< Josua 7 >
1 Men Israels Børn forgrebe sig saare paa det bandlyste Gods; thi Akan, en Søn af Karmi, som var en Søn af Sabdi, Seras Søn, af Judas Stamme, tog af det bandlyste, og Herrens Vrede optændtes imod Israels Børn.
Koma Aisraeli anachita zachinyengo ndi lamulo lija loti asatenge kalikonse koyenera kuwonongedwa. Akani mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera, wa fuko la Yuda anatengako zinthu zina. Choncho Yehova anakwiyira Israeli kwambiri.
2 Og Josva udsendte Mænd fra Jeriko mod Ai, som ligger ved Beth-Aven Østen for Bethel, og sagde til dem: Gaar op og bespejder Landet; og Mændene gik op og bespejdede Ai.
Tsono Yoswa anatuma anthu kuchokera ku Yeriko kukazonda ku mzinda wa Ai umene uli pafupi ndi mzinda wa Beti-Aveni kummawa kwa Beteli, ndipo anawawuza kuti, “Pitani mukazonde chigawochi.” Anthuwo anapitadi kukazonda Ai.
3 Og de kom tilbage til Josva og sagde til ham: Lad ikke alt Folket drage op, lad ved to Tusinde Mand eller ved tre Tusinde Mand drage op og slaa Ai; du skal ikke lade det ganske Folk ulejlige sig derhen; thi de ere faa.
Atabwera kwa Yoswa, anamuwuza kuti, “Sikofunika kuti apite anthu onse kukathira nkhondo mzinda wa Ai. Mutumizeko anthu 2,000 kapena 3,000 kuti akatenge mzindawo. Musawatume anthu onse kumeneko popeza kuli anthu ochepa.”
4 Saa droge af Folket ved tre Tusinde Mænd op derhen; men de flyede for Ais Mænds Ansigt.
Choncho kunapita anthu 3,000. Koma iwo anathamangitsidwa ndi anthu a ku Ai.
5 Og Mændene af Ai sloge ved seks og tredive Mænd af dem og forfulgte dem foran Porten indtil Sebarim og sloge dem, hvor Vejen gik nedad; da blev Folkets Hjerte mistrøstigt og blev som Vand.
Anthu a ku Ai anathamangitsa Aisraeli kuchokera pa chipata cha mzindawo mpaka ku ngwenya ndipo anapha anthu 36. Iwowa anawapha pamene ankatsika phiri. Choncho mitima ya anthu inasweka ndipo analibenso mphamvu.
6 Og Josva sønderrev sine Klæder og faldt paa sit Ansigt til Jorden for Herrens Ark indtil Aftenen, han og de Ældste af Israel, og de kastede Støv paa deres Hoved.
Tsono Yoswa anangʼamba zovala zake nagwada nʼkuweramitsa mutu wake pansi patsogolo pa Bokosi la Yehova. Akuluakulu a Israeli nawonso anadzigwetsa pansi ndipo anakhala pomwepo mpaka madzulo atadziwaza fumbi kumutu kwawo.
7 Og Josva sagde: Ak, Herre, Herre! hvi lod du dog dette Folk gaa over Jordanen for at give os i Amoriternes Haand til vor Fordærvelse? og gid vi havde ladet os nøje og vare blevne paa hin Side Jordanen!
Ndipo Yoswa anati, “Kalanga ine, Ambuye Wamphamvuzonse chifukwa chiyani munatiwolotsa Yorodani? Kodi mumalinga zotipereka mʼmanja mwa Aamori kuti atiwononge chotere? Kukanakhala kwabwino ife tikanakhala tsidya linalo la Yorodani!
8 Hør mig, Herre! hvad skal jeg sige, efter at Israel vender Ryggen for sine Fjenders Ansigt?
Tsono Ambuye, ine ndinene chiyani, pakuti tsopano Israeli anathamangitsidwa ndi adani ake?
9 Naar Kananiterne og alle Landets Indbyggere høre det, da omringe de os og udrydde vort Navn af Jorden; og hvad vil du gøre ved dit store Navn?
Akanaani ndi anthu ena a dziko lino adzamva zimenezi ndipo adzatizinga ndi kutiwonongeratu. Nanga inu mudzatani ndi dzina lanu lamphamvulo?”
10 Da sagde Herren til Josva: Staa du op; hvorfor faldt du paa dit Ansigt?
Koma Yehova anati kwa Yoswa, “Imirira! Chifukwa chiyani wagwada pansi chotere?
11 Israel har syndet, ja, de have overtraadt min Pagt, hvilken jeg bød dem; ja, de toge af det bandlyste Gods, ja, de stjal og dulgte det ogsaa og lagde det iblandt deres eget Tøj.
Aisraeli achimwa. Iwo aphwanya pangano limene ndinawalamula kuti asunge. Anatengako zinthu zina zofunika kuwonongedwa. Choncho anabako, ananena bodza ndi kuyika zinthu zakubazo pamodzi ndi katundu wawo.
12 Og Israels Børn skulle ikke kunne staa for deres Fjenders Ansigt, de maa vende Ryggen for deres Fjenders Ansigt, thi de ere i Band; jeg skal ikke mere blive ved at være med eder, dersom I ikke fjerne denne Band fra eders Midte.
Nʼchifukwa chake Aisraeli sangathe kulimbana ndi adani awo. Iwo anathawa pamaso pa adani awo chifukwa ndiwo oyenera kuwonongedwa. Ine sindikhalanso ndi inu pokhapokha mutawononga chilichonse choyenera kuwonongedwa pakati panu.
13 Staa op, hellig Folket, og sig: Helliger eder til i Morgen; thi saa siger Herren Israels Gud: Der er Band iblandt dig, Israel! du kan ikke staa for dine Fjenders Ansigt, førend I borttage den Band fra eders Midte.
“Nyamuka, ukawawuze anthu kuti, ‘Mudzipatule nokha kukonzekera kuonana nane mawa; pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti choyenera kuwonongedwa chija chili pakati panu, inu Aisraeli. Simungathe kulimbana ndi adani anu mpaka mutachichotsa.’
14 Og i Morgen tidlig skulle I komme frem efter eders Stammer; og det skal ske, hvilken Stamme Herren rammer paa, den skal nærme sig, Slægt for Slægt, og den Slægt, som Herren rammer paa, den skal nærme sig, Hus for Hus, og det Hus, som Herren rammer paa, det skal nærme sig, Mand for Mand.
“Mawa mmamawa adzabwere pamaso pa Yehova fuko limodzilimodzi. Fuko limene Yehova adzaliloze lidzabwere patsogolo mbumba imodziimodzi. Tsono mbumba imene Yehova adzayiloze idzabwere patsogolo banja limodzilimodzi. Banja limene Yehova adzaliloze lidzabwere patsogolo munthu mmodzimmodzi.
15 Og det skal ske, den, som bliver ramt som bandlyst, han skal opbrændes med Ild, han og alt det, han har, fordi han har overtraadt Herrens Pagt, og fordi han har gjort en Daarlighed i Israel.
Iye amene adzagwidwe ndi zinthu zoyenera kuwonongedwazo adzawotchedwa ndi moto, pamodzi ndi banja lake lonse ndi zinthu zake zonse. Iyeyutu wachita chinthu chonyansa pakati pa Aisraeli ndi kuphwanya pangano limene anthu anga anachita ndi Ine!”
16 Og Josva stod tidlig op om Morgenen og lod Israel nærme sig Stamme for Stamme, og Judas Stamme blev ramt.
Mmawa mwake Yoswa anabweretsa Israeli fuko limodzilimodzi ndipo fuko la Yuda linalozedwa.
17 Og han lod Judas Slægt nærme sig, og Seraiternes Slægt blev ramt.
Anabweretsa poyera mbumba zonse za fuko la Yuda, ndipo mbumba ya Zera inagwidwa. Kenaka anatulutsa poyera mabanja onse a mbumba ya Zera ndipo banja la Zabidi linagwidwa.
18 Og han lod Seraiternes Slægt nærme sig, Mand for Mand, og Sabdi blev ramt, og han lod hans Hus nærme sig, Mand for Mand, og Akan, en Søn af Karmi, som var Sabdi Søn, Seras Søn, af Judas Stamme, blev ramt.
Potsiriza anatulutsa anthu onse a banja la Zabidi ndipo Akani anagwidwa. Iyeyu anali mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera wa fuko la Yuda.
19 Og Josva sagde til Akan: Min Søn, giv dog Herren Israels Gud Ære og giv ham Lov, og giv mig nu til Kende, hvad du har gjort, dølg det ikke for mig!
Ndipo Yoswa anati kwa Akani, “Mwana wanga pereka ulemerero kwa Yehova Mulungu wa Israeli ndipo umuyamike Iye. Ndiwuze zimene wachita, ndipo usandibisire.”
20 Og Akan svarede Josva og sagde: Sandelig, jeg syndede for Herren Israels Gud, og saa og saa gjorde jeg.
Akani anayankha kuti, “Zoona! Ine ndachimwira Yehova Mulungu wa Israeli. Chimene ndachita ine ndi ichi:
21 Thi jeg saa en kostelig babylonisk Kappe iblandt Byttet og to Hundrede Sekel Sølv og en Guldtunge, hvis Vægt var halvtredsindstyve Sekel, og jeg fik Lyst til dem og tog dem, og se, de ere skjulte i Jorden, midt i mit Telt, og Sølvet derunder.
Ndinaona mwa zinthu zolanda ku nkhondo zija, mkanjo wokongola wa ku Babuloni, makilogalamu awiri a siliva ndiponso golide wolemera theka la kilogalamu. Zimenezi ndinazikhumba ndipo ndinazitenga. Ndazibisa mʼkati mwa tenti yanga, ndipo siliva ali pansi pake.”
22 Da sendte Josva Bad hen, og de løb til Teltet; og se, det var skjult i hans Telt og Sølvet derunder.
Motero Yoswa anatuma anthu, ndipo anathamanga kupita ku tenti. Anthuwo anakapeza kuti zinthuzo zinabisidwadi mʼtenti yake, ndipo siliva analidi pansi pake.
23 Og de toge de Ting ud af Teltet og førte dem til Josva og til alle Israels Børn; og de lagde dem frem for Herrens Ansigt.
Iwo anazichotsa zinthuzo mu tenti yake nabwera nazo kwa Yoswa ndi kwa Aisraeli onse ndipo anaziyika pamaso pa Yehova.
24 Saa tog Josva og al Israel med ham Akan, Seras Søn, og Sølvet og den kostelige Kappe og Guldtungen og hans Sønner og hans Døtre og hans Øksne og hans Asener og hans Faar og hans Telt, og alt det han havde, og de førte ham op i Akors Dal.
Kenaka Yoswa pamodzi ndi Aisraeli onse anatenga Akani mwana wa Zera pamodzi ndi siliva, mkanjo, golide zimene anapezeka nazo zija. Anatenganso ana ake aamuna ndi aakazi, ngʼombe zake, abulu ndi nkhosa, tenti yake ndi zonse anali nazo, kupita nazo ku chigwa cha Akori.
25 Og Josva sagde: Hvi har du forstyrret os? Herren skal forstyrre dig paa denne Dag; og al Israel stenede ham med Stene og opbrændte dem med Ild og kastede Stene over dem.
Yoswa anati “Chifukwa chiyani wabweretsa mavuto awa pa ife? Yehova ndiye abweretse mavuto pa iwe lero.” Kenaka Aisraeli onse anaponya miyala Akani, namupha. Anaponyanso miyala banja lake lonse, nʼkulipha. Pambuyo pake anatentha Akani uja, banja lake ndi zonse zimene anali nazo.
26 Og de opkastede en stor Stenhob over ham indtil denne Dag, og Herren vendte om fra sin strenge Vrede; derfor kaldte man det samme Steds Navn Akors Dal; den er der indtil denne Dag.
Anawunjika mulu waukulu wa miyala pa Akani, imene ilipobe mpaka lero. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Akori mpaka lero. Ndipo Yehova anachotsa mkwiyo wake.