< Job 33 >

1 Og Job, hør dog nu min Tale, og vend dine Øren til alle mine Ord!
“Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
2 Se nu, jeg har opladt min Mund, min Tunge taler allerede ved min Gane.
Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
3 Mine Taler skulle udsige mit Hjertes Oprigtighed, og mine Læber skulle udtale rent det, som jeg ved.
Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
4 Guds Aand har skabt mig, og den Almægtiges Aande gør mig levende.
Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
5 Dersom du kan, saa giv mig Svar; rust dig for mit Ansigt og fremstil dig!
Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
6 Se, jeg er ligesom du over for Gud, ogsaa jeg er dannet af Ler.
Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
7 Se, Rædsel for mig skal ikke forfærde dig, og intet Tryk fra mig skal være svart over dig.
Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
8 Men du sagde for mine Øren, og jeg hørte Talen, som lød:
“Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
9 Jeg er ren, uden Overtrædelse, jeg er skyldfri, og der er ingen Misgerning hos mig.
‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
10 Se, han har fundet paa Fjendtligheder imod mig, han agter mig for sin Modstander;
Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
11 han har lagt mine Fødder i Stok, han tager Vare paa alle mine Stier.
Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
12 Se, heri har du ikke Ret! jeg vil svare dig; thi Gud er for høj for et Menneske.
“Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
13 Hvorfor har du trættet med ham, fordi han ikke gør dig Regnskab for nogen af sine Gerninger?
Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
14 Men Gud taler een Gang og anden Gang; man agter ikke derpaa.
Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
15 I Drøm, i Syn om Natten, naar den dybe Søvn falder paa Folk, naar de slumre paa Sengen,
Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
16 da aabner han Menneskenes Øren, og besegler Formaningen til dem
amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
17 for at bortdrage Mennesket fra hans Idrætter og for at fjerne Hovmodet fra Manden,
kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
18 for at spare hans Sjæl fra Graven og hans Liv fra at omkomme ved Sværd.
kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
19 Han straffes ogsaa med Pine paa sit Leje og med vedholdende Uro i hans Ben,
“Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
20 saa at hans Liv væmmes ved Brød og hans Sjæl ved lækker Mad;
kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
21 hans Kød fortæres, saa man ikke kan se det, og hans Ben hensmuldre og ses ikke;
Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
22 og hans Sjæl kommer nær til Graven og hans Liv nær til de dræbende Magter.
Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
23 Dersom der da er en Engel, en Talsmand, hos ham, en af de tusinde, til at kundgøre Mennesket hans rette Vej:
“Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
24 Saa skal Gud forbarme sig over ham og sige: Befri ham, at han ikke farer ned i Graven; jeg har faaet Løsepenge;
kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
25 da skal hans Kød blive kraftigt mere end i den unge Alder; sin Ungdoms Dage skal han faa igen.
pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
26 Han skal bede til Gud, og denne skal være ham naadig, og han skal se hans Ansigt med Frydeskrig, og han skal gengive Mennesket hans Retfærdighed.
Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
27 Han skal synge for Mennesker og sige: Jeg har syndet og forvendt Retten; men det er ikke blevet mig gengældt.
Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
28 Han har befriet min Sjæl, at den ikke farer ned i Graven, og mit Liv skal se paa Lyset.
Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
29 Se, alle disse Ting gør Gud to, tre Gange ved en Mand
“Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
30 for at føre hans Sjæl tilbage fra Graven, at den maa beskinnes af de levendes Lys.
kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
31 Mærk det, Job! hør mig; ti stille, og jeg vil tale.
“Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
32 Har du noget at sige, da giv mig Svar; tal, thi jeg har Lyst til at give dig Ret.
Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
33 Men har du intet, da hør du paa mig; ti stille, saa vil jeg lære dig Visdom!
Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”

< Job 33 >