< Salme 7 >
1 En Skiggajon, af David, som han sang for Herren, over Benjaminiten Kus's Ord.
Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini. Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu; pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
2 Herre, min Gud! jeg tror paa dig, frels mig fra alle mine Forfølgere og red mig,
mwina angandikadzule ngati mkango, ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.
3 at han ikke som en Løve skal slide min Sjæl, ja, rive den bort, uden at der er nogen, som redder.
Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
4 Herre, min Gud! dersom jeg har gjort dette, dersom der er Uret i mine Hænder;
ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere, kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
5 dersom jeg har vederlagt den ondt, som holder Fred med mig, — og jeg har dog friet den, som var min Fjende uden Aarsag —;
pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira, lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi ndipo mundigoneke pa fumbi. (Sela)
6 saa forfølge Fjenden min Sjæl og gribe den og nedtræde mit Liv til Jorden og lade min Ære bo i Støvet! (Sela)
Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu; nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga. Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
7 Staa op, Herre! i din Vrede, hæv dig imod mine Fjenders Forbitrelse, og vaagn op mig til Hjælp; du har beskikket Ret.
Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani. Alamulireni muli kumwambako;
8 Og lad Folkenes Forsamling omringe dig, og op over den vend tilbage til det høje!
Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo. Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa, monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
9 Herren dømmer Folkene; døm mig, Herre! efter min Retfærdighed og efter min Oprigtighed, som er hos mig.
Inu Mulungu wolungama, amene mumasanthula maganizo ndi mitima, thetsani chiwawa cha anthu oyipa ndipo wolungama akhale motetezedwa.
10 Lad dog de ugudeliges Ondskab faa Ende, men stadfæst den retfærdige, du, som prøver Hjerter og Nyrer, retfærdige Gud!
Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba, amene amapulumutsa olungama mtima.
11 Mit Skjold er hos Gud, som frelser de oprigtige af Hjertet.
Mulungu amaweruza molungama, Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
12 Gud er en retfærdig Dommer og en Gud, som vredes hver Dag.
Ngati munthu satembenuka, Mulungu adzanola lupanga lake, Iye adzawerama ndi kukoka uta.
13 Dersom de ikke ville omvende sig, da skal han skærpe sit Sværd; han har spændt sin Bue og beredt den;
Mulungu wakonza zida zake zoopsa; Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.
14 og han har beredt dødelige Vaaben imod dem; sine Pile gør han brændende.
Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse. Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
15 Se, han undfanger Uret; og han er frugtsommelig med Misgerning og føder Løgn.
Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
16 Han har gravet en Grav og opkastet den; men han skal falde i Graven, som han gør.
Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini; chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.
17 Hans Misgerning skal komme tilbage paa hans Hoved, og hans Voldsfærd skal nedfare paa hans Isse. Jeg vil takke Herren efter hans Retfærdighed og lovsynge Herren den Højestes Navn.
Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake; ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.