< Salme 43 >
1 Døm mig, o Gud! og udfør min Sag imod et umildt Folk; fra en falsk og uretfærdig Mand udfri mig!
Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu; ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza; mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.
2 Thi du er min Styrkes Gud, hvorfor har du forkastet mig? Hvorfor skal jeg gaa i Sørgeklæder, idet Fjenden trænger mig?
Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga. Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine? Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira, woponderezedwa ndi mdani?
3 Send dit Lys og din Sandhed, at de maa ledsage mig, at de maa føre mig til dit hellige Bjerg og til dine Boliger;
Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu kuti zinditsogolere; mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera, kumalo kumene inu mumakhala.
4 og at jeg maa indgaa til Guds Alter, til Gud, som er min Fryd og Glæde, og takke dig paa Harpe, o Gud, min Gud!
Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu, kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa. Ndidzakutamandani ndi zeze, Inu Mulungu wanga.
5 Hvorfor nedbøjer du dig, min Sjæl? og hvorfor bruser du i mit Indre? Bi efter Gud; thi jeg skal endnu takke ham, mit Ansigts Frelse og min Gud.
Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga? Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandabe Iye, Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.