< Salme 137 >

1 Ved Babylons Floder, der sad vi, og vi græd, naar vi kom Zion i Hu.
Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni.
2 Paa Vidierne i Landet havde vi hængt vore Harper.
Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu,
3 Thi der begærede de, som holdt os fangne, at vi skulde synge; og de, som plagede os, begærede, at vi skulde være glade: „Synger for os af Zions Sange!”
pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
4 Hvorledes skulde vi synge Herrens Sang i et fremmed Land?
Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo?
5 Dersom jeg glemmer dig, Jerusalem, da glemme mig min højre Haand!
Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
6 Min Tunge hænge ved min Gane, hvis jeg ikke kommer dig i Hu, hvis jeg ikke ophøjer Jerusalem over min højeste Glæde.
Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu.
7 Herre! kom Edoms Børn i Hu efter, hvad de gjorde paa Jerusalems Dag, da de sagde: „Gører bart, gører bart indtil Grundvolden i den.”
Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!”
8 Babels Datter, du ødelagte! lyksalig den, som betaler dig din Løn for, hvad du lønnede os med.
Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira.
9 Lyksalig den, som griber og knuser dine spæde Børn imod Klippen.
Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.

< Salme 137 >