< Ordsprogene 7 >

1 Min Søn! bevar mine Ord, og gem mine Bud hos dig.
Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
2 Hold mine Bud, saa skal du leve, og min Lov som din Øjesten.
Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
3 Bind dem om dine Fingre, skriv dem paa dit Hjertes Tavle!
Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
4 Sig til Visdommen: Du er min Søster, og Forstanden kalde du din Kynding;
Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
5 for at den maa bevare dig fra en fremmed Kvinde, fra en ubekendt, som gør sine Ord glatte.
Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
6 Thi jeg saa ud af mit Hus's Vindu, igennem mit Gitter;
Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
7 og jeg saa iblandt de uerfarne, jeg blev var iblandt Sønnerne et ungt Menneske, som fattedes Forstand,
Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
8 og han gik forbi paa Gaden ved hendes Hjørne og skred frem ad Vejen til hendes Hus,
Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
9 i Tusmørket om Aftenen efter Dagen, midt i Natten og Mørket.
Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
10 Og se, en Kvinde mødte ham i Horesmykke og underfundig i Hjertet,
Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
11 støjende og ustyrlig, hendes Fødder kunne ikke blive i hendes Hus.
(Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
12 Stundom er hun ude, stundom paa Gaderne og lurer ved alle Hjørner.
Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
13 Og hun tog fat paa ham og kyssede ham, hun gjorde sit Ansigt frækt og sagde til ham:
Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
14 Der paalaa mig Takoffer, i Dag har jeg betalt mine Løfter;
“Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
15 derfor er jeg gaaet ud at møde dig, at søge dit Ansigt, og jeg har fundet dig.
Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
16 Jeg har redet mit Leje med Tæpper, med stribet Tøj af Garn fra Ægypten;
Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
17 jeg har overstænket min Seng med Myrra. Aloe og Kanel;
Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
18 kom, lader os beruse os i Kærlighed indtil Morgenen, lader os forlyste os i Elskov;
Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
19 thi Manden er ikke hjemme, han er faren lang Vej bort;
Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
20 han tog Pengeknuden med sig, han kommer hjem til Fuldmaanedagen.
Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
21 Hun bøjede ham med sin megen Overtalelse, tilskyndte ham med sine smigrende Læber.
Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
22 Hvo der hastelig gaar efter hende, kommer som Oksen til Slagterbænken og som i Fodlænken, der er til Daarens Tugtelse,
Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
23 indtil en Pil sønderskærer hans Lever; ligesom Fuglen skynder sig til Snaren og ved ikke, at det gælder dens Liv.
mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
24 Saa hører mig nu, I Børn! og agter paa min Munds Ord!
Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
25 Lad dit Hjerte ikke vige af til hendes Veje, lad dig ikke forvildes paa hendes Stier;
Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
26 thi mange ere de gennemborede, som hun har fældet, og mangfoldige alle de, hun har ihjelslaget.
Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
27 Hendes Hus ere Veje til Dødsriget; de gaa ned til Dødens Kamre. (Sheol h7585)
Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol h7585)

< Ordsprogene 7 >