< Salme 33 >

1 Synger med Fryd, I retfærdige, i Herren! Lovsang sømmer sig for de oprigtige.
Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
2 Takker Herren med Harpe; og leger for ham paa Psaltre med ti Strenge.
Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
3 Synger ham en ny Sang, leger lifligt paa Strengeleg med Frydeklang.
Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
4 Thi Herrens Ord er ret, og al hans Gerning er trofast.
Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
5 Han elsker Retfærdighed og Dom; Jorden er fuld af Herrens Miskundhed.
Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
6 Himlene ere gjorte ved Herrens Ord og al deres Hær ved hans Munds Aande.
Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
7 Han holder Vandet sammen i Havet som en Dynge; han lægger de dybe Vande i Forraadskamre.
Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
8 Al Jorden frygte Herren! alle Verdens Indbyggere bæve for ham!
Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
9 Thi han talte, og det skete; han bød, saa stod det der.
Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
10 Herren gjorde Hedningernes Raad til intet, han forstyrrede Folkenes Tanker.
Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
11 Herrens Raad bestaar evindelig, hans Hjertes Tanker fra Slægt til Slægt.
Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
12 Saligt er det Folk, hvis Gud Herren er, det Folk, som han udvalgte sig til Arv.
Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
13 Herren skuede ud fra Himmelen, han saa alle Menneskens Børn.
Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
14 Han saa ned fra sit Højsæde til alle Jordens Indbyggere.
kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
15 Han er den, som danner deres Hjerter til Hobe, som agter paa alle deres Gerninger.
Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
16 En Konge frelses ikke ved stor Magt, en vældig fries ikke ved stor Kraft.
Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
17 Hesten slaar fejl til Frelse og kan ikke redde ved sin store Styrke.
Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
18 Se, Herrens Øje er til dem, som ham frygte, som haabe paa hans Miskundhed,
Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
19 for at fri deres Sjæl fra Død og holde dem i Live i Hungersnøden.
kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
20 Vor Sjæl bier efter Herren, han er vor Hjælp og vort Skjold.
Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
21 Thi i ham glædes vort Hjerte; thi vi forlade os paa hans hellige Navn.
Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
22 Herre! din Miskundhed være over os, ligesom vi haabe paa dig!
Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.

< Salme 33 >