< Ordsprogene 1 >

1 Ordsprog af Salomo, Davids Søn, Israels Konge,
Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
2 for af dem at faa Visdom og Undervisning, for at forstaa Forstandens Ord;
Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
3 for at modtage Undervisning i Klogskab, modtage Ret og Retfærdighed og Retvished;
kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
4 for at give de uvidende Vid, de unge Kundskab og Kløgt.
Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
5 Hvo som er viis, høre til og gaa frem i Lærdom, og hvo som er forstandig, vinde Evne til at styre;
Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
6 for at forstaa Ordsprog og Gaader, Vismænds Ord og deres mørke Taler.
kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
7 Herrens Frygt er Begyndelse til Kundskab; Daarerne foragte Visdom og Undervisning.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
8 Hør, min Søn! din Faders Undervisning, og forlad ikke din Moders Lov;
Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
9 thi de ere en yndig Krans til dit Hoved og Kæder til din Hals.
Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
10 Min Søn! naar Syndere lokke dig, da samtyk ikke!
Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
11 Dersom de sige: Gak med os, vi ville lure efter Blod, vi ville efterstræbe den uskyldige, som er uden Sag;
Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
12 vi ville, som Dødsriget, sluge dem levende, ja hele og holdne, som de, der nedfare i Hulen; (Sheol h7585)
tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
13 vi ville finde alle Haande dyrebart Gods, vi ville fylde vore Huse med Rov;
Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
14 du skal tage din Lod iblandt os, vi ville alle sammen have een Pose:
Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
15 Min Søn! vandre ikke paa Vej med dem, hold din Fod tilbage fra deres Sti;
Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
16 thi deres Fødder haste til ondt, og de skynde sig for at udøse Blod;
Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
17 thi forgæves udspændes Garn for alle Fugles Øjne;
Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
18 og de lure paa deres eget Blod, de efterstræbe deres eget Liv.
Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
19 Saa ere enhvers Veje, som er hengiven til Gerrighed; den tager sine egne Herrers Liv.
Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
20 Visdommen raaber udenfor, den opløfter sin Røst paa Gaderne;
Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
21 paa Hjørnet af de befærdede Gader raaber den; ved Indgangene til Portene, i Staden, taler den sine Ord:
ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
22 Hvor længe ville I uvidende elske Uvidenhed, og Spotterne have Lyst til Spot, og Daarer hade Kundskab?
“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
23 Vender eder til min Revselse; se, jeg vil udgyde min Aand over eder, jeg vil kundgøre eder mine Ord.
Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
24 Efterdi jeg raabte, og I vægrede eder, jeg udrakte min Haand, og ingen gav Agt;
Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
25 og I lode alt mit Raad fare og vilde ikke vide af min Revselse:
Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
26 Saa vil jeg, jeg selv le i eders Ulykke, jeg vil spotte, naar det kommer, som I frygte for;
Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
27 naar det, som I frygte for, kommer som en Ødelæggelse, og eders Ulykke kommer som en Hvirvelvind, naar Angest og Trængsel kommer over eder:
Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
28 Da skulle de paakalde mig, men jeg skal ikke svare, de skulle søge mig, men ikke finde mig.
“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
29 Fordi de hadede Kundskab og udvalgte ikke Herrens Frygt,
Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
30 fordi de ikke vilde vide af mit Raad, men foragtede al min Revselse:
popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
31 Saa skulle de æde Frugten af deres Veje og blive mætte af deres egne Raad.
Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
32 Thi de uvidendes Frafald skal volde dem Død, og Daarers Tryghed skal ødelægge dem selv.
Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
33 Men hvo mig lyder, skal bo tryggelig og være rolig, uden Frygt for det onde.
Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”

< Ordsprogene 1 >