< Zakarias 4 >

1 Og Engelen, som talte med mig, kom igen og vakte mig som en Mand, der opvækkes af sin Søvn.
Kenaka mngelo amene amayankhula nane anabwerera nandidzutsa, ngati mmene amadzutsira munthu amene ali mʼtulo.
2 Og han sagde til mig: Hvad ser du? og jeg sagde: Jeg ser, og se, en Lysestage hel af Guld, med dens Oliekar oven paa den, og dens syv Lamper paa den, syv Rør til hver af Lamperne, som ere oven paa den;
Anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ine ndikuona choyikapo nyale, chonse chagolide ndi mbale pamwamba pake ndi nyale zoyaka zisanu ndi ziwiri, iliyonse ili ndi zibowo zisanu ndi ziwiri zolowetsera zingwe zoyatsira.
3 og tvende Olietræer ved Siden af den: Eet paa den højre Side af Oliekarret, og eet paa dets venstre Side.
Ndiponso pambali pake pali mitengo ya olivi iwiri, umodzi uli kumanja kwa mbaleyo ndipo winawo kumanzere.”
4 Og jeg svarede og sagde til Engelen, som talte med mig, saaledes: Hvad betyde disse Ting, min Herre?
Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi nʼchiyani mbuye wanga?”
5 Og Engelen, som talte med mig, svarede og sagde til mig: Ved du ikke, hvad disse Ting betyde? og jeg sagde: Nej, min Herre!
Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ndinayankha kuti, “Ayi mbuye wanga.”
6 Da svarede han og sagde til mig: Dette er Herrens Ord til Serubabel, saa lydende: „Ikke ved Magt og ikke ved Styrke, men ved min Aand”, siger den Herre Zebaoth.
Choncho iye anandiwuza kuti, “Mawu a Yehova kwa Zerubabeli ndi awa: ‘Osati mwa nkhondo kapena ndi mphamvu, koma ndi Mzimu wanga,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
7 Hvo er du, du store Bjerg for Serubabels Ansigt? bliv til Slette! og han skal føre Slutstenen frem under Fryderaabene: Naade, Naade være over den!
“Kodi ndiwe yani, iwe phiri lamphamvu? Pamaso pa Zerubabeli udzasanduka dziko losalala. Pamenepo adzabweretsa mwala wotsiriza. Akamadzawuyika pamwamba anthu adzafuwula kuti, ‘Mulungu adalitse Nyumbayi! Mulungu adalitse Nyumbayi!’”
8 Og Herrens Ord kom til mig saalunde:
Ndipo Yehova anayankhulanso nane kuti,
9 Serubabels Hænder have lagt Grundvolden til dette Hus, og hans Hænder skulle fuldende det, paa det du skal fornemme, at den Herre Zebaoth har sendt mig til eder.
“Manja a Zerubabeli ndiwo ayika maziko a Nyumbayi; adzatsiriza ndi manja ake omwewo. Pamenepo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye anakutuma.
10 Thi hvo har foragtet ringe Tings Dag? og paa Blyloddet i Serubabels Haand skue med Glæde hine syv, nemlig Herrens Øjne, de fare om over hele Jorden.
“Ndani wanyoza tsiku la zinthu zazingʼono? Anthu adzasangalala akadzaona chingwe choyezera mʼmanja mwa Zerubabeli. (“Nyale zisanu ndi ziwirizi ndi maso a Yehova, amene amayangʼanayangʼana pa dziko lapansi.”)
11 Og jeg svarede og sagde til ham: Hvad betyde disse tvende Olietræer ved Lysestagens højre og ved dens venstre Side?
Kenaka ndinafunsa mngelo uja kuti, “Kodi mitengo ya olivi iwiri ili kumanja ndi kumanzere kwa choyikapo nyalechi ikutanthauza chiyani?”
12 Og jeg svarede anden Gang og sagde til ham: Hvad betyde de tvende Oliegrene, som ligge ind i de to gyldne Render, der udgyde Guld af sig?
Ndinamufunsanso kuti, “Kodi nthambi ziwiri za mtengo wa olivi zomwe zili pambali pa mipopi yodzera mafuta iwiri yagolide zikutanthauza chiyani?”
13 Og han sagde til mig: Ved du ikke, hvad disse betyde? og jeg sagde: Nej, min Herre!
Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ine ndinati, “Ayi mbuye wanga.”
14 Da sagde han: Disse ere de to Oliebørn, som staa for al Jordens Herre.
Choncho iye anati, “Amenewa ndi anthu awiri amene adzozedwa kuti atumikire Ambuye pa dziko lonse lapansi.”

< Zakarias 4 >