< 3 Mosebog 7 >
1 Og dette er Loven om Skyldofret; det er en højhellig Ting.
“‘Malamulo a nsembe yopepesera kupalamula imene ndi nsembe yopatulika kwambiri ndi awa:
2 Paa det Sted, hvor de skulle slagte Brændofret, skulle de slagte Skyldofret, og man skal stænke Blodet deraf paa Alteret rundt omkring.
Nsembe yopepesera machimo iziphedwa pamalo pomwe amaphera nsembe yopsereza ndipo awaze magazi ake mbali zonse za guwa.
3 Og alt Fedtet deraf skal man ofre, nemlig Stjerten og Fedtet, som skjuler Indvoldene,
Tsono apereke mafuta ake onse: mchira wamafuta ndi mafuta amene amakuta matumbo.
4 og de to Nyrer, og Fedtet, som er paa dem, det som er oven for Lænderne; og han skal udtage Hinden over Leveren tilligemed Nyrerne.
Aperekenso impsyo ziwiri, mafuta ake pamodzi ndi mafuta onse amene ali chamʼchiwuno, ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi.
5 Og Præsten skal gøre et Røgoffer af dem paa Alteret, som et Ildoffer for Herren; det er et Skyldoffer.
Wansembe azitenthe pa guwa kuti zikhale nsembe yotentha pa moto, yoperekedwa kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo lopalamula.
6 Alt Mandkøn iblandt Præsterne skal æde det, det skal ædes paa et helligt Sted; det er en højhellig Ting.
Munthu wamwamuna aliyense wa mʼbanja la wansembe angathe kudyako nsembeyo koma adyere ku malo opatulika. Imeneyi ndi nsembe yopatulika kwambiri.
7 Ligesom Syndofret er, saa skal og Skyldofret være, der er een Lov for dem; det skal høre den Præst til, som gør Forligelse derved.
“‘Nsembe yopepesera tchimo lopalamula ndi yofanana ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo. Ndipo nsembe ziwiri zonsezi zili ndi lamulo limodzi lokha. Wansembe amene wachita mwambo wa nsembe yopepesera machimo a kupalamula atenge nyamayo ngati yake.
8 Og den Præst, som ofrer nogens Brændoffer, den Præst skal Huden af det Brændoffer, han har ofret, høre til.
Wansembe wopereka nsembe yopsereza ya munthu wina aliyense, atenge chikopa cha nsembe yopserezayo kuti chikhale chake.
9 Og ethvert Madoffer, som er bagt i Ovnen, og ethvert, som er lavet i Kedelen eller i Panden, det skal høre den Præst til, som ofrer det.
Chopereka chilichonse cha chakudya chophika mu uvuni kapena chokazinga mu mʼphika kapena mu chiwaya ndi cha wansembe amene wapereka nsembezo.
10 Og ethvert Madoffer, som er blandet med Olie, eller som er tørt, skal høre alle Arons Børn til, den ene saavel som den anden.
Ndipo chopereka china chilichonse cha chakudya chosakaniza ndi mafuta kapena chowuma, chikhale cha ana onse a Aaroni ndipo anawo achigawane mofanana.
11 Og dette er Loven om Takofret, som man skal ofre for Herren.
“‘Malamulo a nsembe ya chiyanjano imene munthu angathe kupereka kwa Yehova ndi awa:
12 Vil man ofre det til Lovoffer, da skal man tillige med Lovofrets Slagtoffer bringe usyrede Kager blandede med Olie og usyrede tynde Kager, overstrøgne med Olie, og Mel, æltet til Kager, som ere blandede med Olie.
“‘Ngati munthuyo apereka chifukwa cha kuthokoza, apereke nsembeyo pamodzi ndi makeke wopanda yisiti, osakaniza ndi mafuta; timitanda ta buledi wopanda yisiti, topyapyala, topaka mafuta, ndiponso makeke a ufa wosalala wophikidwa bwino, wosakaniza ndi mafuta.
13 Tillige med Kager af syret Brød skal man bringe sit Offer, med Slagtofret, som hører til Takofrets Lovoffer.
Pamodzi ndi nsembe yachiyanjano yothokozerayo abwerenso ndi makeke opangidwa ndi yisiti ngati chopereka chake.
14 Og man skal ofre deraf et Stykke af hver Offergave som en Gave til Herren; det skal høre den Præst til, som stænker Takofrets Blod.
Munthuyo atenge mtanda umodzi pa mtanda wa buledi wa mtundu uliwonse kuti ukhale nsembe yopereka kwa Yehova. Tsono mtanda umenewo ndi wake wa wansembe amene awaze magazi a nsembe yachiyanjano.
15 Og Kødet af Slagtofret, som hører til nogens Takoffers Lovoffer, skal ædes paa hans Offers Dag; man skal intet lade blive deraf til om Morgenen.
Nyama ya nsembe yachiyanjano yothokozera idyedwe pa tsiku lomwe nsembeyo yaperekedwa ndipo isatsaleko mpaka mmawa.
16 Og dersom det Slagtoffer, som han ofrer, er et Løfteoffer eller et frivilligt Offer, da skal det ædes paa den samme Dag, han ofrer sit Offer, og den næste Dag skal det ædes, som levnes deraf.
“‘Koma ngati nsembe yakeyo apereka chifukwa cha lumbiro kapena mwaufulu, nsembeyo adye tsiku lomwe yaperekedwalo. Koma yotsala angathe kuyidya mmawa mwake.
17 Men hvad der levnes af Ofrets Kød, skal paa den tredje Dag opbrændes med Ild.
Ngati nyama ina ya nsembe yatsalabe mpaka tsiku lachitatu, imeneyo itenthedwe pa moto.
18 Og dersom der alligevel ædes af hans Takoffers Kød paa den tredje Dag, da bliver han ikke behagelig; den, som ofrede det, ham skal det ikke? regnes til gode, det skal være en Vederstyggelighed; og den, som æder deraf, skal bære sin Misgerning.
Ngati munthu adya nyama yachiyanjano pa tsiku lachitatu, nsembeyo sidzalandiridwa. Amene wayipereka nsembeyo Mulungu sadzamulandira ndipo nsembeyo idzakhala yonyansa pamaso pa Mulungu, yosamupindulira kanthu woperekayo.
19 Og det Kød, som rører ved noget urent, skal ikke ædes, det skal opbrændes med Ild, men hvad Kødet ellers angaar, maa enhver, som er ren, æde Kødet.
“‘Nyama imene yakhudza chilichonse chodetsedwa, munthu asayidye, koma itenthedwe pa moto. Aliyense amene ali woyeretsedwa angathe kudya nyama inayo.
20 Og hver den, som æder Kødet af Takofret, som hører Herren til, medens hans Urenhed er paa ham, den Person skal udryddes fra sit Folk.
Koma ngati munthu wina amene ndi wosayeretsedwa adya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, ameneyo achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.
21 Og naar nogen rører ved noget urent, ved et urent Menneske eller ved et urent Dyr eller ved nogen som helst uren Vederstyggelighed og æder af Takofrets Kød, som hører Herren til, da skal den Person udryddes fra sit Folk.
Ndipo ngati munthu wina akhudza chinthu chodetsedwa, kaya chonyansa cha munthu kapena cha nyama, kapenanso chonyansa china chilichonse, ndipo kenaka nʼkudya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati anthu a mtundu wake.’”
22 Og Herren talede til Mose og sagde:
Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
23 Tal til Israels Børn og sig: I skulle intet Fedt æde af Okse eller Lam eller Ged.
“Awuze Aisraeli kuti, ‘Musadye mafuta a ngʼombe, nkhosa kapenanso mbuzi.
24 Men Fedtet af Aadsel og Fedtet af det, som er revet, det maa benyttes til alle Haande Brug, men I skulle aldeles ikke æde det.
Mafuta a nyama yofa yokha, kapena mafuta a nyama yophedwa ndi zirombo akhoza kuwagwiritsa ntchito iliyonse, koma inu musadye mafuta amenewo.
25 Thi om nogen æder Fedtet af Dyr, af hvilke man skal ofre et Ildoffer for Herren, da skal den, som æder deraf, udryddes fra sit Folk.
Pakuti munthu wakudya mafuta a nyama yoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe yotentha pa moto, ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
26 Og I skulle intet Blod æde i alle eders Boliger, enten af Fugle eller af Dyr.
Ndipo kulikonse kumene mukakhale musakadye magazi a mbalame iliyonse kapena magazi a nyama iliyonse.
27 Enhver, som æder noget Blod, den Person skal udryddes fra sit Folk.
Ngati munthu aliyense adya magazi achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.’”
28 Og Herren talede til Mose og sagde:
Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
29 Tal til Israels Børn og sig: Hvo som vil ofre sit Takoffers Slagtoffer for Herren, han skal fremføre sit Offer for Herren, af sit Takoffers Slagtoffer.
“Awuze Aisraeli kuti, Aliyense amene apereka nsembe yachiyanjano kwa Yehova, abwere ndi gawo la nsembeyo kwa Yehova.
30 Hans Hænder skulle frembære Herrens Ildoffer; han skal frembære Fedtet tilligemed Brystet, Brystet, for at røre det med en Rørelse for Herrens Ansigt.
Atenge ndi manja ake zigawo za chopereka zoyenera kuzitentha pa moto ngati chopereka kwa Yehova. Abweretse mafuta, pamodzi ndi chidale chomwe, ndipo chidalecho achiweyule kuti chikhale chopereka choweyula kwa Yehova.
31 Og Præsten skal gøre et Røgoffer af Fedtet paa Alteret, men Brystet skal høre Aron og hans Sønner til.
Wansembe atenthe mafutawo pa guwa koma chidalecho chikhale cha Aaroni ndi ana ake.
32 Og I skulle give Præsten den højre Bov som Offergave, af eders Takoffers Slagtofre.
Mumupatse wansembe ntchafu ya kumanja ya nsembe yanu yachiyanjano kuti ikhale chopereka chanu kwa iye.
33 Den af Arons Sønner, som ofrer Blodet af Takofret og Fedtet, han skal have den højre Bov til Del.
Mwana wa Aaroni amene amapereka magazi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano, adzitenga ntchafu ya kumanja kukhala gawo lake.
34 Thi jeg har taget Brystet, som bliver rørt, og Boven, som bliver given, fra Israels Børn ud af deres Takofres Slagtofre og har givet Præsten Aron og hans Sønner dem, til en evig Rettighed af Israels Børn.
Choncho pa zopereka zachiyanjano za Aisraeli, Ine ndatengapo chidale chomwe amaweyula ndi ntchafu zimene amapereka nsembe ndipo ndazipereka kwa wansembe Aaroni ndi ana ake. Izi ndizo gawo lawo nthawi zonse pa zopereka za Aisraeli.”
35 Dette er Arons Salvelses og hans Sønners Salvelses Del af Herrens Ildofre, paa den Dag han førte dem frem for at gøre Præstetjeneste for Herren,
Zimenezi ndi chigawo cha Aaroni ndi ana ake chotapidwa pa zopereka kwa Yehova zoti zitenthedwe pa moto zimene zinaperekedwa pa tsiku limene anapatulidwa kuti akhale ansembe otumikira Yehova.
36 den, som Herren bød at skulle gives dem, paa den Dag han salvede dem, af Israels Børn, til en evig Rettighed hos deres Efterkommere.
Yehova ndiye analamulira kuti pa zopereka za Aisraeli azitapapo zimenezi ndi kuwapatsa ansembe ngati gawo lawo. Yehovayo analamula zimenezi pa tsiku limene ansembewo anapatulidwa ndipo anachikhazikitsa ngati lamulo la nthawi zonse.
37 Dette er Loven om Brændofret og om Madofret og om Syndofret og om Skyldofret og om Fyldelsesofret og om Takofret,
Awa ndi malamulo a nsembe izi: nsembe yopsereza, nsembe yachakudya, nsembe yopepesera machimo, nsembe yopepesera kupalamula, nsembe ya mwambo wodzoza ndi nsembe yachiyanjano.
38 som Herren befalede Mose paa Sinai Bjerg, paa: den Dag han befalede Israels Børn at ofre Herren deres Ofre, i Sinai Ørk.
Malamulo amenewa Yehova anapereka kwa Mose pa Phiri la Sinai pa tsiku limene Yehova analamulira Aisraeli kuti abwere ndi zopereka za kwa Yehova, ku chipululu cha Sinai kuja.