< Ordsprogene 27 >
1 Ros dig ikke af den Dag i Morgen; thi du ved ikke, hvad Dagen vil føde.
Usamanyadire za mawa, pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
2 Lad en fremmed rose dig og ikke din egen Mund; en anden og ikke dine egne Læber!
Munthu wina akutamande, koma osati wekha; mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
3 Stenen er svar, og Sandet er tungt; men Daarens Fortørnelse er svarere end begge.
Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri, koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
4 Hidsighed er grum, og Vrede strømmer over; men hvo kan staa for Skinsyge?
Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa. Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
5 Aabenbar Irettesættelse er bedre end skjult Kærlighed.
Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino kuposa chikondi chobisika.
6 Saar af en Elsker ere vel mente, men den hadefuldes Kys ere rigelige.
Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino, koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
7 En mæt Sjæl vrager Honningkage; men alt besk er sødt for en hungrig Sjæl.
Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi, koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
8 Ligesom en Spurv, der flagrer om borte fra sin Rede, saa er en Mand, der vanker omkring borte fra sit Sted.
Munthu amene wasochera ku nyumba kwake, ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
9 Olie og Røgelse glæde Hjertet, og en Vens Sødhed glæder, naar den kommer fra hans Sjæls Raad.
Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima, ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
10 Forlad ikke din Ven og din Faders Ven, og gak ikke i din Broders Hus paa din Nøds Dag; bedre er en Nabo nær hos end en Broder langt borte.
Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako, ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto; mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
11 Vær viis, min Søn! og glæd mit Hjerte, paa det jeg kan svare den, som forhaaner mig.
Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga; pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
12 Den kloge saa Ulykken og skjulte sig; men de uerfarne gik frem og maatte bøde.
Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
13 Naar en gaar i Borgen for en fremmed, tag saa hans Klæder, og tag Pant af ham for den fremmede Kvindes Skyld.
Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
14 Hvo som velsigner sin Næste med høj Røst aarle om Morgenen, ham skal det regnes for en Forbandelse.
Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri, anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
15 Et vedholdende Tagdryp paa en Regndag og en trættekær Kvinde ligne hinanden.
Mkazi wolongolola ali ngati mvula yamvumbi.
16 Hver som søger at skjule hende, skjuler Vind, og hans højre Haand griber i Olie.
Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
17 Jern skærpes ved Jern, og en Mand skærpes over for hans Næstes Ansigt.
Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake, chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
18 Hvo, som bevarer et Figentræ, skal æde Frugt deraf, og hvo der tager Vare paa sin Herre, skal æres.
Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake, ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
19 Ligesom i Vandet Ansigt er imod Ansigt, saa er et Menneskes Hjerte imod et Menneske.
Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi, chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
20 Dødsriget og Afgrunden kunne ikke mættes, saa kunne og Menneskens Øjne ikke mættes. (Sheol )
Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol )
21 Diglen er til Sølvet og Ovnen til Guldet, og en Mand prøves efter, hvad han roser.
Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo, chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
22 Dersom du vilde støde en Daare i Morteren med Støderen midt iblandt Gryn, skal hans Daarskab dog ikke vige fra ham.
Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo ndi musi ngati chimanga, uchitsiru wakewo sudzachoka.
23 Du skal grant kende dine Faars Udseende; sæt din Hu til Hjordene!
Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili. Kodi usamalire bwino ziweto zako?
24 Thi Gods er ikke evindelig, og mon en Krone varer. Ira Slægt til Slægt?
Paja chuma sichikhala mpaka muyaya, ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
25 Naar Høet er bortført, saa lader Græsset sig se igen, og Urterne paa Bjergene sankes.
Pamene udzu watha, msipu nʼkumera; ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
26 Lammene ere til dine Klæder, og Bukke ere en Ager værd.
ana ankhosa adzakupatsani chovala ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
27 Og du har Gedemælk nok til Føde for dig, til Føde for dit Hus, og Livs Ophold til dine Piger.
Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri kuti muzidya inuyo ndi banja lanu ndi kudyetsa antchito anu aakazi.