< Jeremias 48 >
1 Imod Moab. Saa siger den Herre Zebaoth, Israels Gud: Ve, Nebo! thi den er ødelagt; beskæmmet, indtaget er Kirjathajm; beskæmmet er Misgab og forfærdet.
Ponena za Mowabu: Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Tsoka kwa mzinda wa Nebo, chifukwa wawonongedwa. Mzinda wa Kiriyataimu wachititsidwa manyazi ndipo wagonjetsedwa; linga lichititsidwa manyazi ndipo lagumulidwa.
2 Med Moabs Pris er det forbi; i Hesbon optænke de ondt imod det: Kommer og lader os udslette det, at det ikke mere er et Folk; ogsaa du, Madmen! skal ødelægges, et Sværd skal forfølge dig.
Palibenso amene akutamanda Mowabu; ku Hesiboni anthu anamupanganira zoyipa: ‘Bwerani, tiyeni timuwonongeretu kuti asakhalenso mtundu wa anthu.’ Inunso anthu a ku Madimena, adzakukhalitsani chete; ankhondo adzakupirikitsani.
3 Der høres et Skrig fra Horanajm: Ødelæggelse og stor Forstyrrelse.
Tamvani mfuwu wa anthu a ku Horonaimu. Iwo akulira kuti, ‘Kusakazika ndi kuwonongeka kwakukulu.’
4 Moab er forstyrret; de smaa derudi lade deres Skrig høre.
Mowabu wawonongeka; ana ake angʼonoangʼono akulira kwambiri.
5 Thi ad Opgangen til Lukit stiger Graad op over Graad; og ved Nedgangen til Horonajm hører man Forstyrrelses Skrig.
Anthu akukwera chikweza cha ku Luhiti, akulira kwambiri pamene akupita. Kulira chifukwa cha chiwonongeko kukumveka pa njira yotsikira ku Horonaimu.
6 Flyr, redder eders Liv! og I skulle være som den enlige i Ørken.
Thawani! Dzipulumutseni; khalani ngati mbidzi ya mʼchipululu.
7 Thi fordi du forlod dig paa dine Gerninger og paa dine Skatte, skal ogsaa du indtages; og Kamos skal vandre i Landflygtighed, hans Præster og hans Fyrster til Hobe.
Popeza inu munkadalira ntchito zanu ndi chuma chanu, nanunso mudzatengedwa ukapolo, ndipo Kemosi adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndi akuluakulu ake.
8 Og der skal komme en Ødelægger til hver Stad, og ingen Stad skal undslippe; og Dalen skal gaa til Grunde og Sletten ødelægges, som Herren har sagt.
Wowononga adzabwera ndi kusakaza mzinda uliwonse, ndipo palibe mzinda umene udzapulumuke. Chigwa chidzasanduka bwinja ndipo malo athyathyathya a pamwamba pa phiri adzawonongedwa monga Yehova wayankhulira.
9 Giver Moab Vinger, thi det skal flyve ud; og dets Stæder skulle være til en Ødelæggelse, saa at ingen skal bo i dem.
Mtsineni khutu Mowabu chifukwa adzasakazika; mizinda yake idzasanduka mabwinja, wopanda munthu wokhalamo.
10 Forbandet være den, som gør Herrens Gerning med Efterladenhed; og forbandet være den, som holder sit Sværd tilbage fra Blod.
“Wotembereredwa munthu amene amagwira ntchito ya Yehova monyinyirika! Wotembereredwa munthu amene amaletsa lupanga lake kupha anthu!
11 Moab har boet trygt fra sin Ungdom af og ligget stille paa sin Bærme og er ikke tømt af et Kar i det andet, og det er ikke draget bort iblandt de bortførte; derfor har det beholdt sin Smag, og dets Lugt er ikke forandret.
“Mowabu wakhala pa mtendere kuyambira ubwana wake, ngati vinyo wokhazikika pa masese ake, osapungulidwa kuchoka mu mtsuko wina kuthira mu mtsuko wina; iye sanatengedwepo ukapolo. Nʼchifukwa chake kukoma kwake nʼkomwe kuja ndipo fungo lake silinasinthe.
12 Derfor se, de Dage skulle komme, siger Herren, da jeg vil sende Folk til det, som skulle vende dets Fade om; de skulle tømme dets Kar og sønderbryde dets Flasker.
Nʼchifukwa chake masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzatuma anthu amene amakhuthula vinyo mʼmitsuko ndipo adzamukhutula; adzakhuthula vinyo yense mitsuko yake pambuyo pake nʼkuphwanya mitsukoyo.
13 Og Moab skal blive til Skamme over Kamos, ligesom Israels Hus blev til Skamme over Bethel, som de forlode sig paa.
Pamenepo Mowabu adzachita manyazi ndi Kemosi, monga momwe Aisraeli anachitira manyazi ndi Beteli amene ankamukhutulira.
14 Hvorledes kunne I sige: Vi ere Helte og duelige Krigsmænd?
“Kodi munganene bwanji kuti, ‘Ife ndife asilikali. Ife ndife ngwazi, anthu amphamvu pa nkhondo?’
15 Moab er ødelagt, og man er steget op i dets Stæder, og dets udvalgte unge Mandskab er steget ned for at slagtes, siger Kongen, hvis Navn er Herre Zebaoth.
Owononga Mowabu ndi mizinda yake abwera ndipo ankhondo adzalowa mʼmidzi yake; anyamata ake okongola apita kukaphedwa,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
16 Moabs Undergang er nær for Haanden, og dets Ulykke skynder sig saare.
Kugwa kwa Mowabu kuli pafupi; masautso ake akubwera posachedwa.
17 Haver Medynk med det, alle I, som bo trindt omkring det! og alle I, som kende dets Navn, siger: Hvorledes er Magtens Stav, Herlighedens Spir sønderbrudt?
Mulireni kwambiri, inu nonse amene mwamuzungulira, inu nonse amene mumadziwa za kutchuka kwake; nenani kuti, “Taonani momwe yathyokera ndodo yamphamvu yaufumu ija, taonani momwe ndodo yaulemu yathyokera!”
18 Stig ned fra Herlighed, og sid i det tørstige Land, du Indbyggerske, Dibons Datter! thi Moabs Ødelægger er stegen op imod dig, han har ødelagt dine Befæstninger.
“Tsikani pa ulemerero wanu ndipo khalani pansi powuma, inu anthu okhala ku Diboni, pakuti wowononga Mowabu wabwera kudzamenyana nanu, wasakaza mizinda yanu yotetezedwa.
19 Stil dig ved Vejen og se dig om, du Aroers Indbyggerske! spørg ham, som er flygtet, og hende, som er undkommet; sig, hvad er der sket?
Inu amene mumakhala ku Aroeri, imani mʼmbali mwa msewu ndi kumaonerera. Funsani mwamuna amene akuthawa ndiponso mkazi amene wapulumuka, afunseni kuti, ‘Kodi chachitika nʼchiyani?’”
20 Moab er beskæmmet; thi det er knust, hyler og skriger; kundgører det ved Arnon, at Moab er ødelagt;
Iwo adzayankha kuti, “Mowabu wachititsidwa manyazi, pakuti wasakazika. Lirani mwachisoni ndipo fuwulani! Lengezani ku mtsinje wa Arinoni kuti Mowabu wawonongedwa.
21 og en Dom er kommet til Slettens Land, til Holon og til Jaza og over Mefaat
Chiweruzo chabwera ku mizinda ya ku mapiri, ndiyo Holoni, Yaza, Mefaati,
22 og over Dibon og over Nebo og over Beth-Diblathajm
Diboni, Nebo, Beti-Dibilataimu,
23 og over Kirjathajm og over Bethgamul og over Bethmeon
Kiriyataimu, Beti-Gamuli, Beti-Meoni,
24 og over Kirjot og over Bozra og over alle Stæder i Moabs Land, de fjerne og de nære.
Keriyoti ndi Bozira ndi mizinda yonse ya Mowabu, yakutali ndi yapafupi yomwe.
25 Moabs Horn er afhugget, og dets Arm er sønderbrudt, siger Herren,
Mphamvu za Mowabu zawonongeka; mkono wake wathyoka,” akutero Yehova.
26 Gører det drukkent! thi det ophøjede sig storlig imod Herren, saa at Moab maa plaske i sit Spy, og at ogsaa det maa blive til Latter.
“Muledzeretseni Mowabu, chifukwa anadzikuza powukira Yehova. Mulekeni Mowabu avivinizike mʼmasanzi ake; mulekeni akhale chinthu chomachiseka.
27 Thi mon Israel ikke var dig til Latter? mon det var grebet iblandt Tyve, at du, saa tit du talte om det, skulde ryste med Hovedet?
Kodi suja Israeli anali kwa iwe ngati chinthu chomachiseka? Kodi Israeli anapezeka pakati pa akuba kuti nthawi zonse poyankhula za iye, iwe uzimupukusira mutu momunyoza?
28 Forlader Stæderne og bor i Klippen, I Indbyggere i Moab! og værer som en Due, der bygger Rede ved Siden af Aabningen ned til en Kløft!
Inu amene mumakhala ku Mowabu, siyani mizinda yanu ndi kukakhala pakati pa matanthwe. Khalani ngati nkhunda imene imamanga chisa chake pa khomo la phanga.
29 Vi have hørt om Moabs Hovmod, det er saare hovmodigt, om dets Hoffærdighed og dets Hovmod og dets Stolthed og dets Hjertes Højhed.
“Tamva za kunyada kwa Mowabu, kunyada kwake nʼkwakukulu. Ndi wodzitama, wonyada ndi wodzitukumula. Ali ndi mtima wodzikweza.
30 Jeg kender, siger Herren, dets Overmod, men det er tomt; dets Pral er i Gerning tom.
Ine ndikuzidziwa ntchito zake, akutero Yehova. Ntchitozo ndi nʼzosapindulitsa kanthu.
31 Derfor maa jeg hyle over Moab og skrige over hele Moab; man maa sukke over Kir-Heres's Folk,
Nʼchifukwa chake ndidzamulira Mowabu, ine ndikulira chifukwa cha anthu onse a ku Mowabu, ndikubuwula chifukwa cha anthu a ku Kiri Heresi.
32 Jeg maa græde over dig, du Vintræ i Sibma! mere end jeg græder over Jaeser, dine Kviste gik hen over Havet, de naaede til Jaesers Hav; en Ødelægger er falden ind over din Frugthøst og over din Vinhøst.
Ndikukhetsa misozi chifukwa cha inu, kupambana momwe ndinalirira Yazeri. Inu anthu a ku Sibina muli ngati mipesa imene nthambi zake zatambalala mpaka ku Nyanja; zafika mpaka ku nyanja ya Yazeri. Wowononga wasakaza zipatso zake zachilimwe ndi mpesa.
33 Og Glæde og Fryd har forladt Frugthaven og Moabs Land; og jeg vil lade Vinen høre op i Persekarrene, ingen skal træde Persen med Frydesang, Frydesangen skal ikke mere være Frydesang.
Chimwemwe ndi chisangalalo zatha ku minda ya zipatso ya ku Mowabu. Ndaletsa kuchucha kwa vinyo mopsinyira mphesa; palibe amene akufuwula mokondwa akamapsinya mphesa. Ngakhale kufuwula kulipo, koma sikufuwula kwa chimwemwe.
34 Af Skriget i Hesbon lade de Lyden høres, indtil Eleale, indtil Jahaz, fra Zoar indtil Horonajm, Eglath Selisia; thi ogsaa Nimjims Vande skulle blive til Ørk.
“A ku Hesiboni ndi Eleali akulira ndipo mfuwu wawo ukumveka mpaka ku Yahazi, kuchokera ku Zowari mpaka ku Horonaimu ndi ku Egilati Selisiya. Ngakhale madzi a ku Nimurimu aphwa.
35 Og jeg vil gøre, siger Herren, at Moab ikke mere skal have nogen, som drager op paa Højen og gør Røgoffer for sine Guder.
Ndidzawaletsa anthu a ku Mowabu kupereka nsembe mʼmalo awo opembedzera ndi kufukiza lubani kwa milungu yawo,” akutero Yehova.
36 Derfor bruser mit Hjerte som Fløjter over Moab, og mit Hjerte bruser over Mændene i Kir-Heres som Fløjter, derfor gaar Levningen, som det havde forhvervet, til Grunde.
“Nʼchifukwa chake mtima wanga ukulirira Mowabu ngati chitoliro. Mtima wanga ukulirira anthu a ku Kiri Heresi ngati chitoliro chifukwa chuma chimene anachipata chatha.
37 Thi hvert Hoved er skaldet, og hvert Skæg er afskaaret; der er Indsnit paa alle Hænder og Sæk om Lænderne.
Aliyense wameta mutu wake ndi ndevu zake; manja a munthu aliyense ndi ochekacheka, ndipo munthu aliyense wavala chiguduli mʼchiwuno mwake.
38 Paa alle Tage i Moab og paa dets Gader er der kun Klage; thi jeg har sønderbrudt Moab som et Kar, man ikke har Lyst til, siger Herren.
Pa madenga onse a ku Mowabu ndiponso mʼmisewu yake anthu akungolira, pakuti ndaphwanya Mowabu ngati mtsuko wopanda ntchito,” akutero Yehova.
39 Hvorledes er det dog knust I Hyler! hvorledes vender Moab dog Nakken til! det er beskæmmet; og Moab skal blive til Latter og til Forfærdelse for alle trindt omkring det.
“Taonani mmene waphwanyikira! Tamvani momwe akulirira! Taonani momwe Mowabu wachititsidwira manyazi. Mowabu wasanduka chinthu chonyozeka, chinthu chochititsa mantha kwa onse amene amuzungulira.”
40 Thi saa siger Hejren: Se, han kommer flyvende som Ørnen og udbreder sine Vinger imod Moab.
Yehova akuti, “Mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkugwera pa Mowabu ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake.
41 Stæderne erobres, og Fæstningerne indtages; og de vældiges Hjerte i Moab skal være paa denne Dag som en beængstet Kvindes Hjerte.
Mizinda idzagwidwa ndipo malinga adzalandidwa. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Mowabu idzakhala ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
42 Og Moab skal ødelægges, saa at det ikke mere er et Folk, thi det har ophøjet sig storlig imod Herren.
Mowabu sudzakhala mtundu wa anthu chifukwa unadzikuza powukira Yehova.
43 Forfærdelse og Grav og Snare over dig, du, som bor i Moab! siger Herren,
Zoopsa, dzenje ndi msampha zikudikira inu anthu a ku Mowabu,” akutero Yehova.
44 Den, som flyr for Forfærdelsen, skal falde i Graven, og den, som kommer op af Graven, skal fanges i Snaren; thi jeg Vil lade komme til det, til Moab, dets Hjemsøgelses Aar, siger Herren,
“Aliyense wothawa zoopsa adzagwera mʼdzenje, aliyense wotuluka mʼdzenje adzakodwa mu msampha. Ndigwetsa zimenezi pa Mowabu pa nthawi ya chilango chake,” akutero Yehova.
45 I Hesbons Skygge stille sig de, der fly som kraftesløse; thi en Ild udgaar fra Hesbon og en Lue fra Sihon, og den skal fortære Moabs Hjørne og Issen af Bulderets Srør, ner.
“Anthu othawa nkhondo ayima pa mthunzi wa Hesiboni chifukwa chotopa. Koma moto wayaka kuchokera ku Hesiboni, malawi a moto abuka kuchokera ku nyumba ya mfumu Sihoni. Motowo ukuwononga mapiri a ku Mowabu, dziko la anthu onyada.
46 Ve dig, Moab! Kamos's Folk er fortabt; thi dine Sønner ere tagne og førte i Fangenskab og dine Døtre i Fangenskab.
Tsoka kwa iwe Mowabu! Anthu opembedza Kemosi awonongeka. Ana ako aamuna ndi aakazi atengedwa ukapolo.
47 Men jeg vil omvende Moabs Fangenskab i de sidste Dage, siger Herren. — Hertil gaar Dommen over Moab.
“Komabe masiku akutsogolo ndidzabwezeranso Mowabu chuma chake,” akutero Yehova. Chiweruzo cha Mowabu chathera pamenepa.