< Romerne 10 >

1 Brødre! mit Hjertes Ønske og Bøn til Gud for dem er om deres Frelse.
Abale, chokhumba cha mtima wanga ndi pemphero langa kwa Mulungu ndi chakuti Aisraeli apulumutsidwe.
2 Thi jeg giver dem det Vidnesbyrd, at de have Nidkærhed for Gud, men ikke med Forstand;
Popeza ndiwachitira umboni kuti ndi achangu pa zinthu za Mulungu koma osati mwachidziwitso.
3 thi da de ikke kendte Guds Retfærdighed og tragtede efter at opstille deres egen Retfærdighed, saa bøjede de sig ikke under Guds Retfærdighed.
Pakuti sanadziwe chilungamo chochokera kwa Mulungu ndipo anafuna kukhazikitsa chawochawo. Iwo sanagonjere chilungamo cha Mulungu.
4 Thi Kristus er Lovens Ende til Retfærdighed for hver den, som tror.
Khristu ndiye mathero amalamulo kuti aliyense amene akhulupirira akhale olungama pamaso pa Mulungu.
5 Moses skriver jo, at det Menneske, som gør den Retfærdighed, der er af Loven, skal leve ved den.
Mose akulemba motere zachilungamo cha malamulo, “Munthu amene achita zinthu izi adzakhala ndi moyo pozichita.”
6 Men Retfærdigheden af Tro siger saaledes: Sig ikke i dit Hjerte: Hvem vil fare op til Himmelen? nemlig for at hente Kristus ned;
Koma chilungamo cha chikhulupiriro chikuti, “Usanene mu mtima mwako kuti, ‘Kodi ndani amene akwere kumwamba?’” (ndiko, kukatsitsa Khristu)
7 eller: Hvem vil fare ned i Afgrunden? nemlig for at hente Kristus op fra de døde. (Abyssos g12)
“kapena ‘Ndani adzatsikira ku dziko la anthu akufa?’” (ndiko, kukamutenga Khristu kwa akufa). (Abyssos g12)
8 Men hvad siger den? Ordet er dig nær, i din Mund og i dit Hjerte, det er det Troens Ord, som vi prædike.
Nanga akuti chiyani? “Mawu ali pafupi ndi inu. Ali mʼkamwa mwanu ndi mu mtima mwanu.” Ndiwo mawu achikhulupiriro amene ife tikuwalalikira,
9 Thi dersom du med din Mund bekender Jesus som Herre og tror i dit Hjerte, at Gud oprejste ham fra de døde, da skal du blive frelst.
kuti ngati udzavomereza ndi pakamwa pako kuti, “Yesu ndiye Ambuye,” ndi kukhulupirira mu mtima mwako kuti Mulungu anamuukitsa kwa akufa, udzapulumuka.
10 Thi med Hjertet tror man til Retfærdighed, og med Munden bekender man til Frelse.
Pakuti ndi mtima wanu mukhulupirira ndi kulungamitsidwa, ndipo ndi pakamwa panu muvomereza ndi kupulumutsidwa.
11 Skriften siger jo: „Hver den, som tror paa ham, skal ikke blive til Skamme.”
Pakuti Malemba akuti, “Aliyense amene akhulupirira Iye, sadzachititsidwa manyazi.”
12 Thi der er ikke Forskel paa Jøde og Græker; thi den samme er alles Herre, rig nok for alle dem, som paakalde ham.
Pakuti palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina, pakuti Ambuye mmodzi yemweyo ndi Ambuye wa onse ndipo amadalitsa mochuluka onse amene ayitana pa Iye
13 Thi hver den, som paakalder Herrens Navn, skal blive frelst.
pakuti, “Aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.”
14 Hvorledes skulde de nu paakalde den, paa hvem de ikke have troet? og hvorledes skulde de tro den, som de ikke have hørt? og hvorledes skulde de høre, uden der er nogen, som prædiker?
Kodi adzayitana bwanji amene sanamukhulupirire? Ndipo adzakhulupirira bwanji asanamve za Iye? Ndipo adzamva bwanji popanda wina kulalikira kwa iwo?
15 og hvorledes skulde de prædike, dersom de ikke bleve udsendte? Som der er skrevet: „Hvor dejlige ere deres Fødder, som forkynde godt Budskab.”
Ndipo iwo adzalalikira bwanji osatumidwa? Kwalembedwa kuti, “Akongoladi mapazi a iwo amene amabweretsa Uthenga Wabwino!”
16 Dog ikke alle løde Evangeliet; thi Esajas siger: „Herre! hvem troede det, han hørte af os?”
Koma si onse amene anavomereza Uthenga Wabwino. Pakuti Yesaya akuti, “Ambuye, ndani amene wakhulupirira uthenga wathu?”
17 Altsaa kommer Troen af det, som høres, men det, som høres, kommer igennem Kristi Ord.
Motero, chikhulupiriro chimabwera pamene timva uthenga ndipo uthenga umamveka kuchokera ku mawu a Khristu.
18 Men jeg siger: Have de ikke hørt? Jo vist, „over hele Jorden er deres Røst udgaaet og til Jorderiges Grænser deres Ord.”
Koma ndikufunsa kuti kodi iwo anamva? Inde, iwo anamva kuti, “Liwu lawo linamveka ponseponse pa dziko lapansi. Mawu awo anafika ku malekezero a dziko lonse.”
19 Men jeg siger: Har Israel ikke forstaaet det? Først siger Moses: „Jeg vil gøre eder nidkære paa et Folk, som ikke er et Folk, imod et uforstandigt Folk vil jeg opirre eder.”
Ine ndifunsanso kuti, kodi Israeli sanazindikire? Poyamba Mose akuti, “Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake. Ine ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.”
20 Men Esajas drister sig til at sige: „Jeg blev funden af dem, som ikke søgte mig; jeg blev aabenbar for dem, som ikke spurgte efter mig.”
Ndipo Yesaya molimba mtima akuti, “Anandipeza anthu amene sanali kundifunafuna. Ndinadzionetsera kwa amene sanafunse za Ine.”
21 Men om Israel siger han: „Den hele Dag udstrakte jeg mine Hænder imod et ulydigt og genstridigt Folk.”
Koma zokhudzana ndi Aisraeli akuti, “Tsiku lonse ndinatambasulira manja anga kwa anthu osandimvera ndi okanika.”

< Romerne 10 >