< Matthæus 16 >
1 Og Farisæerne og Saddukæerne kom hen og fristede ham og begærede, at han vilde vise dem et Tegn fra Himmelen.
Afarisi ndi Asaduki anabwera kwa Yesu ndi kumuyesa pomufunsa kuti awaonetse chizindikiro chochokera kumwamba.
2 Men han svarede og sagde til dem: „Om Aftenen sige I: Det bliver en skøn Dag, thi Himmelen er rød;
Iye anayankha kuti, “Kunja kukamada, inu mumati, kudzakhala nyengo yabwino popeza thambo ndi lofiira.
3 og om Morgenen: Det bliver Storm i Dag, thi Himmelen er rød og mørk. Om Himmelens Udseende vide I at dømme, men om Tidernes Tegn kunne I det ikke.
Ndipo mmawa mumati, ‘Lero kudzakhala mvula yamphepo popeza thambo ndi lofiira ndi mitambo ya mvula.’ Inu mumadziwa kutanthauzira maonekedwe a thambo koma simungathe kutanthauzira zizindikiro za nthawi.
4 En ond og utro Slægt forlanger Tegn; men der skal intet Tegn gives den uden Jonas's Tegn.” Og han forlod dem og gik bort.
Mʼbado woyipa ndi wachigololo umafuna chizindikiro chodabwitsa koma palibe ngakhale chimodzi chidzapatsidwa kupatula chizindikiro cha Yona.” Pamenepo Yesu anawasiya nachoka.
5 Og da hans Disciple kom over til hin Side, havde de glemt at tage Brød med.
Koma atawoloka nyanja, ophunzira anayiwala kutenga buledi.
6 Og Jesus sagde til dem: „Ser til, og tager eder i Vare for Farisæernes og Saddukæernes Surdejg!”
Yesu anawawuza kuti, “Chenjerani, khalani tcheru ndi yisiti wa Afarisi ndi Asaduki.”
7 Men de tænkte ved sig selv og sagde: „Det er, fordi vi ikke toge Brød med.”
Iwo anakambirana pakati pawo za izi ndipo anati, “Ichi nʼchifukwa chakuti sitinatenge buledi aliyense.”
8 Men da Jesus mærkede dette, sagde han: „I lidettroende! hvorfor tænke I ved eder selv paa, at I ikke have taget Brød med?
Yesu atadziwa zokambirana zawo, anawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukukambirana zakuti, ‘mulibe buledi?’ Inu achikhulupiriro chochepa.
9 Forstaa I ikke endnu? Komme I heller ikke i Hu de fem Brød til de fem Tusinde, og hvor mange Kurve I da toge op?
Kodi inu simukumvetsetsabe? Kodi simukukumbukira za buledi musanu amene anadya anthu 5,000 ndi madengu amene munadzaza?
10 Ikke heller de syv Brød til de fire Tusinde, og hvor mange Kurve I da toge op?
Kapena buledi musanu ndi muwiri amene anadya anthu 4,000, nanga ndi madengu angati amene munadzaza?
11 Hvorledes forstaa I da ikke, at det ej var om Brød, jeg sagde det til eder? Men tager eder i Vare for Farisæernes og Saddukæernes Surdejg.”
Zitheka bwanji kuti inu simukumvetsetsa kuti Ine sindinkayankhula nanu za buledi? Koma inu chenjerani ndi yisiti wa Afarisi ndi Asaduki.”
12 Da forstode de, at han havde ikke sagt, at de skulde tage sig i Vare for Surdejgen i Brød, men for Farisæernes og Saddukæernes Lære.
Kenaka iwo anazindikira kuti Iye samawawuza kuti achenjere ndi yisiti wa buledi koma ndi chiphunzitso cha Afarisi ndi Asaduki.
13 Men da Jesus var kommen til Egnen ved Kæsarea Filippi, spurgte han sine Disciple og sagde: „Hvem sige Folk, at Menneskesønnen er?”
Yesu atafika ku chigawo cha Kaisareya Filipo, Iye anafunsa ophunzira ake kuti, “Kodi anthu amati Mwana wa Munthu ndi ndani?”
14 Men de sagde: „Nogle sige Johannes Døberen; andre Elias; andre Jeremias eller en af Profeterne.”
Iwo anayankha kuti, “Ena amati ndi Yohane Mʼbatizi; ena amati ndi Eliya; komanso ena amati Yeremiya kapena mmodzi wa aneneri.”
15 Han siger til dem: „Men I, hvem sige I, at jeg er?”
Iye anafunsa kuti, “Nanga inuyo mumati ndine yani?”
16 Da svarede Simon Peter og sagde: „Du er Kristus, den levende Guds Søn.”
Simoni Petro anayankha kuti, “Inu ndinu Khristu, Mwana wa Mulungu wamoyo.”
17 Og Jesus svarede og sagde til ham: „Salig er du, Simon Jonas's Søn! thi Kød og Blod har ikke aabenbaret dig det, men min Fader, som er i Himlene.
Yesu anati kwa iye, “Ndiwe wodala Simoni mwana wa Yona, popeza si munthu amene anakuwululira izi koma Atate anga akumwamba.
18 Saa siger jeg ogsaa dig, at du er Petrus, og paa denne Klippe vil jeg bygge min Menighed, og Dødsrigets Porte skulle ikke faa Overhaand over den. (Hadēs )
Ndipo Ine ndikuwuza iwe kuti ndiwe Petro ndipo pa thanthwe ili Ine ndidzamangapo mpingo wanga ndipo makomo a ku gehena sadzawugonjetsa. (Hadēs )
19 Og jeg vil give dig Himmeriges Riges Nøgler, og hvad du binder paa Jorden, det skal være bundet i Himlene, og hvad du løser paa Jorden, det skal være løst i Himlene.”
Ine ndidzakupatsa makiyi a Ufumu wakumwamba, ndipo chilichonse chimene iwe udzachimanga pansi pano chidzamangidwanso kumwamba.”
20 Da bød han sine Disciple, at de maatte ikke sige til nogen, at han var Kristus.
Pamenepo Iye anachenjeza ophunzira ake kuti asawuze wina aliyense kuti ndi Khristu.
21 Fra den Tid begyndte Jesus at give sine Disciple til Kende, at han skulde gaa til Jerusalem og lide meget af de Ældste og Ypperstepræsterne og de skriftkloge og ihjelslaas og oprejses paa den tredje Dag.
Kuyambira nthawi imeneyo Yesu anayamba kuwafotokozera ophunzira ake kuti Iye ayenera kupita ku Yerusalemu ndi kukazunzidwa kwambiri mʼmanja mwa akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo kuti ayenera kuphedwa, ndi kuti tsiku lachitatu adzaukitsidwa.
22 Og Peter tog ham til Side, begyndte at sætte ham i Rette og sagde: „Gud bevare dig, Herre; dette skal ingenlunde ske dig!”
Petro anamutengera Iye pambali nayamba kumudzudzula kuti, “Dzichitireni chifundo Ambuye, sizingachitike kwa Inu ayi.”
23 Men han vendte sig og sagde til Peter: „Vig bag mig, Satan! du er mig en Forargelse; thi du sanser ikke, hvad Guds er, men hvad Menneskers er.”
Yesu anatembenuka nati kwa Petro, “Choka pamaso panga Satana! Iwe ndi chokhumudwitsa kwa Ine; iwe suganizira zinthu za Mulungu koma zinthu za anthu.”
24 Da sagde Jesus til sine Disciple: „Vil nogen komme efter mig, han fornægte sig selv og tage sit Kors op og følge mig!
Pamenepo Yesu anati kwa ophunzira ake, “Ngati wina aliyense abwera pambuyo panga ayenera kudzikana ndi kutenga mtanda wake ndi kunditsata Ine.
25 Thi den, som vil frelse sit Liv, skal miste det; men den, som mister sit Liv for min Skyld, skal bjærge det.
Pakuti aliyense amene afuna kupulumutsa moyo wake adzawutaya koma aliyense amene ataya moyo wake chifukwa cha Ine adzawupeza.
26 Thi hvad gavner det et Menneske, om han vinder den hele Verden, men maa bøde med sin Sjæl? Eller hvad kan et Menneske give til Vederlag for sin Sjæl?
Kodi munthu adzapindula chiyani ngati atapeza zonse za dziko lapansi nataya moyo wake? Kapena munthu angapereke chiyani chosinthana ndi moyo wake?
27 Thi Menneskesønnen skal komme i sin Faders Herlighed med sine Engle; og da skal han betale enhver efter hans Gerning.
Pakuti Mwana wa Munthu adzabwera mu ulemerero wa Atate ake ndi angelo ake ndipo pamenepo Iye adzapereka mphotho kwa munthu mofanana ndi zimene anachita.
28 Sandelig, siger jeg eder, der er nogle af dem, som staa her, der ingenlunde skulle smage Døden, førend de se Menneskesønnen komme i sit Rige.”
“Ine ndikuwuzani inu choonadi, ena amene akuyimirira pano sadzalawa imfa asanaone Mwana wa Munthu akudza mu ufumu.”