< Job 5 >
1 Raab, kære, om der er nogen, som svarer dig? og til hvem af de hellige vil du vende Ansigtet?
“Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe? Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
2 Thi Fortørnelse slaar en Daare ihjel, og Nidkærhed dræber den taabelige.
Mkwiyo umapha chitsiru, ndipo njiru imawononga wopusa.
3 Jeg saa en Daare rodfæstet, og jeg forbandede hans Bolig hastelig.
Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu, koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
4 Hans Børn vare langt fra Frelse og nedtraadtes i Porten, og der var ingen, som reddede dem.
Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe; amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
5 Den hungrige opaad hans Høst og hentede den endog fra Tjørnehegnet, og Røverne opslugte hans Formue.
Anthu anjala amamudyera zokolola zake, amamutengera ndi za pa minga pomwe, ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
6 Thi Uretfærdighed skyder ikke frem af Støvet, og Møje vokser ikke op af Jorden;
Pakuti masautso satuluka mʼfumbi, ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
7 men et Menneske bliver født til Møje, ligesom Gnister maa flyve højt op.
Komatu munthu amabadwira kuti azunzike monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.
8 Dog jeg vilde søge hen til Gud, og til Gud vilde jeg rette min Tale;
“Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu; ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
9 til ham, som gør store Ting, hvilke man ikke kan ransage, underlige Ting, saa der er intet Tal paa dem;
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
10 ham, som giver Regn paa Jorden og lader Vand komme paa Markerne;
Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi, ndipo amathirira minda ya anthu.
11 for at sætte de ringe højt op, og at de sørgende ophøjes ved Frelse;
Iye amakweza anthu wamba, ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
12 ham, som gør de træskes Anslag til intet, at deres Hænder ikke kunne udføre Sagen;
Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera, kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
13 ham, som griber de vise i deres Træskhed, saa de underfundiges Raad hastelig omstødes;
Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo, ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
14 om Dagen løbe de an i Mørket og føle sig for om Middagen, som var det Nat.
Mdima umawagwera nthawi yamasana; nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
15 Og han frelser en fattig fra Sværd, fra deres Mund og fra den stærkes Haand,
Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo; amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
16 saa der bliver Haab for den ringe, og Uretfærdighed maa lukke sin Mund.
Choncho osauka ali ndi chiyembekezo, ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.
17 Se, saligt er det Menneske, som Gud straffer; derfor foragte du ikke den Almægtiges Tugtelse!
“Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula; nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
18 Thi han gør Smerte og forbinder; han saargør, og hans Hænder læge.
Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo; Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
19 I seks Angester skal han fri dig, og i syv skal intet ondt røre dig.
Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi, mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
20 I Hunger skal han frelse dig fra Døden og i Krig fra Sværdets Vold.
Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa, ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
21 Du skal finde Skjul for Tungens Svøbe og ikke frygte for Ødelæggelse, naar den kommer.
Adzakuteteza kwa anthu osinjirira, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
22 Du skal le ad Ødelæggelse og Hunger og ikke frygte for Jordens Dyr;
Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala, ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
23 thi med Stenene paa Marken har du Pagt, og Markens Dyr skulle holde Fred med dig.
Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako, ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
24 Og du skal forfare, at dit Telt har Fred, og du skal besøge din Bolig og intet savne.
Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa; udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
25 Og du skal forfare, at din Sæd skal blive mangfoldig, og din Afkom som Græs paa Jorden.
Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri, ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
26 Du skal komme til Graven i Alderdom, ligesom Neg optages i sin Tid.
Udzafika ku manda utakalamba, monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.
27 Se dette, det have vi undersøgt, saa er det; hør det, og forstaa det vel!
“Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona, choncho uzimvere ndi kuzitsata.”