< Salme 32 >
1 Salig er den, hvis Overtrædelse er forladt, hvis Synd er skjult.
Salimo la Davide. Malangizo. Ngodala munthu amene zolakwa zake zakhululukidwa; amene machimo ake aphimbidwa.
2 Saligt er det Menneske, hvem Herren ikke tilregner Skyld, og i hvis Aand der ikke er Svig.
Ngodala munthu amene machimo ake Yehova sawawerengeranso pa iye ndipo mu mzimu mwake mulibe chinyengo.
3 Der jeg vilde tie, hentæredes mine Ben under min Jamren den ganske Dag.
Pamene ndinali chete, mafupa anga anakalamba chifukwa cha kubuwula kwanga tsiku lonse.
4 Thi din Haand laa Dag og Nat svar paa mig; min Livskraft svandt hen i Sommerens Tørhed. (Sela)
Pakuti usana ndi usiku dzanja lanu linandipsinja; mphamvu zanga zinatha monga nthawi yotentha yachilimwe. (Sela)
5 Jeg bekendte min Synd for dig og skjulte ikke min Misgerning, jeg sagde: „Jeg vil bekende mine Overtrædelser for Herren”, du forlod mig min Syndeskyld. (Sela)
Kotero ine ndinavomereza tchimo langa kwa Inu, sindinabise mphulupulu zanga. Ndinati, “Ine ndidzawulula zolakwa zanga kwa Yehova, ndipo Inu munandikhululukira mlandu wa machimo anga.” (Sela)
6 Derfor skal hver hellig bede til dig til den Stund, du findes; komme store Vandskyl, skulle de ikke naa til ham.
Choncho aliyense okhulupirika apemphere kwa Inuyo pomwe mukupezeka; ndithu pamene madzi amphamvu auka, sadzamupeza.
7 Du er mit Skjul, du bevarer mig for Angest; med Frelsens Jubel omgiver du mig. (Sela)
Inu ndi malo anga obisala; muzinditeteza ku mavuto ndipo muzindizinga ndi nyimbo zachipulumutso. (Sela)
8 Jeg vil undervise dig og lære dig den Vej, som du skal gaa; jeg vil raade dig ved mit Øje.
Ndidzakulangiza ndi kukuphunzitsa njira imene udzayendamo; ndidzakupatsa uphungu ndi kukuyangʼanira.
9 Værer ikke som Hest og Mule, der ikke have Forstand, hvis Prydelse er Tømme og Bidsel til at tvinge dem, naar de ikke ville komme nær til dig.
Usakhale ngati kavalo kapena bulu, zimene zilibe nzeru, koma ziyenera kuwongoleredwa ndi zitsulo za mʼkamwa ndi pamutu, ukapanda kutero sizibwera kwa iwe.
10 Den ugudelige har mange Smerter; men den, som forlader sig paa Herren, omgiver han med Miskundhed.
Zowawa ndi zambiri za anthu oyipa koma chikondi chosatha cha Yehova chimamuzinga munthu amene amadalira Iye.
11 Glæder eder i Herren og fryder eder, I retfærdige! og synger med Fryd alle I, som ere oprigtige i Hjertet!
Kondwerani mwa Yehova inu olungama; imbani, inu nonse amene muli owongoka mtima!