< Jonas 2 >
1 Og Jonas bad til Herren sin Gud fra Fiskens Liv,
Yona ali mʼmimba mwa chinsomba chija anapemphera kwa Yehova Mulungu wake.
2 og han sagde: Jeg raabte til Herren ud af min Angest, og han svarede mig; jeg, skreg fra Dødsrigets Skød, du hørte min Røst. (Sheol )
Iye anati: “Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova, ndipo Iye anandiyankha. Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo, ndipo Inu munamva kulira kwanga. (Sheol )
3 Du kastede mig i Dybet, midt i Havet, og Strømmen omgav mig; alle dine Vover og dine Bølger gik over mig.
Munandiponya mʼnyanja yozama, mʼkati mwenimweni mwa nyanja, ndipo madzi oyenda anandizungulira; mafunde anu onse ndi mkokomo wake zinandimiza.
4 Og jeg sagde: Jeg er udstødt fra dine Øjne, men jeg skal atter skue hen til dit hellige Tempel.
Ndinati, ‘Ine ndachotsedwa pamaso panu; komabe ndidzayangʼananso ku Nyumba yanu yopatulika.’
5 Vandene omsluttede mig indtil Sjælen, Dybet omgav mig, Tang var viklet om mit Hoved.
Madzi wondimiza anandichititsa mantha, nyanja yozama inandizungulira; udzu wa mʼmadzi zinakuta mutu wanga.
6 Jeg sank ned til Bjergenes Grunde, Jordens Porte vare lukkede efter mig for evigt; men du Herre, min Gud, drog mit Liv op af Graven.
Ndinatsikira kunsi ndithu, mʼtsinde mwa mapiri; mipiringidzo ya dziko inanditsekereza kosatha. Koma Inu munatulutsa moyo wanga mʼmandamo, Inu Yehova Mulungu wanga.
7 Der min Sjæl i mit Indre forsmægtede, kom jeg Herren i Hu; og min Bøn kom til dig i dit hellige Tempel.
“Pamene moyo wanga umachoka mwa ine, ine ndinakumbukira Inu Yehova, ndipo pemphero langa linafika kwa inu, ku Nyumba yanu yopatulika.
8 De, som tage Vare paa Løgnens Gøglebilleder, de have forladt ham, som er dem Miskundhed.
“Iwo amene amagwiritsitsa mafano achabechabe amataya chisomo chawo.
9 Men jeg, jeg vil med Taksigelses Røst ofre til dig, jeg vil betale det, jeg har lovet; Frelse er der hos Herren.
Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe ndikuyimba nyimbo yamayamiko. Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa. Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”
10 Og Herren bød Fisken, og den udspyede Jonas paa det tørre Land.
Ndipo Yehova analamula chinsomba chija, ndipo chinakamusanza Yonayo mʼmbali mwa nyanja.