< Job 30 >

1 Men nu le de ad mig, som ere yngre af Aar end jeg, de, hvis Fædre jeg vilde have forsmaaet at sætte hos mine Faarehunde.
“Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
2 Ja, hvortil skulde deres Hænders Kraft have gavnet mig? hos dem er Styrken svundet bort.
Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
3 De ere udtærede af Mangel og Hunger, de afgnave den golde Ørk, i Ødelæggelsens og Fordærvelsens Nat;
Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku.
4 de oprykke Katost ved Buskene, og Gyveltræets Rod er deres Føde;
Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
5 de uddrives fra Samfundet, man skriger efter dem som efter en Tyv;
Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
6 de bo i Kløfter i Dalene, i Huler i Jorden og Klipper;
Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
7 imellem Buske skryde de, de samles under Nælder.
Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
8 Børn af Daarer, ja af Mænd uden Navn; de ere udstødte af Landet.
Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko.
9 Men nu er jeg bleven en Spottesang for dem og maa tjene dem til Snak.
“Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
10 De have Vederstyggelighed til mig, de holde sig langt fra mig og spare ikke at spytte mig i Ansigtet.
Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
11 Thi de have løst Tøjlen af sig og plaget mig, og de have kastet Bidselet af for mit Ansigt.
Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa.
12 Til højre for mig staar en Yngel frem, de støde mine Fødder bort, og de bane deres Fordærvelses Veje imod mig;
Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
13 de bryde min Sti op, de hjælpe til min Ulykke, de have ingen Hjælper;
Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa.
14 de komme som igennem et vidt Gab, de vælte sig frem under Bulder.
Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
15 Rædsler ere vendte imod mig, som et Stormvejr forfølge de min Herlighed, og min Frelse er gaaet forbi som en Sky.
Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.
16 Men nu er min Sjæl hensmeltet i mig, Elendigheds Dage komme over mig.
“Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso.
17 Natten gennemborer mine Ben, saa at de falde af mig, og mine nagende Smerter hvile ikke.
Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka.
18 Ved den overvættes Magt er min Klædning helt forandret, den omslutter mig som Kraven paa min Underkjortel.
Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
19 Han har kastet mig i Dyndet, og jeg er lignet ved Støv og Aske.
Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.
20 Jeg skriger til dig, men du svarer mig ikke; jeg staar der, og du bliver ved at se paa mig.
“Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
21 Du har forvendt dig til at være grum imod mig; du modstaar mig med din Haands Styrke.
Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
22 Du løfter mig op i Stormvejret, du lader mig fare hen, og du lader mig forgaa i dets Brag.
Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
23 Thi jeg ved, du fører mig til Døden igen og til alle levendes Forsamlings Hus.
Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako.
24 Mon en ikke udrækker Haanden i sit Fald? eller mon en ikke skriger i sin Ulykke?
“Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
25 Eller græd jeg ikke for den, som havde haarde Dage? ynkedes min Sjæl ikke over den fattige?
Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
26 Thi der jeg forventede godt, da kom det onde, og der jeg haabede til Lys, da kom Mørkhed.
Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
27 Mine Indvolde syde og ere ikke stille; Elendigheds Dage ere komne over mig.
Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso.
28 Jeg gaar sort, uden Sol, jeg staar op, jeg skriger i Forsamlingen.
Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
29 Jeg er bleven Dragers Broder og Strudses Stalbroder.
Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi.
30 Min Hud er bleven sort og falder af mig, og Benene i mig brænde af Hede.
Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
31 Og min Harpe er bleven til Sorrig, og min Fløjte til de grædendes Lyd.
Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.

< Job 30 >