< Markus 9 >

1 Og han sagde til dem: „Sandelig, siger jeg eder, der er nogle af dem, som staa her, der ingenlunde skulle smage Døden, førend de se Guds Rige være kommet med Kraft.‟
Ndipo anawawuza kuti, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti ena amene ayimirira pano sadzafa asanaone ufumu wa Mulungu ukubwera mwa mphamvu.”
2 Og seks Dage derefter tager Jesus Peter og Jakob og Johannes med sig og fører dem alene afsides op paa et højt Bjerg, og han blev forvandlet for deres Øjne.
Patatha masiku asanu ndi limodzi Yesu anatenga Petro, Yakobo ndi Yohane nawatsogolera kupita ku phiri lalitali, kumene anali okhaokha. Kumeneko maonekedwe ake anasinthika pamaso pawo.
3 Og hans Klæder bleve skinnende, meget hvide, saa at ingen Blegemand paa Jorden kan gøre Klæder saa hvide.
Zovala zake zinawala monyezimira kwambiri, kotero kuti palibe sopo wina aliyense amene angaziyeretse monyezimira chotere pa dziko la pansi.
4 Og Elias tillige med Moses viste sig for dem, og de samtalede med Jesus.
Ndipo anaonekera Eliya ndi Mose pamaso pawo, amene ankayankhulana ndi Yesu.
5 Og Peter tog til Orde og siger til Jesus: „Rabbi! det er godt, at vi ere her, og lader os gøre tre Hytter, dig en og Moses en og Elias en.‟
Petro anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, ndi kwabwino kuti ife tili pano. Tiyeni timange misasa itatu; umodzi wanu, wina wa Mose ndi wina wa Eliya.”
6 Thi han vidste ikke, hvad han skulde sige; thi de vare blevne helt forfærdede.
(Iye sanadziwe choti anene, anali ndi mantha akulu).
7 Og der kom en Sky, som overskyggede dem; og en Røst kom fra Skyen: „Denne er min Søn, den elskede, hører ham!‟
Pamenepo mtambo unaoneka ndi kuwaphimba, ndipo mawu anamveka kuchokera mu mtambo kuti, “Uyu ndi Mwana wanga wokondedwa. Mvereni Iye!”
8 Og pludseligt, da de saa sig om, saa de ingen mere uden Jesus alene hos dem.
Mwadzidzidzi, atayangʼanayangʼana, sanaonenso wina aliyense ali ndi iwo kupatula Yesu.
9 Og da de gik ned fra Bjerget, bød han dem, at de ikke maatte fortælle nogen, hvad de havde set, førend Menneskesønnen var opstanden fra de døde.
Pamene ankatsika kuchokera ku phiri, Yesu anawalamulira kuti asawuze aliyense zimene anaona mpaka Mwana wa Munthu atauka kwa akufa.
10 Og de fastholdt dette Ord hos sig selv og spurgte hverandre, hvad det er at opstaa fra de døde.
Iwo anayisunga nkhaniyo nakambirana za tanthauzo lake la “Kuuka kwa akufa.”
11 Og de spurgte ham og sagde: „De skriftkloge sige jo, at Elias bør først komme?‟
Ndipo anamufunsa Iye kuti, “Nʼchifukwa chiyani aphunzitsi amalamulo amati Eliya ayenera kuyamba wabwera?”
12 Men han sagde til dem: „Elias kommer først og genopretter alting; og hvorledes er der skrevet om Menneskesønnen? At han skal lide meget og foragtes.
Yesu anayankha kuti, “Kunena motsimikiza, Eliya ayeneradi kuyamba kubwera kudzakonzanso zinthu zonse. Nʼchifukwa chiyani tsono zinalembedwa, kuti Mwana wa Munthu ayenera kuvutika kwambiri ndi kukanidwa?
13 Men jeg siger eder, at baade er Elias kommen, og de gjorde ved ham alt, hvad de vilde, efter som der er skrevet om ham.‟
Koma ndikuwuzani, kuti Eliya wabweradi, ndipo amuchitira iye zonse zimene iwo anafuna, monga momwe zalembedwera za iye.”
14 Og da de kom til Disciplene, saa de en stor Skare omkring dem og skriftkloge, som tvistedes med dem.
Atafika kwa ophunzira ena aja, anaona gulu lalikulu la anthu litawazungulira ndi aphunzitsi amalamulo akutsutsana nawo.
15 Og straks studsede hele Skaren, da de saa ham, og de løb hen og hilsede ham.
Nthawi yomweyo anthu onse atamuona, anadabwa kwambiri ndipo anathamanga kukamulonjera.
16 Og han spurgte dem: „Hvorom tvistes I med dem?‟
Iye anafunsa kuti, “Mukukangana nawo chiyani iwowa?”
17 Og en af Skaren svarede ham: „Mester! jeg har bragt min Søn til dig; han har en maalløs Aand.
Munthu wina mʼgululo anayankha kuti, “Aphunzitsi, ndinakubweretserani mwana wanga wamwamuna, amene ndi ogwidwa ndi mzimu umene umamulepheretsa kuyankhula.
18 Og hvor som helst den griber ham, slider den i ham, og han fraader og skærer Tænder, og han visner hen; og jeg har sagt til dine Disciple, at de skulde uddrive den, og de kunde ikke.‟
Nthawi iliyonse ukamugwira umamugwetsa pansi. Amatuluka thovu kukamwa, amakukuta mano ake ndipo amawuma. Ndinapempha ophunzira anu kuti awutulutse mzimuwo, koma sanathe.”
19 Men han svarede dem og sagde: „O du vantro Slægt! hvor længe skal jeg være hos eder, hvor længe skal jeg taale eder? Bringer ham til mig!‟
Yesu anayankha kuti, “Haa! Mʼbado osakhulupirira, kodi ndidzakhala nanu mpaka liti? Mubweretseni kwa Ine mnyamatayo.”
20 Og de ledte ham frem til ham; og da han saa ham, sled Aanden straks i ham, og han faldt om paa Jorden og væltede sig og fraadede.
Ndipo anamubweretsa kwa Iye. Mzimu woyipawo utaona Yesu, nthawi yomweyo unamukomola mnyamatayo. Anagwa pansi ndi kumagubuduka, ndi kuchita thovu kukamwa.
21 Og han spurgte hans Fader: „Hvor længe er det siden, at dette er kommet over ham?‟ Men han sagde: „Fra Barndommen af;
Yesu anafunsa abambo a mnyamatayo kuti, “Kodi wakhala chotere nthawi yayitali bwanji?” Iye anayankha kuti, “Kuyambira ali wamngʼono,
22 og den har ofte kastet ham baade i Ild og i Vand for at ødelægge ham; men om du formaar noget, da forbarm dig over os, og hjælp os!‟
wakhala ukumuponya pa moto kapena mʼmadzi kuti umuphe. Koma ngati mungathe kuchita kanthu, tichitireni chifundo ndipo mutithandize.”
23 Men Jesus sagde til ham: „Om du formaar! Alle Ting ere mulige for den, som tror.‟
Yesu anati, “‘Ngati mungathe!’ Zinthu zonse ndi zotheka kwa iye amene akhulupirira.”
24 Straks raabte Barnets Fader og sagde med Taarer: „Jeg tror, hjælp min Vantro!‟
Nthawi yomweyo abambo a mwanayo anafuwula kuti, “Ndikhulupirira; thandizani kusakhulupirira kwanga!”
25 Men da Jesus saa, at Skaren stimlede sammen, truede han den urene Aand og sagde til den: „Du maalløse og døve Aand! jeg byder dig, far ud af ham, og far ikke mere ind i ham!‟
Yesu ataona kuti gulu la anthu likuthamangira kumalowo, anadzudzula mzimu woyipawo kuti, “Iwe mzimu wolepheretsa kuyankhula ndi kumva, ndikulamulira tuluka mwa iye ndipo usadzalowenso.”
26 Da skreg og sled den meget i ham og for ud, og han blev ligesom død, saa at de fleste sagde: „Han er død.‟
Mzimuwo unafuwula ndi kumugubuduza kwambiri ndipo unatuluka. Mnyamatayo anaoneka ngati mtembo ndipo ambiri anati, “Wafa.”
27 Men Jesus tog ham ved Haanden og rejste ham op; og han stod op.
Koma Yesu anamugwira dzanja ndipo anamuyimiritsa, ndipo anayimirira.
28 Og da han var kommen ind i et Hus, spurgte hans Disciple ham i Enrum: „Hvorfor kunde vi ikke uddrive den?‟
Yesu atalowa mʼnyumba, ophunzira ake anamufunsa ali pa okha kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani ife sitinathe kutulutsa chiwandacho?”
29 Og han sagde til dem: „Denne Slags kan ikke fare ud ved noget, uden ved Bøn og Faste.‟
Iye anayankha kuti, “Mtundu uwu umatuluka pokhapokha mwapemphera ndi kusala kudya.”
30 Og da de gik ud derfra, vandrede de igennem Galilæa; og han vilde ikke, at nogen skulde vide det.
Anachoka malo amenewo nadutsa ku Galileya. Yesu sanafune kuti wina aliyense adziwe kumene anali,
31 Thi han lærte sine Disciple og sagde til dem: „Menneskesønnen overgives i Menneskers Hænder, og de skulle slaa ham ihjel; og naar han er ihjelslaaet, skal han opstaa tre Dage efter.‟
chifukwa amaphunzitsa ophunzira ake. Anati kwa iwo, “Mwana wa Munthu adzaperekedwa mʼmanja mwa anthu. Adzamupha, ndipo patatha masiku atatu adzauka.”
32 Men de forstode ikke det Ord og frygtede for at spørge ham.
Koma sanazindikire chimene amatanthauza, ndipo anachita mantha kuti amufunse.
33 Og de kom til Kapernaum, og da han var kommen ind i Huset, spurgte han dem: „Hvad var det, I overvejede med hverandre paa Vejen?‟
Anafika ku Kaperenawo. Pamene anali mʼnyumba, anawafunsa kuti, “Kodi mumatsutsana chiyani mʼnjira muja?”
34 Men de tav; thi de havde talt med hverandre paa Vejen om, hvem der var den største.
Koma anakhala chete chifukwa ali mʼnjira amatsutsana za kuti wamkulu kuposa onse ndani.
35 Og han satte sig og kaldte paa de tolv og siger til dem: „Dersom nogen vil være den første, han skal være den sidste af alle og alles Tjener.‟
Atakhala pansi, Yesu anayitana khumi ndi awiriwo nati, “Ngati wina aliyense afuna kukhala woyamba, ayenera kukhala wotsiriza ndi wotumikira onse.”
36 Og han tog et lille Barn og stillede det midt iblandt dem og tog det i Favn og sagde til dem:
Anatenga kamwana nakayimiritsa pakati pawo ndipo anawawuza kuti,
37 „Den, som modtager eet af disse smaa Børn for mit Navns Skyld, modtager mig; og den, som modtager mig, modtager ikke mig, men den, som udsendte mig.‟
“Aliyense wolandira mmodzi wa ana angʼono awa mʼdzina langa alandira Ine; ndipo aliyense wolandira Ine salandira Ine koma amene anandituma.”
38 Johannes sagde til ham: „Mester! vi saa en, som ikke følger os, uddrive onde Aander i dit Navn; og vi forbøde ham det, fordi han ikke følger os.‟
Yohane anati, “Aphunzitsi, tinaona munthu akutulutsa ziwanda mʼdzina lanu ndipo ife tinamuwuza kuti aleke, chifukwa sanali mmodzi wa ife.”
39 Men Jesus sagde: „Forbyder ham det ikke; thi der er ingen, som gør en kraftig Gerning i mit Navn og snart efter kan tale ilde om mig.
Yesu anati, “Musamuletse, palibe amene amachita chodabwitsa mʼdzina langa ndipo kenaka nanena zoyipa za Ine,
40 Thi den, som ikke er imod os, er for os.
pakuti aliyense amene satsutsana nafe ali mbali yathu.
41 Thi den, som giver eder et Bæger Vand at drikke i mit Navn, fordi I høre Kristus til, sandelig, siger jeg eder, han skal ingenlunde miste sin Løn.
Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti aliyense amene akupatsani chikho cha madzi mʼdzina langa chifukwa ndinu ake a Khristu, sadzataya konse mphotho yake.”
42 Og den, som forarger en af disse smaa, som tro, for ham var det bedre, at der laa en Møllesten om hans Hals, og han var kastet i Havet.
“Ndipo ngati wina aliyense achimwitsa mmodzi wa ana angʼono awa amene akhulupirira Ine, kukanakhala bwino kwa iye kuti aponyedwe mʼnyanja atamangiriridwa mwala waukulu mʼkhosi mwake.
43 Og dersom din Haand forarger dig, saa hug den af; det er bedre for dig at gaa som en Krøbling ind til Livet end at have to Hænder og fare til Helvede til den uudslukkelige Ild, (Geenna g1067)
Ngati dzanja lako likuchimwitsa, lidule. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa mʼmoyo ndi dzanja limodzi kusiyana ndi kukhala ndi manja awiri ndi kupita ku gehena, kumene moto wake suzima. (Geenna g1067)
44 [hvor deres Orm ikke dør, og Ilden ikke udslukkes.]
(Kumene mphutsi zake sizifa ndipo moto wake suzima).
45 Og dersom din Fod forarger dig, saa hug den af; det er bedre for dig at gaa lam ind til Livet end at have to Fødder og blive kastet i Helvede, (Geenna g1067)
Ndipo ngati phazi lako likuchimwitsa, lidule. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa mʼmoyo olumala kusiyana ndi kukhala ndi mapazi awiri ndi kuponyedwa mu gehena. (Geenna g1067)
46 [hvor deres Orm ikke dør, og Ilden ikke udslukkes.]
(Kumene mphutsi zake sizifa ndipo moto wake suzima).
47 Og dersom dit Øje forarger dig, saa riv det ud; det er bedre for dig at gaa enøjet ind i Guds Rige end at have to Øjne og blive kastet i Helvede, (Geenna g1067)
Ndipo ngati diso lako likuchimwitsa, likolowole. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa ufumu wa Mulungu ndi diso limodzi, kusiyana ndi kukhala ndi maso awiri ndi kuponyedwa mu gehena, (Geenna g1067)
48 hvor deres Orm ikke dør, og Ilden ikke udslukkes.
kumene “‘mphutsi zake sizifa ndipo moto wake suzima.’
49 Thi enhver skal saltes med Ild, og alt Offer skal saltes med Salt.
Aliyense adzayesedwa ndi moto.
50 Saltet er godt; men dersom Saltet bliver saltløst, hvormed ville I da give det sin Kraft igen? Haver Salt i eder selv, og holder Fred med hverandre!‟
“Mchere ndi wabwino, koma ngati utasukuluka, mungawukoleretsenso bwanji? Mukhale nawo mchere mwa inu nokha, ndipo mukhale pa mtendere wina ndi mnzake.”

< Markus 9 >