< Job 15 >

1 Da svarede Elifas, Themaniten, og sagde:
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 Skal en viis svare med Kundskab, som kun er Vejr, og fylde sin Bug med Blæst,
“Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
3 idet han fører Bevis med Ord, som ikke gavne, og med Taler, som intet baade!
Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
4 Ja, du tilintetgør Gudsfrygt og svækker Bønnen for Guds Ansigt.
Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
5 Thi din egen Mund beviser din Misgerning, og du vælger de træskes Tunge.
Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
6 Din egen Mund dømmer dig skyldig og ikke jeg, og dine Læber vidne imod dig.
Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
7 Mon du er født som det første Menneske var, og er du avlet førend Højene?
“Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
8 Mon du har hørt til i Guds hemmelige Raad og har revet Visdommen til dig?
Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
9 Hvad ved du, som vi ikke vide? hvad forstaar du, og det skulde ikke være os bekendt?
Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
10 Der er baade graahærdede og bedagede iblandt os, Mænd, som have levet længere end din Fader.
Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
11 Er Guds Trøst dig for ringe og det Ord, som han i Mildhed har talt med dig?
Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
12 Hvorfor betager dit Hjerte dig, og hvorfor blinke dine Øjne?
Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
13 Thi du vender din Harme imod Gud, og du har ladet Taler udfare af din Mund.
moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
14 Hvad er et Menneske, at det skulde være rent? eller at den skulde være retfærdig, som er født af en Kvinde?
“Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
15 Se, han tror ikke sine hellige, og Himlene ere ikke rene for hans Øjne:
Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
16 Hvor meget mindre den, som er vederstyggelig og fordærvet, den Mand, der drikker Uretfærdighed som Vand?
nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
17 Jeg vil kundgøre dig det, hør mig; og hvad jeg har set, vil jeg fortælle:
“Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
18 Hvad de vise have forkyndt, og hvad de ikke have dulgt som en Arv fra deres Fædre,
zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
19 dem alene blev Landet givet, og ingen fremmed trængte ind iblandt dem.
(Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
20 Den ugudelige bæver alle sine Dage, og faa Aar i Tallet ere henlagte til en Voldsmand.
Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
21 Rædsler lyde for hans Øren; midt i Freden kommer en Ødelægger over ham.
Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
22 Han kan ikke tro paa, at han vil komme tilbage fra Mørket, og han er udset til at omkomme ved Sværdet.
Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
23 Han vanker hid og did efter Brødet og siger: Hvor er det? han ved, at Mørkheds Dag er bestemt, ja er ved hans Side.
Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
24 Angest og Nød forfærde ham, det overvælder ham, som var det en Konge, der er rede til Striden;
Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
25 thi han har udrakt sin Haand imod Gud og har vældig sat sig op imod den Almægtige;
chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
26 han løb med oprakt Hals imod ham under sine Skjoldes tætte Tag;
Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
27 thi han har lagt Fedt paa sit Ansigt og lagt sig ud over sin Lænd med Fedme,
“Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
28 og han boede i Stæder, som vare ødelagte, i Huse, som man ikke bor i, som ere bestemte til Grushobe.
munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
29 Han skal ikke blive rig, og hans Formue skal ikke bestaa; og hvad de have erhvervet, skal ikke udbredes i Landet.
Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
30 Han skal ikke komme bort fra Mørket, en Lue skal tørre hans Kvist; men han skal komme bort ved hans Munds Aande.
Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
31 Han skal ikke forlade sig paa Forfængelighed, han skuffer sig; thi Forfængelighed skal vorde ham Betaling.
Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
32 Før hans Dag kommer, skal det opfyldes, og hans Gren skal ikke grønnes.
Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
33 Som Vintræet skal han afryste sine sure Druer og som Olietræet kaste sit Blomster.
Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
34 Thi den vanhelliges Forsamling skal blive øde, og Ild fortærer Bestikkelsens Telte.
Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
35 De undfange Uret og føde Udaad, og deres Inderste bereder Svig.
Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”

< Job 15 >