< Malakias 2 >
1 Og nu, denne Bestemmelse gælder eder, I Præster!
“Tsono chenjezo ili ndi la inu, inu ansembe.”
2 Dersom I ikke høre det, og dersom I ikke lægge det paa Hjerte at give mit Navn Ære, siger den Herre Zebaoth, da vil jeg sende Forbandelsen paa eder og forbande eders Velsignelser; ja, jeg har allerede forbandet dem, fordi I ikke ville lægge det paa Hjerte.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ngati simumvera, ndipo ngati simulemekeza dzina langa mʼmitima mwanu, ndidzakutembererani ndipo madalitso onse munawalandira ndidzawatemberera. Ndithu, ndawatemberera kale, chifukwa simunalemekeze Ine mʼmitima mwanu.”
3 Se, jeg truer Sæden for eder og spreder Møg over eders Ansigter, Møget af eders Festofre, og man skal bringe eder hen til dette.
“Ine ndidzalanga zidzukulu zanu chifukwa cha inu; ndidzakupakani kumaso ndowe za nsembe zanu zachikondwerero, ndipo ndidzakutayani pamodzi ndi ndowezo.”
4 Og I skulle fornemme, at jeg har sendt denne Bestemmelse imod eder, for at den skal vorde min Pagt med Levi, siger den Herre Zebaoth.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Apo mudzadziwa kuti Ine ndatumiza chenjezoli kuti pangano langa ndi Levi lipitirire.
5 Min Pagt var med ham, Livet og Freden, og jeg gav ham dem til Frygt, og han frygtede mig, og for mit Navn var han forfærdet.
Ine ndinali naye pa pangano, pangano lopatsa moyo ndi mtendere, ndipo ndinamupatsa zimenezi kuti azindiopa, ndipo anandiopadi ndi kulemekeza dzina langa.
6 Sandheds Lov var i hans Mund, og der blev ikke fundet Uret paa hans Læber; i Fred og i Oprigtighed vandrede han med mig og omvendte mange fra Misgerning.
Pakamwa pake pankatuluka malangizo woona, ndipo pa milomo yake sipanapezeke chinyengo. Iye anayenda nane mwamtendere ndi molungama mtima, ndipo anabweza anthu ambiri mʼnjira zawo zauchimo.
7 Thi en Præsts Læber skulle bevare Kundskab, og Loven skal man søge af hans Mund; thi han er den Herre Zebaoths Sendebud.
“Pakuti wansembe ayenera kukhala ndi chidziwitso, ndipo anthu ayenera kufunafuna malangizo kuchokera kwa iye, popeza iye ndi mthenga wa Yehova Wamphamvuzonse.
8 Men I ere afvegne fra Vejen, I have bragt mange til at støde an imod Loven; I have fordærvet Levis Pagt, siger den Herre Zebaoth.
Koma inu mwasiya njira yanga ndipo mwapunthwitsa anthu ambiri ndi ziphunzitso zanu; mwayipitsa pangano langa ndi Levi,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
9 Derfor gør ogsaa jeg eder foragtelige og ringe for alt Folket, eftersom I ikke agte paa mine Veje, men anse Personer ved Anvendelse af Loven.
“Choncho Ine ndachititsa kuti munyozedwe ndi kuchititsidwa manyazi pamaso pa anthu onse, chifukwa simunatsate njira zanga koma mwakhala mukuonetsa kukondera pa nkhani za malamulo.”
10 Have vi ikke alle sammen een Fader? har ikke een Gud skabt os? hvorfor handle vi troløst, den ene imod den anden, for at vanhellige vore Fædres Pagt?
Kodi sitili naye Atate mmodzi tonsefe? Kodi anatilenga si Mulungu mmodzi? Chifukwa chiyani tikudetsa pangano la makolo athu posamakhulupirirana wina ndi mnzake?
11 Juda har handlet troløst, og der er sket Vederstyggelighed i Israel og i Jerusalem; thi Juda har vanhelliget Herrens Helligdom, som han elsker, og taget til Ægte en fremmed Guds Datter.
Yuda waleka kukhulupirika. Chinthu chonyansa chachitika mu Israeli ndi mu Yerusalemu: Yuda wayipitsa malo opatulika amene Yehova amawakonda, pokwatira mkazi wopembedza mulungu wachilendo.
12 For den Mand, som gør dette, udrydde Herren den, som er vaagen, og den, som svarer, af Jakobs Telte, og den, som fremfører Offergaver til den Herre Zebaoth!
Ndipo wina aliyense wochita zimenezi, kaya munthuyo ndi wotani, Yehova amuchotse ku banja la Yakobo, ngakhale atabweretsa zopereka kwa Yehova Wamphamvuzonse.
13 For det andet gøre I ogsaa dette: I bedække Herrens Alter med Taarer, med Graad og Suk, saa at han ikke mere vender sit Ansigt til Offergaven eller modtager noget som velbehageligt af eders Haand.
China chimene mumachita ndi ichi: Mumakhathamiritsa guwa lansembe la Yehova ndi misozi. Mumalira ndi kufuwula kwambiri chifukwa Iye amakana kuyangʼana nsembe zanu, kapena kulandira mokondwera nsembe za mʼmanja mwanu.
14 Og I sige: Hvorfor? Fordi Herren har været Vidne imellem dig og din Ungdoms Hustru, som du har handlet troløst imod, da hun dog var din Ægtefælle og din Pagts Hustru.
Inu mukufunsa kuti, “Chifukwa chake nʼchiyani?” Chifukwa chake nʼchakuti Yehova ndi mboni ya pangano limene unachita ndi mkazi wa unyamata wako, chifukwa sunakhulupirike kwa iye, ngakhale kuti iyeyo ndiye mnzako, ndi mkazi wako mwapangano.
15 Og een, som havde en Rest af Aand, har ikke handlet saaledes. Men hvad gjorde den ene? Han søgte den af Gud forjættede Sæd. Saa skulle I vogte eder for eders Aands Skyld, og ingen handle troløst imod sin Ungdoms Hustru!
Kodi Yehova sanawalenge iwo ngati munthu mmodzi? Ndi ake mʼthupi ndi mu mzimu. Nʼchifukwa chiyani ali mmodzi? Chifukwa Iye amafuna ana opembedza Mulungu. Motero samala moyo wako wauzimu, ndipo usakhale wosakhulupirika kwa mkazi wa unyamata wako.
16 Thi jeg hader Skilsmisse, siger den Herre Israels Gud, og man bedækker derved sit Klædebon med Vold, siger den Herre Zebaoth; saa skulle I vogte eder for eders Aands Skyld og ikke handle troløst.
Yehova Mulungu wa Israeli akuti, “Ndimadana ndi kulekana ukwati. Ndimadana ndi munthu wochita zankhanza zotere kwa mkazi wake,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. Choncho tetezani mzimu wanu, ndipo musakhale osakhulupirika.
17 I have trættet Herren med eders Ord; og dog sige I: Hvormed have vi trættet ham? Idet I sige: Hver, som gør ondt, er god for Herrens Øjne, og til dem har han Lyst, eller: Hvor er Dommens Gud?
Mwamutopetsa Yehova ndi zoyankhula zanu. Inu mukufunsa kuti, “Kodi tamutopetsa bwanji?” Mwamutopetsa ponena kuti, “Aliyense amene amachita zoyipa ndi wabwino pamaso pa Yehova ndipo iye amakondwera naye” kapena pofunsa kuti, “Ali kuti Mulungu woweruza mwachilungamo?”