< Salme 68 >

1 Til Sangmesteren, af David; en Psalme, en Sang.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Adzuke Mulungu, adani ake amwazikane; adani ake athawe pamaso pake.
2 Gud staar op, hans Fjender adspredes, og de, som hade ham, fly for hans Ansigt.
Monga momwe mphepo imachotsera utsi; Inu muwawulutsire kutali. Monga phula limasungunukira pa moto, oyipa awonongeke pamaso pa Mulungu.
3 Som Røg driver bort, vil du bortdrive dem; som Voks smelter for Ild, skulle de ugudelige omkomme for Guds Ansigt.
Koma olungama asangalale ndi kukondwera pamaso pa Mulungu; iwo akondwere ndi kusangalala.
4 Men de retfærdige skulle glædes, de skulle fryde sig for Guds Ansigt og juble med Glæde.
Imbirani Mulungu imbirani dzina lake matamando, mukwezeni Iye amene amakwera pa mitambo; dzina lake ndi Yehova ndipo sangalalani pamaso pake.
5 Synger for Gud, lovsynger hans Navn, baner Vej for ham, som farer frem igennem Ørkenen; Herren er hans Navn, og fryder eder for hans Ansigt.
Atate wa ana amasiye, mtetezi wa akazi amasiye, ndiye Mulungu amene amakhala mʼmalo oyera.
6 Faderløses Fader og Enkers Dommer er Gud i sin hellige Bolig.
Mulungu amakhazikitsa mtima pansi osungulumwa mʼmabanja, amatsogolera amʼndende ndi kuyimba; koma anthu osamvera amakhala ku malo owuma a dziko lapansi.
7 Gud lader de enlige bo i Huse, han udfører de bundne i Frihed; kun de genstridige bo i det fortørrede Land.
Pamene munatuluka kutsogolera anthu anu, Inu Mulungu, pamene munayenda kudutsa chipululu,
8 Gud! da du drog ud foran dit Folk, da du skred frem gennem Ørkenen (Sela)
dziko lapansi linagwedezeka, miyamba inakhuthula pansi mvula, pamaso pa Mulungu, Mmodzi uja wa ku Sinai. Pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israeli.
9 Da bævede Jorden, og Himlene dryppede for Guds Ansigt, hint Sinaj! for Guds, Israels Guds Ansigt.
Munapereka mivumbi yochuluka, Inu Mulungu; munatsitsimutsa cholowa chanu cholefuka.
10 En Regn af Gaver lod du strømme ned, o Gud! din Arv, som var træt, styrkede du.
Anthu anu anakhala mʼmenemo ndipo munapatsa anthu osauka zimene zinkawasowa chifukwa cha ubwino wanu Mulungu.
11 Din Hjord bosatte sig i Landet; du beredte det, Gud! for den elendige ved din Godhed.
Ambuye analengeza mawu, ndipo gulu linali lalikulu la iwo amene anapita kukawafalitsa;
12 Herren lader. Ordet udgaa; de Kvinder, som bringe glad Budskab, ere en stor Hær.
“Mafumu ndi ankhondo anathawa mwaliwiro; mʼmisasa anthu anagawana zolanda pa nkhondo.
13 Hærskarernes Konger fly, de fly; og hun, som bor i Huset, uddeler Bytte.
Ngakhale mukugona pakati pa makola a ziweto, mapiko a nkhunda akutidwa ndi siliva, nthenga zake ndi golide wonyezimira.”
14 Naar I ligge mellem Foldene, er det som en Dues Vinger, skjulte med Sølv, og hvis Vingefjedre ere indsprængte med Guldets gyldengrønne Glans.
Pamene Wamphamvuzonse anabalalitsa mafumu mʼdziko, zinali ngati matalala akugwa pa Zalimoni.
15 Naar den Almægtige spreder Konger derudi, da falder der Sne paa Zalmon.
Mapiri a Basani ndi mapiri aulemerero; mapiri a Basani, ndi mapiri a msonga zambiri.
16 Et Guds Bjerg er Basans Bjerg, et Bjerg med mange Tinder er Basans Bjerg.
Muyangʼaniranji mwansanje inu mapiri a msonga zambiri, pa phiri limene Mulungu analisankha kuti azilamulira, kumene Yehova mwini adzakhalako kwamuyaya?
17 Hvorfor se I Bjerge med de mange Tinder med Avind til det Bjerg, som Gud havde Lyst at bo paa? ja, Herren vil bo derpaa evindelig.
Magaleta a Mulungu ndi osawerengeka, ndi miyandamiyanda; Ambuye wabwera kuchokera ku Sinai, walowa mʼmalo ake opatulika.
18 Guds Vogne ere to Gange ti Tusinde, tusinde Gange tusinde; Herren er iblandt dem som paa Sinaj i Hellighed.
Pamene Inu munakwera mmwamba, munatsogolera a mʼndende ambiri; munalandira mphatso kuchokera kwa anthu, ngakhale kuchokera kwa owukira, kuti Inu Mulungu, mukhale kumeneko.
19 Du opfor i Højheden, du bortførte Fanger, du annammede Gaver iblandt Mennesker, ja, endog iblandt de genstridige, at du maa blive boende, o Herre, o Gud!
Matamando akhale kwa Ambuye, kwa Mulungu Mpulumutsi wathu amene tsiku ndi tsiku amasenza zolemetsa zathu.
20 Lovet være Herren fra Dag til Dag! lægger han os en Byrde paa, saa er Gud dog vor Frelse. (Sela)
Mulungu wathu ndi Mulungu amene amapulumutsa; Ambuye Wamphamvuzonse ndiye amene amatipulumutsa ku imfa.
21 Vi have en Gud, som er en Gud til Frelse, og hos den Herre, Herre ere Udgange fra Døden.
Ndithu Mulungu adzaphwanya mitu ya adani ake, zipewa za ubweya za iwo amene amapitiriza kuchita machimo awo.
22 Men Gud skal knuse sine Fjenders Hoved, dens haarrige Isse, som vandrer frem i sin Skyld.
Ambuye akunena kuti, “Ndidzawabweretsa kuchokera ku Basani; ndidzawabweretsa kuchokera ku nyanja zozama.
23 Herren sagde: Jeg vil føre dem tilbage fra Basan, jeg vil føre dem tilbage fra Havets Dybheder,
Kuti muviyike mapazi anu mʼmagazi a adani anu, pamene malilime a agalu anu akudyapo gawo lawo.”
24 paa det din Fod maa vade i Blod, og dine Hundes Tunge faa sin Del af Fjenderne.
Mayendedwe aulemu a anthu anu aonekera poyera, Inu Mulungu; mayendedwe olemekeza Mulungu wanga ndi Mfumu yanga yokalowa mʼmalo opatulika.
25 Gud! de saa dine Tog, min Guds, min Konges Tog i Hellighed.
Patsogolo pali oyimba nyimbo pakamwa, pambuyo pawo oyimba nyimbo ndi zipangizo; pamodzi ndi iwo pali atsikana akuyimba matambolini.
26 Foran gik Sangerne, bagefter de, som legede paa Strengeleg, midt imellem Pigerne, som sloge paa Tromme.
Tamandani Mulungu mu msonkhano waukulu; tamandani Yehova mu msonkhano wa Israeli.
27 Lover Gud i Forsamlingerne; lover Herren, I, som ere af Israels Kilde!
Pali fuko lalingʼono la Benjamini, kuwatsogolera, pali gulu lalikulu la ana a mafumu a Yuda, ndiponso pali ana a mafumu a Zebuloni ndi Nafutali.
28 Der er Benjamin, den lille, der herskede over dem, Judas Fyrster, som stenede dem, Sebulons Fyrster, Nafthalis Fyrster.
Kungani mphamvu zanu Mulungu; tionetseni nyonga zanu, Inu Mulungu, monga munachitira poyamba.
29 Din Gud har befalet dig at være stærk; styrk, o Gud! det, du har gjort os.
Chifukwa cha Nyumba yanu ku Yerusalemu, mafumu adzabweretsa kwa Inu mphatso.
30 Fra dit Tempel i Jerusalem skulle Konger fremføre dig Gave.
Dzudzulani chirombo pakati pa mabango, gulu la ngʼombe zazimuna pakati pa ana angʼombe a mitundu ya anthu. Mochititsidwa manyazi, abweretse mitanda ya siliva. Balalitsani anthu a mitundu ina amene amasangalatsidwa ndi nkhondo.
31 Skæld paa Dyret iblandt Rørene, de stærke Øksnes Hob med Folkekalvene, som nedkaste sig med Sølvstykker; han adspredte Folkene, som have Lyst til Strid.
Nthumwi zidzachokera ku Igupto; Kusi adzadzipereka yekha kwa Mulungu.
32 Fyrster skulle komme fra Ægypten; Morland skal hastelig udstrække sine Hænder til Gud.
Imbirani Mulungu Inu mafumu a dziko lapansi imbirani Ambuye matamando. (Sela)
33 I Riger paa Jorden! synger for Gud, lovsynger Herren (Sela)
Kwa Iye amene amakwera pa mitambo yakalekale ya mmwamba amene amabangula ndi mawu amphamvu.
34 ham, som farer i Himlenes Himle, som ere fra fordums Tid, se, han udgiver sin Røst, den mægtige Røst.
Lengezani za mphamvu za Mulungu, amene ulemerero wake uli pa Israeli amene mphamvu zake zili mʼmitambo.
35 Giver Gud Magten; hans Højhed er over Israel og hans Magt i Skyerne. Forfærdelig er du, o Gud! fra dine Helligdomme; Israels Gud, han giver Folket Kraft og Styrke; lovet være Gud!
Ndinu woopsa, Inu Mulungu mʼmalo anu opatulika; Mulungu wa Israeli amapereka mphamvu ndi nyonga kwa anthu ake. Matamando akhale kwa Mulungu!

< Salme 68 >