< 4 Mosebog 36 >

1 Og de Øverste for Fædrenehusene i Gileads Børns Slægt, hans, som var en Søn af Makir, Manasse Søn, af Josefs Børns Slægt, gik frem, og de talede for Mose Ansigt og for Fyrsternes Ansigt, dem, som vare de Øverste for Fædrenehusene blandt Israels Børn,
Atsogoleri a mabanja a fuko la Giliyadi, mwana wa Makiri, mwana wa Manase omwe anali ochokera ku fuko la ana a Yosefe anabwera ndi kuyankhula ndi Mose, atsogoleri ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli.
2 og de sagde: Herren har budet min Herre at give Israels Børn Landet til Arv ved Lod; og min Herre er befalet af Herren at give vor Broder Zelafehads Arv til hans Døtre;
Iwo anati, “Pamene Yehova analamula mbuye wanga kuti apereke dziko ngati cholowa kwa Aisraeli mwa maere, anakulamulani inu kupereka cholowa cha mʼbale wathu Zelofehadi kwa ana ake aakazi.
3 men blive de en af de Sønner, som høre til de andre Israels Børns Stammer, til Hustruer, da vil deres Arv gaa bort fra vore Fædres Arv og lægges til den Stamme, som de gaa over til, og gaa bort fra vor Arvs Lod;
Tsopano ngati akwatiwa ndi aamuna ochokera ku mafuko ena a mitundu ya Aisraeli, cholowa chawo chidzatengedwa kuchoka pa cholowa cha makolo athu ndipo adzachiwonjezera ku fuko limene akwatiwakolo. Ndipo gawo lina la cholowacho, lopatsidwa kwa ife lidzatengedwa.
4 og naar det bliver Jubelaar for Israels Børn, da lægges deres Arv til den Stammes Arv, som de gik over til; og dermed vil deres Arv gaa bort fra vore Fædres Stammes Arv.
Pamene chaka cha chikondwerero cha zaka makumi asanu, cha Aisraeli chafika, cholowa chawo chidzawonjezeredwa ku fuko limene iwo akwatiwako. Ndipo katundu wawo adzachotsedwa pa cholowa cha fuko la makolo athu.”
5 Og Mose bød Israels Børn efter Herrens Mund og sagde: Josefs Børns Stamme taler ret.
Tsono mwa lamulo la Yehova, Mose anapereka lamulo ili kwa Aisraeli: “Zimene ana a Yosefe akunena ndi zoona.
6 Dette er det Ord, som Herren byder om Zelafehads Døtre og siger: De maa vorde dem til Hustruer, som synes gode for deres Øjne, kun at de vorde dem til Hustruer, som ere af deres Fædres Stammes Slægtskab,
Izi ndi zimene Yehova akulamula kwa ana aakazi a Zelofehadi: Atha kukwatiwa ndi aliyense amene angakondweretsedwe naye koma zingakhale bwino atakwatiwa mʼfuko la abambo awo
7 at Israels Børns Arv ej skal komme omkring fra en Stamme til en anden; men hver iblandt Israels Børn skal hænge ved sine Fædres Stammes Arv.
kuti cholowa cha Israeli chisapite ku fuko lina, pakuti Mwisraeli aliyense ayenera kusunga cholowa cha fuko la makolo ake.
8 Og hver Datter af Israels Børns Stammer, som arver nogen Arv, skal vorde en af sin Faders Stammes Slægtskab til Hustru, paa det Israels Børn kunne arve hver sine Fædres Arv,
Mwana wamkazi aliyense amene adzalandira cholowa cha dziko la fuko lililonse la Israeli ayenera kukwatiwa ndi munthu wa fuko la abambo ake.
9 og at en Arv ikke skal komme omkring fra en Stamme til en anden Stamme; men Israels Børns Stammer skulle hænge hver ved sin Arv.
Cholowa chilichonse mu Israeli sichiyenera kupita ku fuko lina, popeza fuko lililonse la Israeli liyenera kusunga cholowa chimene linalandira.”
10 Som Herren havde befalet Mose, saa gjorde Zelafehads Døtre.
Choncho ana aakazi a Zelofehadi anachita monga Yehova analamulira Mose.
11 Og Mahela, Tirza og Hogla og Milka og Noa, Zelafehads Døtre, bleve deres Farbroders Sønners Hustruer.
Ana aakazi a Zelofehadi amene ndi Mahila, Tiriza, Hogila, Milika ndi Nowa, anakwatiwa ndi asuweni awo a ku mbali ya abambo awo.
12 Dem, som vare af Manasse Børns, Josefs Søns, Slægter, bleve de til Hustruer, og deres Arv blev hos deres Faders Slægtskabs Stamme.
Anakwatiwa mʼmafuko a zidzukulu za Manase mwana wa Yosefe, ndipo cholowa chawo chinakhalabe mʼfuko la abambo awo.
13 Disse ere de Bud og de Love, som Herren bød ved Mose for Israels Børn paa Moabiternes slette Marker, ved Jordanen over for Jeriko.
Awa ndi malamulo ndi malangizo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli kupyolera mwa Mose ku chigwa cha Mowabu mʼmbali mwa Yorodani, ku Yeriko.

< 4 Mosebog 36 >