< Salme 128 >

1 Lyksalig hver den, som frygter Herren, som gaar paa hans Veje!
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Odala ndi onse amene amaopa Yehova, amene amayenda mʼnjira zake.
2 Thi du skal æde Frugten af dine Hænders Arbejde; lyksalig er du, og det gaar dig vel.
Udzadya chipatso cha ntchito yako; madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
3 Din Hustru er som et frugtbart Vintræ paa Siderne af dit Hus, dine Børn som Oliekviste omkring dit Bord.
Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka mʼkati mwa nyumba yako; ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi kuzungulira tebulo lako.
4 Se, saaledes skal den Mand velsignes, som frygter Herren.
Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa amene amaopa Yehova.
5 Herren skal velsigne dig fra Zion, og du skal se Jerusalems Lykke alle dit Livs Dage.
Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni masiku onse a moyo wako; uwone zokoma za Yerusalemu,
6 Og du skal se Børn af dine Børn! Fred være over Israel!
ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israeli.

< Salme 128 >