< Salme 82 >

1 Gud staar i Guds Menighed; han dømmer midt iblandt Guder.
Salimo la Asafu. Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu; Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
2 Hvor længe ville I dømme Uret og anse de ugudeliges Personer? (Sela)
“Mudzateteza osalungama mpaka liti, ndi kukondera anthu oyipa?
3 Skaffer den ringe og den faderløse Ret; hjælper den elendige og den arme til Retfærdighed!
Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye; mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
4 Redder den ringe og den fattige; udfrier ham af de ugudeliges Haand!
Landitsani anthu ofowoka ndi osowa; apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
5 De skønne ikke og forstaa ikke, de vandre i Mørke; alle Jordens Grundpiller ryste.
“Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse. Amayendayenda mu mdima; maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
6 Jeg har sagt: I ere Guder, og I ere alle den Højestes Sønner.
“Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu, nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
7 Men I skulle dø som Mennesker, og som en af Fyrsterne skulle I falde.
Koma mudzafa ngati anthu wamba; mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
8 Gud! gør dig rede, døm Jorden; thi du skal tage Arv iblandt alle Hedninger.
Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi, pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.

< Salme 82 >