< Salme 72 >

1 Gud! giv Kongen dine Domme og Kongens Søn din Retfærdighed,
Salimo la Solomoni. Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo, Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
2 at han kan dømme dit Folk med Retfærdighed og dine elendige med Retvished.
Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo, anthu anu ozunzika mosakondera.
3 Lad Bjergene bære Fred for Folket og Højene ligesaa ved Retfærdigheden.
Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu, timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
4 Han skal skaffe de elendige iblandt Folket Ret, han skal frelse den fattiges Børn og knuse Voldsmanden.
Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu ndi kupulumutsa ana a anthu osowa; adzaphwanya ozunza anzawo.
5 De skulle frygte dig, saa længe Solen er til, og saa længe Maanen lyser, fra Slægt til Slægter.
Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse, nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
6 Han stige ned som Regn paa den slaaede Eng, som Draaber, der væde Jorden!
Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
7 I hans Dage blomstre den retfærdige og megen Fred, indtil Maanen ikke er mere!
Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika; chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.
8 Og han regerer fra Hav til Hav, og fra Floden indtil Jordens Ende!
Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
9 De, som bo i Ørken, skulle bøje sig for hans Ansigt, og hans Fjender skulle slikke Støv.
Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake ndipo adani ake adzanyambita fumbi.
10 Konger fra Tarsis og Øerne skulle bringe Skænk! Konger fra Skeba og Seba skulle fremføre Gave.
Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali adzabweretsa mitulo kwa iye, mafumu a ku Seba ndi Seba adzapereka mphatso kwa iyeyo.
11 Og alle Konger skulle tilbede for ham; alle Hedninger skulle tjene ham.
Mafumu onse adzamuweramira ndipo mitundu yonse idzamutumikira.
12 Thi han skal fri den fattige, som raaber, samt den elendige, som ingen Hjælper har.
Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira, wozunzika amene alibe wina womuthandiza.
13 Han skal spare den ringe og fattige og frelse de fattiges Sjæle.
Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa ndi kupulumutsa osowa ku imfa.
14 Han skal udløse deres Sjæl fra Undertrykkelse og fra Vold, og deres Blod skal være dyrebart for hans Øjne.
Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.
15 Og de skulle leve og give ham af Skebas Guld og altid bede for ham, love ham den ganske Dag.
Iye akhale ndi moyo wautali; golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye. Anthu amupempherere nthawi zonse ndi kumudalitsa tsiku lonse.
16 Der vorde Overflod af Korn i Landet paa Bjergenes Top; dets Frugt suse som Libanon, og Folk blomstre frem af Staden som Urter paa Jorden!
Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse; pamwamba pa mapiri pakhale tirigu. Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni; zichuluke ngati udzu wakuthengo
17 Hans Navn blive evindelig; saa længe Solen lyser, forplante sig hans Navn, og de skulle velsigne sig selv i ham, alle Hedninger skulle prise ham salig!
Dzina lake likhazikike kwamuyaya, lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa. Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye ndipo iwo adzamutcha iye wodala.
18 Lovet være den Herre Gud, Israels Gud, han, som ene gør underfulde Ting!
Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
19 Og lovet være hans Æres Navn evindelig; og al Jorden fyldes med hans Ære! Amen, ja, Amen!
Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake. Ameni ndi Ameni.
20 Davids, Isajs Søns Bønner have Ende.
Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.

< Salme 72 >