< Ordsprogene 23 >
1 Naar du sidder til Bords hos en Hersker, da agt vel paa, hvad der staar for dit Ansigt,
Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
2 og at du sætter en Kniv paa din Strube, hvis du har Begærlighed.
ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
3 Fat ikke Lyst til hans Livretter, da det er bedragerisk Mad.
Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
4 Anstreng dig ikke for at blive rig, brug ej din Forstand dertil!
Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
5 Skulde du lade dine Øjne flyve efter det, da det ikke er der? thi det skal gøre sig Vinger som en Ørn, der flyver imod Himmelen.
Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
6 Æd ikke Brød hos den, der har et ondt Øje, og hav ikke Lyst til hans Livretter!
Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
7 Thi ligesom han tænker i sit Hjerte, saa er han; han siger til dig: Æd og drik; men hans Hjerte er ikke med dig.
paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
8 Din Mundfuld, som du har spist, skal du udspy og have spildt dine liflige Ord.
Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
9 Tal ikke for Daarens Øren; thi han foragter din Tales Klogskab.
Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
10 Flyt ikke det gamle Landemærke, og kom ikke paa de faderløses Agre!
Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
11 Thi deres Løser er stærk; han skal udføre deres Sag imod dig.
paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
12 Vend dit Hjerte til Undervisning og dine Øren til Kundskabs Ord!
Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
13 Vægre dig ikke ved at tugte den unge; thi slaar du ham med Riset, dør han ikke deraf.
Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
14 Du skal slaa ham med Riset og fri hans Sjæl fra Dødsriget. (Sheol )
Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol )
15 Min Søn! dersom dit Hjerte er viist, skal ogsaa mit Hjerte glæde sig,
Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
16 og mine Nyrer skulle fryde sig, naar dine Læber tale Retvished.
Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
17 Lad dit Hjerte ikke være misundeligt imod Syndere, men bliv hver Dag i Herrens Frygt!
Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
18 Thi kommer der en Eftertid, saa vil din Forhaabning ikke tilintetgøres.
Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
19 Hør du, min Søn! og bliv viis, og lad dit Hjerte gaa lige frem ad Vejen.
Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
20 Vær ikke iblandt Vindrankere, iblandt dem, som fraadse i Kød.
Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
21 Thi en Dranker og Fraadser skal blive fattig; og Søvn klæder en i Pjalter.
Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
22 Adlyd din Fader, som avlede dig, og foragt ikke din Moder, naar hun bliver gammel.
Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
23 Køb Sandhed, og sælg den ej, saa og Visdom, Lærdom og Forstand.
Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
24 Den retfærdiges Fader skal fryde sig; den, som avler en viis, skal glædes ved ham.
Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
25 Lad din Fader og din Moder glædes, og lad hende, som fødte dig, fryde sig!
Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
26 Min Søn! giv mig dit Hjerte, og lad dine Øjne have Behag i mine Veje.
Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
27 Thi Skøgen er en dyb Grav og den fremmede Kvinde en snæver Brønd.
Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
28 Hun ligger paa Lur som efter Rov og formerer Tallet paa de troløse iblandt Menneskene.
Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
29 Hvo har Ak? hvo har Ve? hvo har Trætter? hvo har Bekymring? hvo har Saar uden Skel? hvo har røde Øjne?
Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
30 De, som sidde længe ved Vinen, de, som gaa ind at prøve den stærke Drik.
Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
31 Se ikke til Vinen, hvor den er rød, hvor den perler i Bægeret; glat gaar den ned.
Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
32 Til sidst skal den bide som en Slange og stikke som en Basilisk;
Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
33 dine Øjne ville se efter fremmede Kvinder, og dit Hjerte vil tale forvendte Ting;
Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
34 og du vil blive som den, der sover midt paa Havet, og som den, der sover paa Toppen af Masten:
Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
35 „De sloge mig, det smertede mig ikke; de stødte mig, jeg fornam det ikke; naar skal jeg opvaagne? jeg vil søge den endnu engang.”
Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”