< Josua 14 >
1 Og dette er det, som Israels Børn arvede i Kanaans Land, som Eleasar, Præsten, og Josva, Nuns Søn, og Øversterne for Fædrenehusene iblandt Israels Børns Stammer, uddelte dem til Arv,
Umu ndi mmene Aisraeli analandirira cholowa chawo mʼdziko la Kanaani. Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni pamodzi ndi akuluakulu a mafuko a Israeli ndiwo anagawa dzikolo kugawira Aisraeli.
2 ved Lodkastning om deres Arv, som Herren havde befalet ved Mose, at give de ni Stammer og den halve Stamme.
Madera anagawidwa mwa maere kwa mafuko asanu ndi anayi ndi theka, monga momwe Yehova analamulira kudzera mwa Mose.
3 Thi Mose havde givet de to Stammer og den halve Stamme Arv paa hin Side Jordanen; men han gav ikke Leviterne Arv midt iblandt dem.
Mose anapereka kwa mafuko awiri ndi theka dziko la kummawa kwa Yorodani, koma fuko la Levi lokha silinagawiridwe malo.
4 Thi Josefs Børn vare to Stammer, Manasse og Efraim; men de gave ikke Leviterne nogen Del i Landet, uden Stæder at bo udi og Markerne deromkring for deres Kvæg og for deres Gods.
Tsono fuko la Yosefe analigawa pawiri, Manase ndi Efereimu. Mose sanawagawire malo mabanja a fuko la Levi, koma iwo anangolandira mizinda imene ankakhalamo pamodzi ndi malo amene ankawetako nkhosa ndi ngʼombe zawo.
5 Som Herren bød Mose, saa gjorde Israels Børn, og de delte Landet.
Choncho Aisraeli anagawana dzikolo, monga momwe Yehova analamulira Mose.
6 Og Judas Børn gik frem til Josva i Gilgal, og Kaleb, Jefunne den Kenisiters Søn, sagde til ham: Du ved det Ord, som Herren talede til Mose, den Guds Mand, angaaende mig og dig i Kades-Barnea.
Tsono anthu a fuko la Yuda anabwera kwa Yoswa ku Giligala, ndipo Kalebe mwana wa Yefune Mkeni anati kwa iye, “Inu mukudziwa zimene Yehova ananena kwa Mose munthu wa Mulungu za inu ndi ine ku Kadesi Barinea.
7 Jeg var fyrretyve Aar gammel, der Mose, Herrens Tjener, sendte mig fra Kades-Barnea til at spejde Landet; og jeg bragte ham Svar igen, ligesom jeg mente.
Nthawi imene Mose mtumiki wa Yehova anandituma kuchokera ku Kadesi Barinea kudzayendera dzikoli ndinali ndi zaka makumi anayi. Ndipo nditabwerako ndinamuwuza zoona zokhazokha monga momwe ndinaonera.
8 Men mine Brødre, som gik op med mig, mistrøstede Folkets Hjerte; men jeg efterfulgte Herren min Gud fuldkommeligen.
Koma abale anga amene ndinapita nawo anachititsa anthu mantha. Komabe ine ndinamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wonse.
9 Da svor Mose paa den samme Dag og sagde: Det Land, som din Fod traadte paa, skal blive dig og dine Børn til Arv evindeligen, fordi du fuldkommeligen efterfulgte Herren min Gud.
Kotero tsiku limenelo Mose anandilonjeza kuti, ‘Dziko limene unayendamo lidzakhala lako ndiponso la ana ako kwamuyaya chifukwa unamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wako wonse.’
10 Og nu, se, Herren har ladet mig leve, som han sagde, disse fyrretyve og fem Aar, fra den Tid, da Herren talede dette Ord til Mose, den Gang Israel vandrede i Ørken; og nu, se, jeg er i Dag fem og firsindstyve Aar gammel.
“Tsono papita zaka 45 chiyankhulire Yehova zimenezi kwa Mose. Nthawi imeneyo nʼkuti Aisraeli akuyendayenda mʼchipululu. Yehova wandisunga ndipo tsopano ndili ndi zaka 85.
11 Jeg er endnu i Dag saa stærk, som paa den Dag, der Mose sendte mig: Som min Kraft var da, saa er og min Kraft nu til Krigen og til at gaa ud og til at gaa ind.
Komabe ndikanali ndi mphamvu lero, monga ndinalili tsiku lija Mose anandituma. Ndili ndi mphamvu moti ndikhoza kupita ku nkhondo kapena kuchita kanthu kena kalikonse.
12 Saa giv mig nu dette Bjerg, som Herren talede om paa den samme Dag; thi du hørte paa den samme Dag, at Anakiterne ere der, og store og faste Stæder; maaske Herren vil være med mig, at jeg kan fordrive dem, ligesom Herren har sagt.
Tsopano ndipatseni dziko la ku mapiri limene Yehova anandilonjeza tsiku lija. Inu munamva nthawi ija kuti Aanaki anali kumeneko ndipo kuti mizinda yawo inali ikuluikulu ndi yotetezedwa. Komabe Yehova atakhala nane ndidzawathamangitsa monga Iye ananenera.”
13 Saa velsignede Josva ham, og han gav Kaleb, Jefunne Søn, Hebron til Arv.
Ndipo Yoswa anadalitsa Kalebe mwana wa Yefune ndi kumupatsa Hebroni kukhala dziko lake.
14 Derfor blev Hebron Kaleb, Jefunne den Kenisiters Søn, til Arv indtil denne Dag, fordi han fuldkommeligen efterfulgte Herren Israels Gud.
Choncho dera la Hebroni lakhala lili la Kalebe mwana wa Yefune Mkeni mpaka lero chifukwa anamvera Yehova Mulungu wa Israeli ndi mtima wonse.
15 Men Hebron kaldtes tilforn Arbas Stad, han var det største Menneske iblandt Anakiterne; og Landet hvilede fra Krig.
(Hebroni ankatchedwa Kiriati Ariba chifukwa cha Ariba amene anali munthu wamphamvu kwambiri pakati pa Aanaki). Ndipo kenaka mʼdziko monse munakhala mtendere.