< Job 12 >
1 Men Job svarede og sagde:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Sandelig, I ere Folket, og med eder dør Visdommen ud!
“Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
3 Jeg har ogsaa Forstand ligesom I, jeg falder ikke igennem for eder; og hvo ved ikke saadanne Ting?
Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
4 Jeg er til Latter for min Ven, jeg, som raabte til Gud og fik Svar; den retfærdige, den oprigtige er til Latter.
“Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
5 En foragtet Lampe i den trygges Tanke er den, som er nær ved at snuble med Foden.
Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
6 Ødelæggernes Telte have Ro, og de, som rase imod Gud, ere meget trygge, ja den, som sætter sin Haand som Gud.
Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
7 Og sandelig, spørg dog Dyrene ad, og de skulle lære dig det; og Himmelens Fugle, og de skulle forkynde dig det.
“Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
8 Eller tal til Jorden, og den skal lære dig det, og Fiskene i Havet skulle fortælle dig det.
kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
9 Hvo ved ikke om alle disse Ting, at Herrens Haand har gjort dette?
Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
10 han, i hvis Haand hver levende Sjæl er, og Aanden i hvert Menneskes Kød!
Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
11 Mon ikke Øret prøver Talen, og Ganen smager Maden?
Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
12 Hos de graahærdede er Visdom, og Dagenes Længde giver Forstand.
Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
13 Hos ham er Visdom og Vælde, ham hører Raad og Forstand til.
“Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
14 Se, han nedbryder, og det skal ikke bygges, han lukker til for en Mand, og der skal ikke lukkes op.
Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
15 Se, han holder Vandene tilbage, og de borttørres, og han udlader dem, og de omvælte Landet.
Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
16 Hos ham er Styrke og Kraft; ham hører den til, som farer vild, og den, som fører vild.
Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
17 Han lader Raadgiverne gaa afklædte bort og gør Dommerne til Daarer.
Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
18 Han løser Kongernes Herredømme og lægger Baand om deres Lænder.
Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
19 Han lader Præsterne gaa afklædte bort og omkaster de stærke.
Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
20 Han berøver de sikre Talere Mælet, tager Forstanden fra de gamle.
Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
21 Han udøser Vanære over Fyrsterne og løser de stærkes Bælte.
Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
22 Han aabenbarer de dybe Ting af Mørket og udfører Dødens Skygge til Lyset.
Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
23 Han formerer Folkene og lader dem gaa til Grunde; han udbreder Folkene og bortfører dem.
Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
24 Han borttager Forstand fra Folkets Øverster i Landet og lader dem fare vild i det øde, hvor ingen Vej er.
Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
25 De famle i Mørke, hvor intet Lys er, og han bringer dem til at fare vild som den drukne.
Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.