< Salme 144 >

1 Lovet være Herren, min Klippe! han, som lærer mine Hænder til Striden, mine Fingre til Krigen,
Salimo la Davide. Atamandike Yehova Thanthwe langa, amene amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; zala zanga kumenya nkhondo.
2 han, som er Miskundhed imod mig og min Befæstning, min faste Borg og min Befrier, mit Skjold og den, paa hvem jeg har forladt mig; han, som tvinger mit Folk under mig.
Iye ndiye Mulungu wanga wachikondi ndi malo anga otetezedwa, linga langa ndi mpulumutsi wanga, chishango changa mmene ine ndimathawiramo, amene amagonjetsa mitundu ya anthu pansi panga.
3 Herre! hvad er et Menneske, at du kendes ved ham? et Menneskes Barn, at du agter paa ham?
Inu Yehova, munthu nʼchiyani kuti mumamusamalira, mwana wa munthu kuti muzimuganizira?
4 Mennesket er ligt et Aandepust, hans Dage ere som en Skygge, der farer forbi.
Munthu ali ngati mpweya; masiku ake ali ngati mthunzi wosakhalitsa.
5 Herre! bøj dine Himle og far ned, rør ved Bjergene, saa at de ryge.
Ngʼambani mayiko akumwamba, Inu Yehova, ndipo tsikani pansi; khudzani mapiri kuti atulutse utsi.
6 Lad Lynet lyne og adspred dem, udskyd dine Pile og forfærd dem!
Tumizani zingʼaningʼani ndi kubalalitsa adani; ponyani mivi yanu ndi kuwathamangitsa.
7 Udræk dine Hænder fra det høje, udfri mig og red mig af de store Vande, af de fremmedes Haand,
Tambasulani dzanja lanu kuchokera kumwamba; landitseni ndi kundipulumutsa, ku madzi amphamvu, mʼmanja mwa anthu achilendo,
8 hvis Mund taler Falskhed, og hvis højre Haand er Løgnens højre Haand.
amene pakamwa pawo ndi podzala ndi mabodza, amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.
9 Gud! jeg vil synge dig en ny Sang, jeg vil synge Psalmer for dig til Psalteren med ti Strenge,
Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano Inu Mulungu; ndidzakuyimbirani nyimbo pa zeze wa nsambo khumi,
10 ham, som giver Konger Frelse, som udriver sin Tjener David fra det grumme Sværd!
kwa Iye amene amapambanitsa mafumu, amene amapulumutsa Davide mtumiki wake ku lupanga loopsa.
11 Udfri mig og red mig af de fremmedes Haand, hvis Mund taler Falskhed, og hvis højre Haand er Løgnens højre Haand,
Landitseni ndi kundipulumutsa, mʼmanja mwa anthu achilendo, amene pakamwa pawo ndi podzaza ndi mabodza, amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.
12 at vore Sønner maa være som Planter, der ere komne til Frodighed i deres Ungdom; vore Døtre som Hjørnepiller, der ere udhuggede efter Templets Stil;
Ndipo ana aamuna pa chinyamata chawo adzakhala ngati mbewu yosamalidwa bwino, ana athu aakazi adzakhala ngati zipilala zosemedwa bwino, zokongoletsera nyumba yaufumu.
13 at vore Forraadskamre maa være fulde, at de kunne frembyde baade det ene og det andet Slags; at vore Faar kunne føde tusinde, ja, ti Tusinde paa vore Gader;
Nkhokwe zathu zidzakhala zodzaza ndi zokolola za mtundu uliwonse. Nkhosa zathu zidzaswana miyandamiyanda pa mabusa athu.
14 at vore Øksne maa være kraftige, at der intet Brud og ingen Afgang maa være, ej heller Klagemaal paa vore Gader.
Ngʼombe zathu zidzanyamula katundu wolemera. Sipadzakhala mingʼalu pa makoma, sipadzakhalanso kupita ku ukapolo, mʼmisewu mwathu simudzakhala kulira chifukwa cha mavuto.
15 Saligt er det Folk, som det gaar saaledes; saligt er det Folk, hvis Gud Herren er!
Odala anthu amene adzalandira madalitso awa; odala anthu amene Mulungu wawo ndi Yehova.

< Salme 144 >