< Salme 146 >
Tamandani Yehova. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
2 Jeg vil love Herren, medens jeg lever, jeg vil synge min Gud Psalmer, medens jeg er til.
Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.
3 Forlader eder ikke paa Fyrster, paa et Menneskes Barn, hos hvem der ingen Frelse er.
Musamadalire mafumu, anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.
4 Hans Aand udfarer, han vender tilbage til sit Støv; paa den Dag er det forbi med hans stolte Anslag.
Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi; zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.
5 Salig er den, hvis Hjælp Jakobs Gud er, hvis Haab er til Herren hans Gud;
Wodala ndi amene thandizo lake ndi Mulungu wa Yakobo.
6 som gjorde Himmelen og Jorden, Havet og alt det, som der er i dem, han, som bliver Sandhed tro evindelig;
Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo; Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.
7 som skaffer dem Ret, der lide Vold, som giver de hungrige Brød; Herren løser de bundne.
Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala. Yehova amamasula amʼndende,
8 Herren aabner de blindes Øjne; Herren oprejser de nedbøjede; Herren elsker de retfærdige.
Yehova amatsekula maso anthu osaona, Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi, Yehova amakonda anthu olungama.
9 Herren bevarer de fremmede; han opholder faderløse og Enker, men forvender de ugudeliges Vej.
Yehova amasamalira alendo ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye, koma amasokoneza njira za anthu oyipa.
10 Herren skal regere evindelig, din Gud, o Zion! fra Slægt til Slægt. Halleluja!
Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya, Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse. Tamandani Yehova.