< Klagesangene 5 >

1 Herre! kom i Hu, hvad der er sket os; sku ned og se vor Forhaanelse!
Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
2 Vor Arv er gaaet over til fremmede, vore Huse til Udlændinge.
Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
3 Vi ere blevne faderløse, uden Fader, vore Mødre ere som Enker.
Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
4 Vandet, vi drikke, købe vi for Penge; vort Brænde kommer til os for Betaling.
Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
5 Man er os paa Halsen, vi forfølges; vi blive trætte og faa ikke Hvile.
Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
6 Vi have rakt Haanden imod Ægypten, imod Assyrien for at mættes af Brød.
Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
7 Vore Fædre have syndet, de ere ikke mere, og vi bære deres Misgerninger.
Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
8 Trælle herske over os; der er ingen, som frier af deres Haand.
Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
9 Vi hente vort Brød med Fare for vort Liv, formedelst Sværdet i Ørken.
Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
10 Vor Hud er forbrændt som en Ovn, af Hungerens Glød.
Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
11 De krænke Kvinderne i Zion, Jomfruerne i Judas Stæder.
Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
12 Fyrster ere hængte af deres Haand, Oldingers Person bliver ikke æret.
Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
13 Unge Karle maatte tage fat paa Kværnen, og Drenge segnede under Byrden af Ved.
Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
14 De Ældste have hørt op med at sidde i Porten, de unge Karle med deres Strengeleg.
Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
15 Vort Hjertes Glæde er hørt op, vor Dans er vendt om til Sorrig.
Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
16 Vort Hoveds Krone er affalden; o ve os! thi vi have syndet.
Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
17 Derfor er vort Hjerte sygt, derfor ere vore Øjne formørkede:
Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
18 For Zions Bjergs Skyld, som er øde, Ræve løbe derpaa.
pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
19 Du, Herre! du bliver evindelig, din Trone fra Slægt til Slægt.
Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
20 Hvorfor vil du glemme os evindelig? forlade os saa lang en Tid?
Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
21 Herre! før os tilbage til dig, saa ville vi vende tilbage, forny vore Dage som i fordums Tid!
Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
22 Thi mon du aldeles har forkastet os? mon du er saa saare vred paa os?
pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.

< Klagesangene 5 >