdig i dens Midte, han gør ikke Uret; hver Morgen lader han sin Ret komme for Lyset, det fattes ikke derpaa; men den uretfærdige kender ikke til Skam.
Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama; Iye salakwa. Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama, ndipo tsiku lililonse salephera, komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.
6 Jeg udryddede Hedningerne, deres Hjørnetaarne ere ødelagte, jeg gjorde deres Gader øde, saa at ingen gaar igennem dem; deres Stæder ere forstyrrede, saa at der er ingen Mand der, og ingen bor der.
“Ndachotseratu mitundu ya anthu; ndagwetsa malinga awo. Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo, popanda aliyense wodutsa. Mizinda yawo yawonongedwa; palibe aliyense adzatsalemo.
7 Jeg sagde: Du skal kun frygte mig, annamme Tugt, saa skal dens Bolig ikke udryddes, alt eftersom jeg havde bestemt over den; men de have aarle gjort sig rede til at gøre alle deres Gerninger fordærvelige.
Ndinati, ‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa ndi kumvera kudzudzula kwanga!’ Ndipo sindidzawononga nyumba zawo, kapena kuwalanganso. Koma iwo anali okonzeka kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.
8 Derfor, bier efter mig, siger Herren, efter den Dag, da jeg rejser mig til Rov! thi min Ret er den, at jeg vil sanke Hedningerne, at jeg vil samle Rigerne, for over dem at udøse min Fortørnelse, al min brændende Vrede; thi ved min Nidkærheds Ild skal den hele Jord fortæres.
Choncho mundidikire,” akutero Yehova, “chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni. Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu, kusonkhanitsa maufumu ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo; mkwiyo wanga wonse woopsa. Dziko lonse lidzatenthedwa ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.
9 Thi da vil jeg omskifte Læberne til rene for Folkene, at de alle skulle paakalde Herrens Navn og tjene ham endrægtelig.
“Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova ndi kumutumikira Iye pamodzi.
10 Fra hin Side af Morlands Floder skulle de bringe mine Tilbedere, mit adspredte Folk, som en Gave til mig.
Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi anthu anga ondipembedza, omwazikana, adzandibweretsera zopereka.
11 Paa den Dag skal du ikke skamme dig ved nogen af dine Gerninger, med hvilke du forsyndede dig imod mig; thi da vil jeg borttage af din Midte dine stolte Pralere, og du skal ikke blive ved at ophøje dig ydermere paa mit hellige Bjerg.
Tsiku limenelo simudzachita manyazi chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira, popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo. Simudzakhalanso odzikuza mʼphiri langa lopatulika.
12 Men jeg vil lade et nedtrykt og ringe Folk blive tilovers i din Midte, og de skulle forlade sig paa Herrens Navn.
Koma ndidzasiya pakati panu anthu ofatsa ndi odzichepetsa, amene amadalira dzina la Yehova.
13 De overblevne af Israel skulle ikke gøre Uret og ikke tale Løgn, Og der skal ikke findes en svigefuld Tunge i deres Mund; thi de skulle finde Føde og Hvile, og ingen skal forfærde dem.
Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika; sadzayankhulanso zonama, ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo. Adzadya ndi kugona ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”
14 Syng, du Zions Datter! raab højt, o Israel! vær glad og fryd dig af dit ganske Hjerte, du Jerusalems Datter!
Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni; fuwula mokweza, iwe Israeli! Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!
15 Herren har borttaget Dommene over dig, har udryddet din Fjende; Herren, Israels Konge, er i din Midte, du skal ikke se Ulykke ydermere.
Yehova wachotsa chilango chako, wabweza mdani wako. Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako; sudzaopanso chilichonse.
16 Paa den Dag skal siges til Jerusalem: Frygt ikke! til Zion: Lad ikke dine Hænder synke!
Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti, “Usaope, iwe Ziyoni; usafowoke.
17 Herren din Gud i din Midte, din vældige, skal frelse; han skal glæde sig over dig med Fryd, han skal tie i sin Kærlighed, han skal juble over dig med Frydesang.
Yehova Mulungu wako ali pakati pako, ali ndi mphamvu yopulumutsa. Adzakondwera kwambiri mwa iwe, adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake, adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”
18 Dem, som vare bedrøvede, fordi de ikke kunde komme til Højtiden, dem vil jeg samle; fra dig vare de; Forhaanelse har hvilet som en Byrde over dem.
“Ndidzakuchotserani zowawa za pa zikondwerero zoyikika; nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.
19 Se, paa den Tid vil jeg skride ind imod alle, som plage dig; og jeg vil frelse den haltende og samle de fordrevne og sætte dem til Pris og til Navnkundighed i hele det Land, hvori de lede Skændsel.
Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi onse amene anakuponderezani; ndidzapulumutsa olumala ndi kusonkhanitsa amene anamwazika. Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.
20 Paa den Tid vil jeg lade eder komme, og det paa den Tid naar jeg sanker eder; thi jeg vil sætte eder til Navnkundighed og til Pris iblandt alle Folk paa Jorden, naar jeg omvender eders Fangenskab for eders Øjne, siger Herren.
Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani; pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu. Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu inu mukuona,” akutero Yehova.