< Matthæus 17 >
1 Og seks Dage derefter tager Jesus Peter og Jakob og hans Broder Johannes med sig og fører dem afsides op paa et højt Bjerg.
Patapita masiku asanu ndi limodzi Yesu anatenga Petro, Yakobo, ndi Yohane mʼbale wa Yakobo pa okha ndipo anakwera nawo pa phiri lalitali.
2 Og han blev forvandlet for deres Øjne, og hans Aasyn skinnede som Solen, men hans Klæder bleve hvide som Lyset.
Pamenepo Iye anasinthika maonekedwe ake pamaso pawo. Nkhope yake inawala ngati dzuwa ndipo zovala zake zinayera kuti mbuu.
3 Og se, Moses og Elias viste sig for dem og samtalede med ham.
Nthawi yomweyo Mose ndi Eliya anaonekera kwa iwo akuyankhulana ndi Yesu.
4 Da tog Peter til Orde og sagde til Jesus: „Herre! det er godt, at vi ere her; vil du, da lader os gøre tre Hytter her, dig en og Moses en og Elias en.”
Petro anati kwa Yesu, “Ambuye ndi bwino kuti ife tikhale pano. Ngati mufuna ndidzamanga misasa itatu umodzi wanu, wina wa Mose ndi wina wa Eliya.”
5 Medens han endnu talte, se, da overskyggede en lysende Sky dem; og se, der kom fra Skyen en Røst, som sagde: „Denne er min Søn, den elskede, i hvem jeg har Velbehag; hører ham!”
Iye akuyankhulabe, mtambo owala unawaphimba, ndipo mawu ochokera mu mtambo anati, “Uyu ndiye Mwana wanga amene ndimukonda ndipo ndikondwera naye kwambiri. Mumumvere Iye!”
6 Og da Disciplene hørte det, faldt de paa deres Ansigt og frygtede saare.
Ophunzira atamva zimenezi, anachita mantha nagwa pansi chafufumimba.
7 Og Jesus traadte hen og rørte ved dem og sagde: „Staar op, og frygter ikke!”
Ndipo Yesu anabwera nawakhudza nati, “Dzukani, musaope.”
8 Men da de opløftede deres Øjne, saa de ingen uden Jesus alene.
Atayangʼana, sanaone wina aliyense kupatula Yesu yekha.
9 Og da de gik ned fra Bjerget, bød Jesus dem og sagde: „Taler ikke til nogen om dette Syn, førend Menneskesønnen er oprejst fra de døde.”
Akutsika ku phiriko, Yesu anawalamula kuti, “Musawuze wina aliyense zimene mwaona, mpaka Mwana wa Munthu ataukitsidwa kwa akufa.”
10 Og hans Disciple spurgte ham og sagde: „Hvad er det da, de skriftkloge sige, at Elias bør først komme?”
Ophunzira anamufunsa Iye kuti, “Nanga nʼchifukwa chiyani aphunzitsi amalamulo amati Eliya ayenera kukhala woyamba kubwera?”
11 Og han svarede og sagde: „Vel kommer Elias og skal genoprette alting.
Yesu anayankha kuti, “Kunena zoona, Eliya adzayenera kubwera ndipo adzakonza zinthu zonse.
12 Men jeg siger eder, at Elias er allerede kommen, og de erkendte ham ikke, men gjorde med ham alt, hvad de vilde; saaledes skal ogsaa Menneskesønnen lide ondt af dem.”
Koma Ine ndikuwuzani inu kuti Eliya anabwera kale koma iwo sanamuzindikire ndipo anachita naye chilichonse chimene anafuna. Momwemonso iwo adzazunza Mwana wa Munthu.”
13 Da forstode Disciplene, at han havde talt til dem om Johannes Døberen.
Pamenepo ophunzira anazindikira kuti amawawuza za Yohane Mʼbatizi.
14 Og da de kom til Folkeskaren, kom en Mand til ham og faldt paa Knæ for ham og sagde:
Atafika ku gulu la anthu, munthu wina anamuyandikira Yesu ndi kugwada pamaso pake.
15 „Herre! forbarm dig over min Søn, thi han er maanesyg og lidende; thi han falder ofte i Ild og ofte i Vand;
Iye anati, “Ambuye, muchitireni chifundo mwana wanga akudwala matenda akugwa ndipo akuvutika kwambiri. Kawirikawiri iye amagwa pa moto kapena mʼmadzi.
16 og jeg bragte ham til dine Disciple, og de kunde ikke helbrede ham.”
Ine ndinabwera naye kwa ophunzira anu koma alephera kumuchiritsa.”
17 Og Jesus svarede og sagde: „O du vantro og forvendte Slægt! hvor længe skal jeg være hos eder, hvor længe skal jeg taale eder? Bringer mig ham hid!”
Yesu anayankha nati, “Haa, mʼbado wosakhulupirira ndi wokhota maganizo! Kodi ndidzakhala nanu mpaka liti? Ndidzapirira nanu mpaka liti? Bwera nayeni kwa Ine mnyamatayo.”
18 Og Jesus talte ham haardt til, og den onde Aand for ud af ham, og Drengen blev helbredet fra samme Time.
Yesu anadzudzula chiwandacho ndipo chinatuluka mwa mnyamatayo ndipo anachira nthawi yomweyo.
19 Da gik Disciplene til Jesus afsides og sagde: „Hvorfor kunde vi ikke uddrive den?”
Pamenepo ophunzira anabwera kwa Yesu mwamseri ndi kumufunsa kuti, “Chifukwa chiyani ife tinalephera kutulutsa chiwandacho?”
20 Og han siger til dem: „For eders Vantros Skyld; thi sandelig, siger jeg eder, dersom I have Tro som et Sennepskorn, da kunne I sige til dette Bjerg: Flyt dig herfra derhen, saa skal det flytte sig; og intet skal være eder umuligt.
Iye anayankha kuti, “Chifukwa inu muli ndi chikhulupiriro chachingʼono. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti ngati muli ndi chikhulupiriro monga kambewu ka mpiru, mukhoza kunena ndi phiri ili kuti, ‘Choka apa nupite apo,’ ndipo lidzachoka. Palibe kanthu kamene kadzakukanikani.
21 Men denne Slags farer ikke ud uden ved Bøn og Faste.”
Chiwanda cha mtundu uwu sichingachoke chabe koma ndi pemphero ndi kusala kudya.”
22 Og medens de vandrede sammen i Galilæa, sagde Jesus til dem: „Menneskesønnen skal overgives i Menneskers Hænder;
Atasonkhana pamodzi ku Galileya, Iye anawawuza kuti, “Mwana wa Munthu akupita kukaperekedwa mʼmanja mwa anthu.
23 og de skulle slaa ham ihjel, og paa den tredje Dag skal han oprejses.” Og de bleve saare bedrøvede.
Iwo adzamupha koma pa tsiku lachitatu adzaukitsidwa.” Ndipo ophunzira anadzazidwa ndi chisoni.
24 Men da de kom til Kapernaum, kom de, som opkrævede Tempelskatten, til Peter og sagde: „Betaler eders Mester ikke Skatten?”
Yesu ndi ophunzira ake atafika ku Kaperenawo, wolandira msonkho wa ku Nyumba ya Mulungu anabwera kwa Petro namufunsa kuti, “Kodi aphunzitsi anu sapereka msonkho wa Nyumba ya Mulungu?”
25 Han sagde: „Jo.” Og da han kom ind i Huset, kom Jesus ham i Forkøbet og sagde: „Hvad tykkes dig, Simon? Af hvem tage Jordens Konger Told eller Skat, af deres egne Sønner eller af de fremmede?”
Iye anayankha kuti, “Inde amapereka.” Petro atalowa mʼnyumba, Yesu ndiye anayamba kuyankhula. Ndipo anamufunsa kuti, “Ukuganiza bwanji Simoni, kodi mafumu a dziko lapansi amalandira msonkho kuchokera kwa ana awo kapena kwa ena?”
26 Og da han sagde: „Af de fremmede,” sagde Jesus til ham: „Saa ere jo Sønnerne frie.
Petro anayankha kuti, “Kuchokera kwa ena.” Yesu ananena kwa iye kuti, “Ndiye kuti ana sapereka.”
27 Men for at vi ikke skulle forarge dem, saa gaa hen til Søen, kast en Krog ud, og tag den første Fisk, som kommer op; og naar du aabner dens Mund, skal du finde en Stater; tag denne, og giv dem den for mig og dig!”
Koma kuti ife tisawakhumudwitse pita ku nyanja kaponye mbedza yako. Katenge nsomba imene ukayambe kuyikola; kayitsekule kukamwa ndipo ukapezamo ndalama. Katenge ndalamayo ndi kukapereka msonkho wanga ndi wanu.