< Salme 19 >
1 Til Sangmesteren; en Psalme af David.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Zakumwamba zimalengeza za ulemerero wa Mulungu; thambo limalalikira ntchito za manja ake.
2 Himlene fortælle Guds Ære, og den udstrakte Befæstning forkynder hans Hænders Gerning.
Tsiku ndi tsiku zimayankhula mawu ambiri, usiku ndi usiku zimaonetsa poyera nzeru.
3 En Dag udgyder sin Tale til den anden, og en Nat kundgør den anden Vidskab.
Palibe kuyankhula, palibe mawu aliwonse; liwu lawo silimveka.
4 Der er ingen Tale og ej Ord, med hvilke deres Røst ej er hørt.
Koma uthenga wawo umapita pa dziko lonse lapansi, mawuwo amafika mpaka kumalekezero a dziko lapansi.
5 Deres Maalesnor er udgangen over al Jorden og deres Ord til Jorderiges Ende, han satte et Telt for Solen paa dem.
Dzuwa lili ngati mkwatibwi wobwera kuchokera ku nsanja yake, ngati katswiri wokondwerera kuthamanga pa mpikisano.
6 Og den gaar ud som en Brudgom af sit Brudekammer; den glæder sig som en Helt ved at løbe sin Bane.
Limatuluka kuyambira mbali ina ya thambo ndi kuzungulira mpaka mbali inanso; palibe chinthu chotha kupewa kutentha kwake.
7 Dens Udgang er fra Himmelens ene Ende, og dens Omgang indtil dens anden Ende, og intet er dækket for dens Hede.
Lamulo la Yehova ndi langwiro, kutsitsimutsa moyo. Maumboni a Yehova ndi odalirika, amapereka nzeru kwa wopanda nzeru.
8 Herrens Lov er fuldkommen, den vederkvæger Sjælen; Herrens Vidnesbyrd er trofast, det gør den vankundige viis.
Malangizo a Yehova ndi olungama, amapereka chimwemwe mu mtima. Malamulo a Yehova ndi onyezimira, amapereka kuwala.
9 Herrens Befalinger ere rette, de glæde Hjertet; Herrens Bud er rent, det oplyser Øjnene.
Kuopa Yehova ndiye chinthu changwiro, chimakhala mpaka muyaya. Maweruzo a Yehova ndi owona ndipo onse ndi olungama;
10 Herrens Frygt er ren, den bestaar evindelig; Herrens Domme ere Sandhed, de ere alle sammen retfærdige.
ndi a mtengowapatali kuposa golide, kuposa golide weniweni; ndi otsekemera kuposa uchi, kuposa uchi wochokera pa chisa chake.
11 De ere kosteligere end Guld, ja, end meget fint Guld, og sødere end Honning og Honningkage.
Mtumiki wanu amachenjezedwa nawo; powasunga pali mphotho yayikulu.
12 Ogsaa din Tjener bliver paamindet ved dem; naar man holder dem, da er der stor Løn.
Ndani angathe kudziwa zolakwa zake? Mundikhululukire zolakwa zanga zobisika.
13 Hvo mærker Vildfarelserne? rens du mig fra lønlig Brøst!
Muteteze mtumiki wanunso ku machimo ochita akudziwa; iwo asandilamulire. Kotero ndidzakhala wosalakwa, wopanda mlandu wa tchimo lalikulu.
14 Hold og din Tjener borte fra de hovmodige, at de ikke skulle herske over mig, da bliver jeg urokkelig og uden Skyld for store Overtrædelser. Lad min Munds Ord og mit Hjertes Betænkning være til Behag for dit Ansigt, Herre, min Klippe og min Genløser!
Mawu a mʼkamwa mwanga ndi zolingalira za mu mtima mwanga zikhale zokondweretsa pamaso panu, Inu Yehova, Thanthwe langa ndi Mpulumutsi wanga.