< Job 31 >

1 Jeg gjorde en Pagt med mine Øjne, og hvad skulde jeg agte paa en Jomfru?
“Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
2 Og hvad for en Lod vilde Gud have givet ovenfra og hvad for en Arv den Almægtige fra det høje?
Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
3 Mon ikke Ulykke er beredt for den uretfærdige og Undergang for dem, som gøre Uret?
Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
4 Mon han ikke ser mine Veje og tæller alle mine Skridt?
Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
5 Dersom jeg har vandret med Falskhed, og min Fod har hastet til Svig,
“Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
6 — han veje mig paa Retfærdigheds Vægtskaaler, og Gud kende min Uskyldighed —
Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
7 dersom min Gang har bøjet af fra Vejen, og mit Hjerte er gaaet efter mine Øjne, og en Plet har klæbet ved mine Hænder:
ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
8 Da gid jeg maa saa, men en anden æde, og mit Afkom maa oprykkes med Rod.
Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
9 Dersom mit Hjerte er forlokket til en Kvinde, og jeg har luret ved min Næstes Dør:
“Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
10 Da gid min Hustru maa male for en anden, og andre bøje sig over hende.
pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
11 Thi det var en Skændselsgerning, og det var en Misgerning, som hørte hen for Dommerne;
Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
12 thi det var en Ild, som fortærede indtil Afgrunden, og som skulde have oprykket al min Afgrøde med Rode.
Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
13 Dersom jeg havde foragtet min Tjeners eller min Tjenestepiges Ret, naar de trættede med mig;
“Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
14 — og hvad vilde jeg gøre, naar Gud vilde opstaa? og naar han vilde hjemsøge, hvad skulde jeg svare ham?
ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
15 har ikke han, som skabte mig i Moders Liv, skabt ham? og har ikke en og den samme beredt os i Moderskød? —
Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
16 dersom jeg har nægtet de ringe deres Begæring og ladet Enkens Øjne vansmægte,
“Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
17 og jeg har ædt min Mundbid for mig alene, saa at den faderløse ikke aad deraf;
ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
18 — tværtimod, han er opvokset hos mig som hos en Fader fra min Ungdom af, og hende ledede jeg, fra min Moders Liv af —
chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
19 dersom jeg har set en forkommen, uden Klæder, og at den fattige intet Dække havde;
ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
20 dersom hans Lænder ikke have velsignet mig, medens han varmede sig ved Ulden af mine Faar;
ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
21 dersom jeg har løftet min Haand imod den faderløse, fordi jeg saa Hjælp for mig i Porten:
ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
22 Da gid min Skulder maa falde fra Skulderbladet, og min Arm brydes fra Armpiben!
pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
23 Thi en Rædsel vilde være kommen over mig, en Ulykke fra Gud, og imod hans Højhed formaaede jeg intet.
Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
24 Dersom jeg har sat Guld til mit Haab eller sagt til det kostelige Guld: Du er min Tillid;
“Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
25 dersom jeg har glædet mig, at mit Gods var meget, og at min Haand havde forhvervet mangfoldigt;
ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
26 dersom jeg har set til Sollyset, naar det skinnede, eller til Maanen, naar den gaar herlig,
ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
27 og mit Hjerte har ladet sig forlokke i Løndom, saa at min Mund kyssede min Haand:
ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
28 — Ogsaa dette havde været en Misgerning, som hørte hen under Dommerne; thi jeg havde hyklet for Gud i det høje —!
pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
29 dersom jeg har glædet mig over min Fjendes Undergang og jublet, naar Ulykken ramte ham;
“Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
30 — men jeg tilstedede ikke min Gane at synde, saa at jeg under Forbandelse begærede hans Sjæl —
ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
31 dersom ikke Mændene i mit Telt have sagt: Hvor finder man nogen, som ikke er bleven mæt af hans Kød?
ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
32 — den fremmede maatte ikke ligge udenfor om Natten, jeg lod mine Døre op for vejfarende —
Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
33 dersom jeg har skjult mine Overtrædelser som Adam og dulgt min Misgerning i min Barm,
ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
34 fordi jeg frygtede den store Hob, og Slægters Foragt kunde have forfærdet mig, saa at jeg tav og ikke gik ud af en Dør —
chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
35 Havde jeg dog den, som vilde høre paa mig! se her min Underskrift — den Almægtige svare mig — og her den Klage, min Modpart har opsat;
“Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
36 sandelig, jeg skulde tage den paa min Skulder, jeg skulde binde den omkring mig som et Hovedsmykke!
Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
37 Jeg vil tilkendegive ham ethvert af mine Skridt, som en Fyrste vil jeg nærme mig ham.
Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
38 Dersom min Ager raaber imod mig, og alle dens Furer græde;
“Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
39 dersom jeg har fortæret dens Grøde uden at have betalt den og udblæst Sjælen fra dens Ejermand:
ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
40 Gid da vokse Tjørn i Stedet for Hvede, og Ukrudt i Stedet for Byg; — Jobs Ord have Ende.
pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.

< Job 31 >